< Genèse 43 >
1 Or, la famine était fort grande dans le pays.
Njala inakula kwambiri mʼdzikomo.
2 Et quand ils eurent achevé de manger le blé qu'ils avaient apporté d'Égypte, leur père leur dit: Retournez nous acheter un peu de vivres.
Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”
3 Et Juda lui répondit: Cet homme nous a expressément protesté et dit: Vous ne verrez point ma face, que votre frère ne soit avec vous.
Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’
4 Si tu envoies notre frère avec nous, nous descendrons en Égypte, et nous t'achèterons des vivres.
Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya.
5 Mais si tu ne l'envoies pas, nous n'y descendrons point; car cet homme nous a dit: Vous ne verrez point ma face, que votre frère ne soit avec vous.
Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’”
6 Et Israël dit: Pourquoi m'avez-vous fait ce tort, de déclarer à cet homme que vous aviez encore un frère?
Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”
7 Et ils répondirent: Cet homme s'est enquis avec soin de nous et de notre parenté, en disant: Votre père vit-il encore? Avez-vous encore un frère? Et nous le lui avons déclaré, d'après ces questions. Pouvions-nous savoir qu'il dirait: Faites descendre votre frère?
Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”
8 Et Juda dit à Israël, son père: Envoie l'enfant avec moi, et nous nous lèverons, et partirons; et nous vivrons et ne mourrons point, ni nous, ni toi, ni nos petits enfants.
Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo.
9 Je réponds de lui; tu me le redemanderas. Si je ne te le ramène et ne le présente devant ta face, je serai coupable envers toi à toujours.
Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse.
10 Car si nous n'avions pas différé, nous serions maintenant deux fois de retour.
Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”
11 Alors Israël, leur père, leur dit: S'il en est ainsi, faites donc ceci: Prenez dans vos bagages des produits les plus renommés du pays, et portez à cet homme un présent, un peu de baume et un peu de miel, des aromates et de la myrrhe, des pistaches et des amandes;
Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
12 Et prenez d'autre argent dans vos mains, et reportez dans vos mains l'argent qui a été remis à l'entrée de vos sacs. Peut-être est-ce une erreur.
Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa.
13 Prenez aussi votre frère, et levez-vous, retournez vers cet homme.
Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga.
14 Et que le Dieu Tout-Puissant vous fasse trouver grâce devant cet homme, qu'il vous relâche votre autre frère, et Benjamin! Et s'il faut que je sois privé d'enfants, que j'en sois privé!
Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”
15 Ils prirent donc le présent, et le double d'argent dans leurs mains, et Benjamin. Puis, se levant, ils descendirent en Égypte, et se présentèrent devant Joseph.
Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe.
16 Et Joseph vit Benjamin avec eux, et il dit à l'intendant de sa maison: Mène ces hommes à la maison, tue quelque bête et apprête-la; car ils mangeront avec moi à midi.
Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”
17 Et l'homme fit comme Joseph avait dit, et il amena ces hommes à la maison de Joseph.
Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe.
18 Et ces hommes eurent peur de ce qu'on les menait à la maison de Joseph; et ils dirent: C'est à cause de l'argent qui fut remis dans nos sacs la première fois, qu'on nous emmène; c'est pour se jeter, se précipiter sur nous et nous prendre pour esclaves, et se saisir de nos ânes.
Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”
19 Alors ils s'approchèrent de l'intendant de la maison de Joseph, et lui parlèrent à la porte de la maison, et dirent:
Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti,
20 Pardon, mon seigneur! nous sommes descendus une première fois pour acheter des vivres;
“Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya
21 Et lorsque nous arrivâmes à l'hôtellerie, et que nous ouvrîmes nos sacs, voici, l'argent de chacun était à l'entrée de son sac, notre argent selon son poids; et nous l'avons rapporté en nos mains.
koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo.
22 Et nous avons apporté d'autre argent en nos mains, pour acheter des vivres; nous ne savons qui avait remis notre argent dans nos sacs.
Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”
23 Et il dit: Tout va bien pour vous! Ne craignez point: C'est votre Dieu, le Dieu de votre père qui vous a donné un trésor dans vos sacs; votre argent m'est parvenu. Et il leur amena Siméon.
Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.
24 Et cet homme les fit entrer dans la maison de Joseph; il leur donna de l'eau, et ils lavèrent leurs pieds; il donna aussi du fourrage à leurs ânes.
Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo.
25 Et ils préparèrent le présent, en attendant que Joseph vînt à midi; car ils avaient appris qu'ils mangeraient là le pain.
Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.
26 Joseph revint à la maison. Alors ils lui offrirent dans la maison le présent qu'ils avaient en leurs mains; et ils se prosternèrent en terre devant lui.
Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi.
27 Et il leur demanda comment ils se portaient, et il leur dit: Votre vieux père, dont vous m'avez parlé, se porte-t-il bien? Vit-il encore?
Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”
28 Et ils répondirent: Ton serviteur notre père se porte bien; il vit encore. Et ils s'inclinèrent, et se prosternèrent.
Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.
29 Et, levant les yeux, il vit Benjamin son frère, fils de sa mère, et dit: Est-ce là votre jeune frère, dont vous m'avez parlé? Et il lui dit: Dieu te fasse miséricorde, mon fils!
Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.”
30 Et Joseph se hâta, car ses entrailles étaient émues pour son frère, et il chercha un lieu pour pleurer; et il entra dans la chambre intérieure et y pleura.
Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.
31 Puis il se lava le visage et sortit; et, se faisant violence, il dit: Servez le pain.
Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.
32 Et on le servit à part, et eux à part; et les Égyptiens qui mangeaient avec lui furent aussi servis à part, parce que les Égyptiens ne peuvent manger le pain avec les Hébreux; car c'est une abomination pour les Égyptiens.
Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri.
33 Ils s'assirent donc en sa présence, l'aîné selon son droit d'aînesse, et le plus jeune selon son âge. Et ces hommes se regardaient l'un l'autre avec étonnement.
Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa.
34 Et il leur fit porter des mets de devant lui; mais la portion de Benjamin était cinq fois plus grosse que les portions de tous les autres; et ils burent et firent bonne chère avec lui.
Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.