< 2 Samuel 22 >

1 Et David adressa à l'Éternel les paroles de ce cantique, au jour où l'Éternel l'eut délivré de la main de tous ses ennemis, et de la main de Saül.
Davide anayimbira Yehova nyimbo iyi pamene Yehovayo anamupulumutsa mʼdzanja la adani ake onse ndiponso mʼdzanja la Sauli.
2 Il dit: Éternel, mon rocher, ma forteresse et mon libérateur!
Iye anati, “Yehova ndiye thanthwe langa, chitetezo changa ndi mpulumutsi wanga.
3 O Dieu, mon rocher, vers qui je me retire; mon bouclier et la force qui me délivre, ma haute retraite et mon asile! mon Sauveur! tu me garantis de la violence.
Mulungu wanga ndiye thanthwe langa, mʼmene ndimathawiramo, chishango changa ndi ndodo yachipulumutso changa. Iye ndi linga langa, pothawirapo panga ndi mpulumutsi wanga. Munandipulumutsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
4 Je m'écrie: Loué soit l'Éternel! Et je suis délivré de mes ennemis.
“Ndimayitana Yehova amene ndi woyenera matamando, ndipo ndapulumutsidwa kwa adani anga.
5 Car les flots de la mort m'avaient environné, les torrents des méchants m'avaient effrayé;
“Mafunde a imfa anandizinga; mitsinje yothamanga yachiwonongeko inandiopsa kwambiri.
6 Les liens du Sépulcre m'avaient environné; les filets de la mort m'avaient surpris. (Sheol h7585)
Anandimanga ndi zingwe za ku manda; misampha ya imfa inalimbana nane. (Sheol h7585)
7 Dans ma détresse, j'invoquai l'Éternel, je criai à mon Dieu; de son palais il entendit ma voix, et mon cri parvint à ses oreilles.
“Mʼmasautso anga ndinapemphera kwa Yehova; ndinapemphera kwa Mulungu wanga. Iye ali mʼnyumba yake, anamva mawu anga; kulira kwanga kunafika mʼmakutu ake.
8 Alors la terre fut ébranlée et trembla, les fondements des cieux s'agitèrent et s'ébranlèrent, parce qu'il était courroucé.
“Dziko lapansi linanjenjemera ndi kuchita chivomerezi, maziko a miyamba anagwedezeka; ananjenjemera chifukwa Iye anakwiya.
9 Une fumée montait de ses narines, et de sa bouche un feu dévorant; il en jaillissait des charbons embrasés.
Mʼmphuno mwake munatuluka utsi; moto wonyeketsa unatuluka mʼkamwa mwake, makala amoto anali lawilawi mʼkamwa mwake.
10 Il abaissa les cieux, et descendit, ayant l'obscurité sous ses pieds.
Iye anangʼamba thambo natsika pansi; pansi pa mapazi ake panali mitambo yakuda.
11 Il était monté sur un chérubin et volait; il parut sur les ailes du vent.
Iye anakwera pa Kerubi ndi kuwuluka; nawuluka ndi mphepo mwaliwiro.
12 Il mit autour de lui les ténèbres comme une tente, des amas d'eaux, des nuées épaisses.
Iye anapanga mdima kukhala chofunda chake, mitambo yakuda ya mlengalenga.
13 De la splendeur qui était devant lui, s'embrasèrent des charbons de feu.
Mʼkuwala kumene kunali pamaso pake munkachokera makala amoto alawilawi.
14 L'Éternel tonna des cieux; le Très-Haut fit retentir sa voix.
Yehova anabangula kumwamba ngati bingu, mawu a Wammwambamwamba anamveka ponseponse.
15 Il lança des flèches, et dispersa mes ennemis; il lança des éclairs, et les mit en déroute.
Iye anaponya mivi yake, nabalalitsa adani ake, ndi zingʼaningʼani zake anawagonjetsa.
16 Alors le fond de la mer apparut, et les fondements du monde se découvrirent, par la menace de l'Éternel, par le souffle du vent de sa colère.
Zigwa za mʼnyanja zinaonekera poyera, ndipo maziko a dziko lapansi anakhala poyera, Yehova atabangula mwaukali, pamene mpweya wamphamvu unatuluka mʼmphuno mwake.
17 Il étendit sa main d'en haut, et me prit; il me tira des grosses eaux.
“Ali kumwamba, Iye anatambalitsa dzanja lake ndipo anandigwira; anandivuwula mʼmadzi ozama.
18 Il me délivra de mon ennemi puissant, et de mes adversaires qui étaient plus forts que moi.
Anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu, adani anga amene anali amphamvu kuposa ine.
19 Ils m'avaient surpris au jour de ma calamité, mais l'Éternel fut mon appui.
Adaniwo analimbana nane pamene ndinali pa mavuto, koma Yehova anali thandizo langa.
20 Il m'a mis au large; il m'a délivré, parce qu'il a pris son plaisir en moi.
Iye anandipititsa kumalo otakasuka; anandipulumutsa chifukwa amakondwera nane.
21 L'Éternel m'a traité selon ma justice; il m'a rendu selon la pureté de mes mains;
“Yehova wandithandiza molingana ndi chilungamo changa; molingana ndi makhalidwe anga abwino, Iye wandipulumutsa.
22 Car j'ai gardé les voies de l'Éternel, et je n'ai point été infidèle à mon Dieu.
Pakuti ine ndinatsata njira za Yehova; ndilibe mlandu wochoka pamaso pa Mulungu wanga.
23 Car toutes ses ordonnances sont devant moi, et je ne m'écarte point de ses statuts.
Malamulo ake onse ali pamaso panga, sindinasiye malangizo ake.
24 J'ai été intègre devant lui, et je me suis gardé de mon iniquité.
Ndakhala moyo wosalakwa pamaso pake ndipo ndakhala ndi kupewa tchimo.
25 Aussi l'Éternel m'a rendu selon ma justice, selon ma pureté à ses yeux.
Yehova wandipatsa mphotho molingana ndi chilungamo changa, molingana ndi makhalidwe anga abwino pamaso pake.
26 Avec celui qui est bon, tu es bon; avec l'homme intègre tu es intègre.
“Kwa wokhulupirika, Inu mumaonetsa kukhulupirika kwanu, kwa anthu amakhalidwe abwino, Inu mumaonetsanso makhalidwe abwino,
27 Avec celui qui est pur, tu te montres pur; mais avec le pervers, tu agis selon sa perversité.
Kwa woyera mtima, Inu mumaonetsa kuyera mtima kwanu, koma kwa anthu achinyengo mumaonetsanso kunyansidwa nawo.
28 Tu sauves le peuple affligé; mais de ton regard tu abaisses les orgueilleux.
Inu mumapulumutsa anthu odzichepetsa, koma maso anu amatsutsana ndi odzikuza ndipo mumawatsitsa.
29 Car tu es ma lampe, ô Éternel! Et l'Éternel fait resplendir mes ténèbres.
Inu Yehova, ndinu nyale yanga; Yehova wasandutsa mdima wanga kukhala kuwunika.
30 Avec toi je fonds sur une troupe; avec mon Dieu je franchis la muraille.
Ndi thandizo lanu nditha kulimbana ndi gulu la ankhondo, ndi Mulungu wanga nditha kuchita zosatheka ndi munthu.
31 La voie de Dieu est parfaite, la parole de l'Éternel est éprouvée; il est le bouclier de tous ceux qui se retirent vers lui.
“Kunena za Mulungu, zochita zake ndi zangwiro; mawu a Yehova alibe cholakwika. Iye ndi chishango kwa onse amene amathawira kwa iye.
32 Car qui est Dieu, sinon l'Éternel? Et qui est un rocher, sinon notre Dieu?
Mulungu wina ndi uti wofanana nanu Yehova? Ndipo ndani amene ndi Thanthwe kupatula Mulungu wathu?
33 Le Dieu qui est ma forteresse assurée, et qui enseigne à l'homme intègre sa voie;
Ndi Mulungu amene anandipatsa mphamvu ndi kulungamitsa njira yanga.
34 Qui rend mes pieds semblables à ceux des biches, et m'affermit sur mes hauteurs;
Iye amasandutsa mapazi anga kukhala ngati ambawala yayikazi; Iye amandithandiza kuyimirira pamwamba pa mapiri.
35 Qui forme mes mains au combat, et mes bras bandent un arc d'airain.
Iye amaphunzitsa manja anga kuchita nkhondo; manja anga amatha kuthyola uta wachitsulo.
36 Tu m'as donné le bouclier de ton salut, et ta bonté m'a fait devenir grand.
Inu mundipatsa ine chishango chanu cha chigonjetso; mumawerama kuti mundikweze.
37 Tu élargis le chemin sous mes pas, et mes pieds ne chancellent point.
Inu mwalimbitsa njira yanga kuti ndiyende bwino, kuti mapazi anga asaterereke.
38 Je poursuis mes ennemis; je les détruis; et je ne reviens qu'après les avoir exterminés.
“Ine ndinathamangitsa adani anga ndi kuwakantha; sindinabwerere mpaka iwo atawonongedwa.
39 Je les consume, je les écrase, et ils ne se relèvent plus; ils tombent sous mes pieds.
Ndinawakantha kotheratu, ndipo sanathe kudzukanso; Iwo anagwera pansi pa mapazi anga.
40 Car tu m'as ceint de force pour le combat; tu fais plier sous moi mes adversaires.
Inu munandipatsa ine mphamvu yochitira nkhondo; munagwaditsa adani anga pa mapazi anga.
41 Tu fais tourner le dos à mes ennemis devant moi; ceux qui me haïssent, je les détruis.
Inu muchititsa kuti adani anga atembenuke ndi kuthawa; ndipo ndinawononga adani anga.
42 Ils regardent, et point de libérateur! Ils crient à l'Éternel, mais il ne leur répond point.
Iwo anafuwula kupempha thandizo, koma panalibe ndi mmodzi yemwe owapulumutsa. Analirira kwa Yehova, koma sanawayankhe.
43 Et je les broie comme la poussière de la terre; je les écrase, je les foule comme la boue des rues.
Ine ndinawaperesa ngati fumbi la pa dziko lapansi; ndinawasinja ndipo ndinawapondaponda ngati matope a mʼmisewu.
44 Tu me sauves des dissensions de mon peuple; tu me gardes pour être chef des nations. Le peuple que je ne connaissais pas, m'est assujetti.
“Inu mwandipulumutsa mʼmanja mwa mitundu ya anthu; Inu mwandisunga kuti ndikhale mtsogoleri wa anthu a mitundu ina. Anthu amene sindikuwadziwa ali pansi pa ulamuliro wanga.
45 Les fils de l'étranger viennent me flatter; dès que leur oreille a entendu, ils se sont soumis.
Alendo amadzipereka okha pamaso panga; akangomva za ine, amandigonjera.
46 Les fils de l'étranger défaillent, et sortent tremblants de leurs retraites.
Iwo onse anataya mtima; anatuluka mʼmalinga awo akunjenjemera.
47 L'Éternel est vivant! Et béni soit mon rocher! Que Dieu, le rocher de mon salut, soit exalté!
“Yehova ndi wamoyo! Litamandidwe Thanthwe langa. Akuzike Mulungu, Thanthwe, Mpulumutsi wanga!
48 Le Dieu qui me donne vengeance, et qui m'assujettit les peuples; qui me fait échapper à mes ennemis.
Iye ndi Mulungu amene amabwezera chilango, amene amayika anthu a mitundu yonse pansi pa ulamuliro wanga,
49 Tu m'élèves au-dessus de mes adversaires, tu me délivres de l'homme violent.
amene amandimasula mʼmanja mwa adani anga. Inu munandikuza kuposa adani anga; munandilanditsa mʼmanja mwa anthu ankhanza.
50 C'est pourquoi, ô Éternel, je te louerai parmi les nations, et je chanterai ton nom!
Choncho ine ndidzakutamandani Inu Yehova, pakati pa anthu a mitundu ina; ndidzayimba nyimbo zotamanda dzina lanu.
51 C'est lui qui délivre magnifiquement son roi, et qui fait miséricorde à son oint, à David et à sa postérité, à jamais!
“Iye amapereka chipambano chachikulu kwa mfumu yake, amaonetsa kukoma mtima kwa wodzozedwa wake, kwa Davide ndi zidzukulu zake kwamuyaya.”

< 2 Samuel 22 >