< 2 Chroniques 22 >
1 Les habitants de Jérusalem établirent pour roi à sa place Achazia, le plus jeune de ses fils, parce que les troupes qui étaient venues au camp avec les Arabes, avaient tué tous les plus âgés; et Achazia, fils de Joram, roi de Juda, régna.
Anthu a mu Yerusalemu anayika Ahaziya mwana wamngʼono kwambiri wa Yehoramu kukhala mfumu mʼmalo mwake, popeza gulu lankhondo limene linabwera ndi Aarabu ku misasa, linapha ana onse aakulu. Motero Ahaziya mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Achazia était âgé de quarante-deux ans, quand il devint roi, et il régna un an à Jérusalem. Sa mère s'appelait Athalie, fille d'Omri.
Ahaziya anali wa zaka 22 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu chaka chimodzi. Dzina la amayi ake linali Ataliya, chidzukulu cha Omuri.
3 Il suivit aussi les voies de la maison d'Achab; car sa mère était sa conseillère pour faire du mal.
Nayenso anayenda mʼnjira ya banja la Ahabu, pakuti amayi ake anamulimbikitsa kuchita zolakwika.
4 Il fit donc ce qui est mauvais aux yeux de l'Éternel, comme la maison d'Achab; parce qu'ils furent ses conseillers après la mort de son père, pour sa ruine.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova monga momwe banja la Ahabu linachitira, pakuti atamwalira abambo ake, iwo anakhala alangizi ake, kumene kunali kudziwononga kwake.
5 Gouverné par leurs conseils, il alla même avec Joram, fils d'Achab, roi d'Israël, à la guerre, à Ramoth de Galaad, contre Hazaël, roi de Syrie. Et les Syriens frappèrent Joram,
Iyeyo anatsatiranso uphungu wawo pamene anapita ndi Yehoramu, mwana wa Ahabu, mfumu ya Israeli kukachita nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aramu ku Ramoti Giliyadi. Aaramu anavulaza Yehoramu,
6 Qui s'en retourna pour se faire guérir à Jizréel, des blessures que les Syriens lui avaient faites à Rama, lorsqu'il faisait la guerre contre Hazaël, roi de Syrie. Alors Azaria, fils de Joram, roi de Juda, descendit pour voir Joram, le fils d'Achab, à Jizréel, parce qu'il était malade.
kotero iye anabwerera ku Yezireeli kuti akachire mabala amene anamuvulaza ku Ramoti pa nkhondo ndi Hazaeli mfumu ya Aaramu. Ndipo Ahaziya, mwana wa Yehoramu mfumu ya Yuda anapita ku Yezireeli kukaona Yehoramu mwana wa Ahabu chifukwa anavulazidwa.
7 Or ce fut pour son entière ruine, qui procédait de Dieu, qu'Achazia vint auprès de Joram. En effet, quand il fut arrivé, il sortit avec Joram au-devant de Jéhu, fils de Nimshi, que l'Éternel avait oint pour exterminer la maison d'Achab.
Mulungu anakonza kuti Ahaziya akaphedwe pa ulendo wake wokacheza. Ahaziya atafika, iye ndi Yoramu anapita kukakumana ndi Yehu mwana wa Nimisi, amene Yehova anamudzoza kuti akawononge banja la Ahabu.
8 Et il arriva, comme Jéhu faisait justice de la maison d'Achab, qu'il trouva les chefs de Juda et les fils des frères d'Achazia, qui servaient Achazia, et il les tua.
Pamene Yehu ankalanga banja la Ahabu anapeza atsogoleri a ku Yuda ndiponso ana aamuna a abale ake a Ahaziya amene amatumikira Ahaziya, ndipo anawapha.
9 Il chercha ensuite Achazia, qui s'était caché à Samarie; on le prit, et on l'amena vers Jéhu, et on le fit mourir. Puis on l'ensevelit, car on dit: C'est le fils de Josaphat, qui a recherché l'Éternel de tout son cœur. Et il n'y eut plus personne dans la maison d'Achazia qui fût capable de régner.
Kenaka anapita kukafunafuna Ahaziya, ndipo anthu ake anagwira Ahaziya pamene amabisala mu Samariya. Anabwera naye kwa Yehu ndipo anaphedwa. Iwo anamuyika mʼmanda, pakuti anati, “Iyeyu anali mwana wa Yehosafati amene anafunafuna Yehova ndi mtima wake wonse.” Kotero panalibe wamphamvu mʼbanja la Ahaziya kuti nʼkukhala mfumu.
10 Or Athalie, mère d'Achazia, voyant que son fils était mort, se leva, et extermina toute la race royale de la maison de Juda.
Ataliya, amayi ake a Ahaziya, ataona kuti mwana wawo wafa, ananyamuka nakapha onse a banja laufumu la Yuda.
11 Mais Joshabath, fille du roi Joram, prit Joas, fils d'Achazia, le déroba d'entre les fils du roi qu'on faisait mourir, et le mit avec sa nourrice, dans la salle des lits. Ainsi Joshabath, fille du roi Joram et femme de Jéhojada, le sacrificateur, étant la sœur d'Achazia, le cacha aux yeux d'Athalie, qui ne le fit point mourir.
Koma Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, anatenga Yowasi mwana wa Ahaziya, momuba ndi kumuchotsa pakati pa ana aamuna a mfumu amene amati aphedwe ndipo anamuyika iye ndi mlezi wake mʼchipinda chogona. Motero Yehoseba, mwana wamkazi wa mfumu Yehoramu, mkazi wa wansembe Yehoyada, yemwe anali mlongo wake wa Ahaziya anamubisa mwanayo kuti Ataliya asamuphe.
12 Il fut ainsi caché avec eux, six ans, dans la maison de Dieu; et Athalie régnait sur le pays.
Mwanayo anakhala mobisala pamodzi ndi iwo mu Nyumba ya Mulungu kwa zaka zisanu ndi chimodzi muulamuliro wa Ataliya.