< Ézéchiel 23 >

1 La parole de l'Éternel me fut adressée en ces termes:
Yehova anandiyankhula nati:
2 Fils de l'homme, il y avait deux femmes, filles d'une même mère.
“Iwe mwana wa munthu, panali atsikana awiri ana a mayi mmodzi.
3 Elles se prostituèrent en Égypte; elles se prostituèrent dans leur jeunesse; là leurs mamelles furent pressées, leur sein virginal y fut flétri.
Iwo ankachita za chiwerewere ku Igupto. Za chiwerewerezo anayamba ali achichepere. Kumeneko anthu ankangowasisita pa chifuwa ndi kuwagwiragwira mawere awo aja.
4 L'aînée se nommait Ohola et sa sœur Oholiba. Elles m'appartenaient, et enfantèrent des fils et des filles. Celle qui s'appelle Ohola, c'est Samarie, et Oholiba, c'est Jérusalem.
Wamkulu dzina lake anali Ohola, ndipo mngʼono wakeyo anali Oholiba. Ine ndinawakwatira ndipo anabereka ana aamuna ndi ana aakazi. Ohola ndiye Samariya, ndipo Yerusalemu ndiye Oholiba.
5 Ohola me fut infidèle, et s'éprit de ses amants, les Assyriens, ses voisins,
“Ohola anachita zachiwerewere ngakhale anali mkazi wanga; ndipo iye anakangamira abwenzi ake a ku Asiriya.
6 Vêtus de pourpre, gouverneurs et seigneurs, tous beaux jeunes hommes, des cavaliers montés sur des coursiers.
Amenewo anali asilikali ovala zibakuwa zamlangali, abwanamkubwa ndiponso atsogoleri a nkhondo. Onsewo anali anyamata osiririka ndipo ankakwera pa akavalo.
7 Elle commit adultère avec eux tous, l'élite des enfants d'Assur; elle se souilla avec tous ceux dont elle s'était éprise, et avec toutes leurs idoles.
Ohola anachita zachiwerewere ndi onsewa, anthu otchuka a ku Asiriya. Iye anadziyipitsa ndi mafano a munthu aliyense amene anagona naye.
8 Elle n'a pas renoncé à ses prostitutions d'Égypte; car ils avaient déshonoré sa jeunesse, flétri son sein virginal, et répandu sur elle la souillure.
Iye sanaleke za chiwerewere zimene anaziphunzira ku Igupto. Paja akanali mtsikana anyamata ankagona naye. Iwo ankamusisita mawere akanali anthete nachita naye zachiwerewere.
9 C'est pourquoi je l'ai livrée aux mains de ses amants, aux mains des enfants d'Assur, dont elle s'était éprise.
“Nʼchifukwa chake Ine ndinamupereka kwa achikondi ake, Asiriya, amene iye ankawalakalaka.
10 Ils ont découvert sa nudité; ils ont enlevé ses fils et ses filles, et l'ont fait périr elle-même par l'épée. Elle est devenue fameuse parmi les femmes, après les jugements exercés sur elle.
Iwowa anamuvula, namulanda ana ake aamuna ndi aakazi ndipo anamupha ndi lupanga. Ndipo atalangidwa choncho, iye anasanduka chinthu chonyozeka pakati pa akazi.
11 Sa sœur Oholiba avait vu cela; néanmoins elle fut plus déréglée encore dans sa passion, et dans ses prostitutions elle a fait pire que sa sœur.
“Mphwake Oholiba anaona zimenezi natengerako. Koma iye anachita zachiwerewere kuposa mkulu wake.
12 Elle s'éprit des enfants d'Assur, gouverneurs et seigneurs, ses voisins, magnifiquement vêtus, cavaliers montés sur des coursiers, tous beaux jeunes hommes.
Iyenso anakangamira Asiriya, abwanamkubwa, olamulira asilikali, ankhondo ovala zovala zonse za nkhondo ndi okwera pa akavalo. Onsewa anali anyamata osiririka.
13 Je vis qu'elle s'était souillée, et que toutes les deux suivaient la même voie.
Ndinaona kuti iyenso anadziyipitsa; ndipo onse awiriwo anatsata njira imodzi.
14 Mais elle est allée plus loin encore dans ses prostitutions; car elle vit des peintures d'hommes sur la muraille, des images de Caldéens peints en vermillon.
“Koma Oholiba uja anachita chigololo kopitirira mkulu wake. Iye anaona zithunzi za amuna pa khoma, zithunzi za Ababuloni zolembedwa ndi inki yofiira,
15 Ils portaient des ceintures autour de leurs reins, et sur leurs têtes des rubans flottants de diverses couleurs; ils avaient tous l'aspect de nobles guerriers, portraits des enfants de Babylone en Caldée, leur pays natal.
atamanga malamba mʼchiwuno mwawo ndi kuvala nduwira pa mitu yawo. Onse amaoneka ngati atsogoleri a magaleta a Ababuloni, mbadwa za ku Kaldeya.
16 Elle s'éprit d'eux, au premier regard de ses yeux, et leur envoya des messagers en Caldée.
Oholiba atangowaona, anawalakalaka ndipo anatuma amithenga ku Kaldeya kukawayitana.
17 Et les enfants de Babylone sont venus vers elle, pour partager la couche des amours, et ils l'ont souillée par leurs adultères; elle aussi s'est souillée avec eux, puis son cœur s'est détaché d'eux.
Ndipo Ababuloni anabwera nʼkudzagona naye. Choncho mwa chilakolako chawo anamuyipitsa. Koma atamuyipitsa choncho, iye ananyansidwa nawo.
18 Elle a mis à nu ses adultères; elle a découvert sa nudité, et mon cœur s'est détaché d'elle, comme il s'était détaché de sa sœur;
Iye atachita chiwerewere chake poyera ndi kuonetsa umaliseche wake, Ine ndinamuchokera monyansidwa monga mmene ndinachitira ndi mʼbale wake.
19 Car elle a multiplié ses prostitutions, en songeant aux jours de sa jeunesse, où elle s'était prostituée au pays d'Égypte.
Koma anachitabe zachiwerewere osalekeza. Ankakumbukira masiku a ubwana wake pamene ankachita za chiwerewere mʼdziko la Igupto.
20 Elle s'est éprise de ces débauchés dont la chair est comme la chair des ânes, et l'ardeur pareille à celle des chevaux.
Kumeneko iye ankalakalaka zibwenzi zake, amene ziwalo zawo zinali ngati za abulu ndipo kutentha kwawo kunali ngati kwa akavalo.
21 Tu es retournée aux crimes de ta jeunesse, alors que les Égyptiens pressaient tes mamelles, à cause de ton sein virginal.
Motero, iwe Oholiba unafuna kuchitanso zadama monga unkachitira ku Igupto pamene unali mtsikana. Nthawi imene ija ankakusisita pa chifuwa ndi kugwiragwira mawere ako osagwa aja.
22 C'est pourquoi, Oholiba, ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Voici, j'excite contre toi tes amants dont ton cœur s'est détaché; je les amène de toute part contre toi:
“Tsono iwe Oholiba, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzakudzutsira zibwenzi zako zimene unkanyansidwa nazo zija kuti zilimbane nawe. Ndidzaziyitana kuti zibwere kuchokera mbali zonse.
23 Les enfants de Babylone et tous les Caldéens, chefs, princes et nobles, et tous les enfants d'Assur avec eux, de beaux jeunes hommes, tous gouverneurs et seigneurs, guerriers fameux, tous montés sur des coursiers.
Ndidzayitana anthu a ku Babuloni ndi Akaldeya onse, anthu a ku Pekodi, Sowa ndi Kowa pamodzi ndi Asiriya onse. Onsewa ndi amuna osiririka, abwanamkubwa, atsogoleri a ankhondo, oyenda pa magaleta, anthu a maudindo akuluakulu. Onsewa ndi okwera akavalo.
24 Ils viennent contre toi avec des armes, des chars, de grands trains et une foule de peuples; ils t'environnent de toute part avec des pavois, des boucliers, des casques; je remets entre leurs mains le jugement; ils te jugeront à leur façon.
Iwo adzabwera kudzalimbana nawe ndi zida za nkhondo, magaleta ndi ngolo, pamodzi ndi anthu ambiri. Adzakuzinga mbali zonse atavala zishango zankhondo ndi zipewa zankhondo. Ndidzakupereka kwa iwo kuti akulange ndipo adzakulanga monga momwe adzafunire.
25 Je donne libre cours à l'ardeur de ma jalousie contre toi, et ils te traiteront avec fureur; ils te couperont le nez et les oreilles; et ce qui restera de toi périra par l'épée; ils enlèveront tes fils et tes filles, et ce qui restera de toi sera dévoré par le feu.
Ndidzaonetsa mkwiyo wanga pa iwe ndipo iwo adzakulanga iwe mwankhanza. Adzadula mphuno zanu ndi makutu anu, ndipo amene adzatsalira mwa iwe adzaphedwa ndi lupanga. Iwo adzakulanda ana ako aamuna ndi aakazi ndipo amene adzatsalira adzaphedwa ndi moto.
26 Ils te dépouilleront de tes vêtements, et enlèveront les ornements dont tu te pares.
Adzakuvulaninso zovala zanu ndikukulandani zodzikongoletsera zanu zamtengowapatali.
27 Je mettrai un terme à tes infamies et à tes prostitutions du pays d'Égypte; tu ne lèveras plus les yeux vers eux, et tu ne te souviendras plus de l'Égypte.
Motero ndidzathetsa zonyansa zako ndi zachigololo zomwe unaziyamba ku Igupto. Choncho sudzalakalaka za ku Igupto kapena kuzikumbukiranso.
28 Car ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Voici, je te livre aux mains de ceux que tu hais, aux mains de ceux dont ton cœur s'est détaché.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikukupereka mʼmanja mwa amene amadana nawe, kwa iwo amene unawafulatira moyipidwa nawo.
29 Ils te traiteront avec haine, ils t'enlèveront tout le fruit de tes labeurs; ils te laisseront nue, entièrement nue, et aussi sera mise à découvert la honte de tes impudicités, de ton crime et de tes prostitutions.
Adzachita nawe mwachidani. Adzakulanda zonse zimene unagwirira ntchito. Adzakusiya wamaliseche ndiponso wausiwa. Kuyipa kwa makhalidwe ako achiwerewere kudzakhala pammbalambanda. Zonyansa zako ndi chiwerewere chako,
30 On te fera ces choses, parce que tu t'es prostituée auprès des nations, que tu t'es souillée avec leurs idoles.
zabweretsa izi pa iwe chifukwa unachita zonyansa ndi anthu a mitundu ndi kudziyipitsa ndi mafano awo.
31 Tu as marché dans la voie de ta sœur, c'est pourquoi je mettrai sa coupe dans ta main.
Unatsata zochita za mkulu wako; choncho Ine ndidzayika chikho cha chilango chake mʼdzanja lako.
32 Ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Tu boiras la coupe de ta sœur, coupe profonde et large; tu deviendras un objet de dérision et de moquerie; grande est sa capacité.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Udzamwera chikho cha mkulu wako, chikho chachikulu ndi chakuya; anthu adzakuseka ndi kukunyoza, pakuti chikhocho ndi chodzaza kwambiri.
33 Tu seras remplie d'ivresse et de douleur; c'est une coupe de désolation et de stupeur que la coupe de ta sœur Samarie.
Udzaledzera ndipo mtima wako udzadzaza ndi chisoni. Chimenechi ndi chikho chachiwonongeko ndi chipasupasu, chikho cha mkulu wako Samariya.
34 Tu la boiras, tu la videras, tu en rongeras les morceaux, et tu te déchireras le sein. Car j'ai parlé, dit le Seigneur, l'Éternel.
Udzamwa chikhocho mpaka kugugudiza. Tsono udzaphwanyaphwanya chikhocho ndipo udzangʼamba mawere ako ndi zigoba zake. Ine ndayankhula, akutero Ambuye Yehova.
35 C'est pourquoi ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Parce que tu m'as mis en oubli, et que tu m'as rejeté derrière ton dos, porte donc aussi la peine de tes infamies et de tes adultères.
“Chifukwa chake, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza wandiyiwala Ine ndi kundifulatira, chomwecho uyenera kulangidwa chifukwa cha zonyansa zako ndi chiwerewere chako.”
36 Et l'Éternel me dit: Fils de l'homme, ne jugeras-tu pas Ohola. et Oholiba? Mets sous leurs yeux leurs abominations.
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi udzaweruza Ohola ndi Oholiba? Tsono uwayimbe mlandu chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
37 Elles ont commis adultère, et il y a du sang à leurs mains; elles ont commis adultère avec leurs idoles; et même, les enfants qu'elles ont enfantés, elles les ont fait passer par le feu pour être dévorés!
Iwo achita chigololo ndipo anapha anthu. Anachita chigololo popembedza mafano awo. Ngakhale ana amene anandiberekera Ine anawapereka kwa mafanowo ngati chakudya chawo.
38 Voici ce qu'elles m'ont encore fait: en un même jour, elles ont souillé mon sanctuaire et profané mes sabbats;
Anachitanso izi: Iwo anayipitsa malo anga opatulika ndi kudetsa masabata anga.
39 Après avoir immolé leurs enfants à leurs idoles, elles sont entrées le même jour dans mon sanctuaire pour le profaner! Voilà ce qu'elles ont fait au milieu de ma maison.
Atapereka ana awo kwa mafano, tsiku lomwelo anakalowanso mʼNyumba yanga yopatulika ndi kuyipitsamo. Izi ndi zimene anachita mʼNyumba mwanga.
40 Bien plus, elles ont fait chercher des hommes venant d'un pays éloigné; elles leur ont envoyé des messagers, et voici, ils sont venus. Pour eux tu t'es lavée, tu as fardé ton visage, et tu t'es parée d'ornements.
“Iwo anatuma amithenga kukayitana amuna a ku mayiko akutali. Anthuwo atabwera, abale awiri aja anasambasamba, kudzola utoto wodzikometsera kumaso, kenaka ndi kuvala zovala zamakaka.
41 Tu t'es assise sur un lit magnifique, devant lequel était dressée une table, et où tu as placé mon parfum et mon huile de senteur.
Anakhala pa bedi lokongola ndipo patsogolo pawo panali tebulo pamene munayikapo lubani ndi mafuta. Zonse zowapatsa Ine.
42 Là on entendait le bruit d'une multitude joyeuse; et parmi cette foule d'hommes, on a fait venir des Sabéens du désert, qui ont mis des bracelets aux mains des deux sœurs, et de magnifiques couronnes sur leur tête.
“Mfuwu wa chigulu cha anthu unamveka. Anthu oledzera ochokera ku chipululu anabwera pamodzi ndi anthu wamba ndipo anaveka akaziwo zibangiri kumanja ndi zipewa zaufumu zokongola ku mutu.
43 Et je dis, touchant celle qui avait vieilli dans l'adultère: Continueront-ils maintenant leurs impudicités avec elle, et elle avec eux?
Ndipo ine ndinati za mkazi wotheratu ndi chigololoyo, ‘Tsono asiyeni kuti achite naye monga wachiwerewere, pakuti ichi ndi chimene iye ali basi.’
44 Et l'on est venu chez elle, comme l'on va chez une prostituée; c'est ainsi qu'on est allé vers Ohola et Oholiba, ces femmes coupables.
Tsono anapita kwa iwo monga mmene anthu amapitira kwa mkazi wadama. Momwemo anapita kwa Ohola ndi kwa Oholiba kukachita nawo zadama.
45 Mais des hommes justes les jugeront comme on juge des femmes adultères, comme on juge celles qui répandent le sang, car elles sont adultères et il y a du sang à leurs mains.
Koma anthu olungama adzawazenga anthuwa mlandu wa chigololo ndi wa kupha anthu. Ndi iwodi anthu achigololo ndiponso mʼmanja mwawo muli magazi.
46 C'est pourquoi, ainsi a dit le Seigneur, l'Éternel: Je ferai monter contre elles une multitude, et les livrerai à l'insulte et au pillage.
“Ambuye Yehova akuti: Itanitsani chigulu cha anthu kuti chidzawalange ndi kulanda chuma chawo.
47 Et cette multitude les assommera à coups de pierres, et les taillera en pièces par l'épée; ils égorgeront leurs fils et leurs filles; ils brûleront leurs maisons par le feu.
Anthuwo adzawaponye miyala akazi awiriwo ndi kuwatema ndi malupanga awo. Ana awo aamuna ndi aakazi adzawaphe ndi kutentha nyumba zawo.
48 Ainsi je mettrai fin aux infamies dans le pays, et toutes les femmes apprendront à ne point imiter vos désordres.
“Motero Ine ndidzathetsa zachigololo mʼdzikomo, ndipo akazi onse adzatengapo phunziro kuti asadzachite zachigololo monga za iwowo.
49 On fera retomber sur vous-mêmes vos infamies; vous porterez la peine de vos péchés d'idolâtrie, et vous saurez que je suis le Seigneur, l'Éternel.
Ndidzawalanga chifukwa cha ntchito zawo za dama ndipo adzazunzika chifukwa cha tchimo lawo lopembedza mafano. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Ambuye Yehova.”

< Ézéchiel 23 >