< Ézéchiel 34 >

1 La parole de l'Éternel me fut adressée en ces termes:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Fils de l'homme, prophétise contre les pasteurs d'Israël; prophétise et dis-leur, aux pasteurs: Ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Malheur aux pasteurs d'Israël, qui ne paissaient qu'eux-mêmes!
“Iwe mwana wa munthu, yankhula mawu oyimba mlandu abusa a Israeli. Lengeza ndipo uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Tsoka kwa abusa a Israeli amene mumangodzisamala nokha! Kodi abusa sayenera kusamalira nkhosa?
3 N'est-ce pas le troupeau que les pasteurs doivent paître? Vous mangiez la graisse, et vous vous revêtiez de la laine; vous tuiez ce qui était gras, vous ne paissiez point le troupeau!
Mumadya chambiko, mumadziveka zovala zaubweya, ndi kupha nyama zonenepa, koma simusamalira nkhosazo.
4 Vous n'avez pas fortifié les faibles, vous n'avez pas guéri les malades, vous n'avez point bandé les blessées; vous n'avez pas ramené les égarées, et n'avez pas cherché les perdues; mais vous les avez dominées avec dureté et rigueur.
Simunalimbitse nkhosa zofowoka, kapena kuchiritsa zodwala, kapena kumanga mabala a nkhosa zopweteka. Simunabweze zosochera kapena kufunafuna zotayika. Munaziweta mozunza ndi mwankhanza.
5 Faute de pasteurs, elles se sont dispersées; elles ont été exposées à devenir la proie de toutes les bêtes des champs; elles se sont dispersées.
Kotero zinabalalika chifukwa zinalibe mʼbusa, ndipo pamene zinabalalika zinakhala chakudya cha zirombo zonse zakuthengo.
6 Mes brebis sont errantes sur toutes les montagnes et sur toutes les collines élevées; mes brebis sont dispersées sur toute la surface de la terre; personne ne s'en inquiète, personne ne s'en informe.
Nkhosa zanga zinayendayenda mʼmapiri onse ndi mʼzitunda zonse zazitali. Zinabalalika pa dziko lonse lapansi, ndipo palibe amene anazilondola kapena kuzifunafuna.
7 C'est pourquoi, pasteurs, écoutez la parole de l'Éternel:
“‘Choncho Inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
8 Je suis vivant! dit le Seigneur, l'Éternel, parce que mes brebis sont livrées au pillage, parce que, faute de pasteurs, elles ont été exposées à devenir la proie de toutes les bêtes des champs, que mes pasteurs n'ont pris nul souci de mes brebis, mais se paissaient eux-mêmes au lieu de faire paître mes brebis;
Pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Wamphamvuzonse, ndithu, nkhosa zanga zinajiwa ndi zirombo zakuthengo, zinasanduka chakudya cha zirombo chifukwa panalibe abusa. Abusa anga sanafunefune nkhosa zanga. Iwo ankangosamala za iwo okha mʼmalo mosamala nkhosa zanga.
9 A cause de cela, pasteurs, écoutez la parole de l'Éternel:
Chifukwa chake, inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
10 Ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Voici, j'en veux à ces pasteurs, et je redemanderai mes brebis de leurs mains; je ne les laisserai plus paître mes brebis, et ils ne se paîtront plus eux-mêmes; mais je délivrerai mes brebis de leur bouche, afin qu'elles ne leur servent plus de pâture.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndayipidwa nanu, inu abusa. Ndidzakulandani nkhosa zanga ndipo simudzazidyetsanso. Ndidzakuchotsani pa ntchito ya ubusa kuti musamangodzidyetsa nokha. Ndidzalanditsa nkhosa zanga kukamwa kwanu ndipo simudzazidyanso.
11 Car ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Voici, je redemanderai mes brebis, et j'en ferai la revue.
“‘Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, mwini wakene ndidzazifunafuna nkhosa zanga ndi kuzisamalira.
12 Comme un pasteur inspecte son troupeau, lorsqu'il est au milieu de ses brebis éparses, ainsi je ferai la revue de mes brebis: je les recueillerai de tous les lieux où elles ont été dispersées, au jour des nuages et de l'obscurité.
Monga mʼbusa amanka nafunafuna nkhosa zake pamene zina zabalalikira kutali, moteronso Ine ndidzafunafuna nkhosa zanga. Ndidzazipulumutsa kuchoka kumalo onse kumene zinabalalikira pa nthawi yankhungu ndi mdima.
13 Je les retirerai d'entre les peuples, je les rassemblerai des divers pays, je les ramènerai dans leur pays, et les ferai paître sur les montagnes d'Israël, dans les ravins et dans tous les lieux habités du pays.
Ndidzazitulutsa pakati pa mitundu ya anthu ndi kuzisonkhanitsa kuchokera ku mayiko ena, ndipo ndidzazibwezera ku dziko lawo. Ndidzaziwetera ku mapiri a Israeli, mʼmbali mwa mitsinje ndi kumalo kumene kumakhala anthu.
14 Je les ferai paître dans de bons pâturages, et leur parc sera dans les hautes montagnes d'Israël; elles y reposeront dans un bon parc, et paîtront dans de gras pâturages sur les montagnes d'Israël.
Ndidzaziwetera kumalo a msipu wabwino. Mapiri okwera a Israeli adzakhala malo azidyetserako. Kumeneko zidzapumula ku abusa abwino a msipu ndipo zizidzadyadi msipu wonenepetsa pa mapiri a Israeli.
15 Car moi-même je paîtrai mes brebis et les ferai reposer, dit le Seigneur, l'Éternel.
Ine mwini wake ndidzaziweta nkhosa zanga ndi kuzilola kuti zipumule. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
16 Je chercherai celle qui était perdue, je ramènerai l'égarée, je panserai la blessée et fortifierai la malade; mais je détruirai les grasses et les vigoureuses; car je les paîtrai avec justice.
Ndidzafunafuna zotayika ndi kubweza zosochera. Ndidzamanga mabala a zopweteka ndi kulimbikitsa zofowoka. Koma zonenepa ndi zamphamvu ndidzaziwononga. Ndidzaweta nkhosazo mwachilungamo.
17 Et vous, mes brebis, ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Voici, je veux juger entre brebis et brebis, entre béliers et boucs.
“‘Kunena za inu, nkhosa zanga, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa, pakati pa nkhosa zazimuna ndi mbuzi zazimuna.
18 Est-ce trop peu pour vous de paître dans un bon pâturage, que vous fouliez de vos pieds le reste de votre pâturage; de boire de belles eaux, que vous troubliez de vos pieds ce qui reste?
Kodi sikukukwanirani kudya msipu wabwino kuti muzichita kuponderezanso msipu umene simunadyewo? Kodi simukhutira ndi kumwa madzi abwino kuti muzinka mudetsanso madzi otsalawo ndi mapazi anu?
19 Et mes brebis doivent paître ce que foulent vos pieds, et ce que vous troublez de vos pieds!
Kodi nkhosa zanga zidye zimene mwazipondaponda ndi kumwa madzi amene mwawadetsa ndi mapazi anu?
20 C'est pourquoi, ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Voici, je veux moi-même juger entre la brebis grasse et la brebis maigre.
“‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Taonani, Ine mwini wake ndidzaweruza pakati pa nkhosa zonenepa ndi nkhosa zowonda.
21 Parce que vous avez poussé, du côté et de l'épaule, et heurté de vos cornes toutes celles qui sont languissantes, jusqu'à ce que vous les ayez chassées dehors,
Popeza zofowoka mumaziwomba ndi kuzikankhira kumbali, ndipo mumazigunda ndi nyanga zanu nʼkuzimwazira kutali,
22 Je sauverai mon troupeau, afin qu'il ne soit plus exposé au pillage, et je jugerai entre brebis et brebis.
tsono Ine ndidzapulumutsa nkhosa zanga, ndipo sindidzalolanso kuti zijiwe. Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ina ndi nkhosa inanso.
23 J'établirai sur elles un seul pasteur qui les paîtra: David, mon serviteur; il les paîtra, et il sera lui-même leur pasteur;
Ndidzaziyikira mʼbusa mmodzi, mtumiki wanga Davide. Iyeyo ndiye azidzazisamala. Adzakhala mʼbusa wawo.
24 Et moi l'Éternel, je serai leur Dieu, et David, mon serviteur, sera prince au milieu d'elles. Moi, l'Éternel, j'ai parlé.
Ine Yehova ndidzakhala Mulungu wake ndipo mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu pakati pa nkhosazo. Ine Yehova ndayankhula.
25 Je traiterai avec elles une alliance de paix, et j'exterminerai du pays les bêtes sauvages; et mes brebis habiteront en sécurité au désert, et dormiront dans les bois.
“‘Ndidzapangana nazo pangano la mtendere. Ndidzachotsa mʼdzikomo zirombo zolusa. Choncho nkhosa zanga zidzakhala mu mtendere mu chipululu ngakhalenso mʼthengo.
26 Je les comblerai de bénédictions, elles et les environs de mon coteau; en sa saison je ferai tomber la pluie: ce seront des pluies de bénédiction.
Ndidzakhazika anthu anga pafupi ndi phiri langa loyera ndipo ndidzawadalitsa. Ndidzawagwetsera mvula pa nthawi yake ndipo idzakhala mvula ya madalitso.
27 Les arbres des champs produiront leur fruit, et la terre rapportera son revenu; elles seront en sécurité dans leur pays, et elles sauront que je suis l'Éternel, quand je briserai le bois de leur joug, et que je les délivrerai des mains de leurs oppresseurs.
Mitengo ya mʼminda idzabereka zipatso zake, ndipo nthaka idzakhala ndi zokolola zake. Anthu adzakhala mwamtendere mʼdziko lawo. Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzathyola magoli awo ndi kuwapulumutsa kuchoka mʼmanja mwa amene anawagwira ukapolo.
28 Elles ne seront plus la proie des nations; les bêtes de la terre ne les dévoreront plus; elles demeureront en sécurité, sans que personne les épouvante.
Anthu amitundu ina sadzawafunkhanso ndipo sadzadyedwa ndi zirombo zakuthengo. Adzakhala mwamtendere ndipo palibe amene adzawaopseze.
29 Je leur susciterai une plantation de renom; elles ne périront plus de faim dans le pays, et ne porteront plus l'opprobre des nations.
Ndidzawapatsa zokolola zochuluka motero kuti sadzavutikanso ndi njala. Anthu a mitundu ina sadzawanyozanso.
30 Et ils sauront que moi, l'Éternel leur Dieu, suis avec elles, et qu'elles, la maison d'Israël, sont mon peuple, dit le Seigneur, l'Éternel.
Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wawo ndili nawo pamodzi, ndipo kuti iwo, Aisraeli, ndi anthu anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
31 Vous, mes brebis, les brebis de mon pâturage, vous êtes des hommes; je suis votre Dieu, dit le Seigneur, l'Éternel.
Inu ndinu nkhosa zanga, nkhosa zimene ndimazidyetsa. Ine ndine Mulungu wanu. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.’”

< Ézéchiel 34 >