< Luc 14 >
1 Un jour de sabbat, Jésus entra dans la maison d'un des principaux pharisiens pour y manger; et on l'observait.
Pa tsiku lina la Sabata, Yesu atapita kukadya ku nyumba ya Mfarisi wodziwika, Afarisi anamulonda mosamalitsa.
2 Comme il se trouvait avoir devant lui un homme hydropique,
Poteropo, patsogolo pake panali munthu amene anadwala matenda otupa mimba ndi miyendo.
3 il prit la parole, et s'adressant aux docteurs de la Loi et aux pharisiens, il leur dit: «Est-il permis, oui ou non, de guérir au jour du sabbat?»
Yesu anafunsa Afarisi ndi akatswiri amalamulo kuti, “Kodi ndi zololedwa kuchiritsa pa tsiku la Sabata kapena ayi?”
4 Ils gardèrent le silence. Alors Jésus saisissant l'hydropique, le guérit, et le renvoya.
Koma iwo sanayankhe. Tsono atamutenga munthuyo, Iye anamuchiritsa ndipo anamuwuza kuti azipita.
5 Puis, prenant la parole, il dit: «Qui de vous, si son fils ou son boeuf vient à tomber dans un puits, ne l'en retire aussitôt, le jour du sabbat?»
Kenaka Iye anawafunsa kuti, “Kodi ngati mmodzi mwa inu ali ndi mwana wamwamuna kapena ngʼombe imene yagwera mʼchitsime tsiku la Sabata, kodi simungamuvuwulemo tsiku lomwelo?”
6 Et ils ne surent que lui répondre.
Ndipo iwo analibe choyankha.
7 Ayant remarqué que les conviés choisissaient les premières places, il leur adressa cette comparaison:
Iye ataona momwe alendo amasankhira malo aulemu pa tebulo, Iye anawawuza fanizo ili:
8 «Quand on t'invitera à des noces, ne prends pas la première place, de peur qu'il ne se trouve parmi les invités un homme plus considéré que toi,
“Pamene wina wakuyitanani ku phwando la ukwati, musakhale pa malo aulemu ayi, chifukwa mwina anayitananso munthu wina wolemekezeka kuposa inu.
9 et que celui qui vous aura invités, l'un et l'autre, ne te dise: «Cède-lui la place, » car alors tu auras la confusion d'aller occuper la dernière place.
Ngati zitatero, ndiye kuti munthu uja amene anakuyitani inu nonse awiri adzakuwuzani kuti, ‘Mupatseni munthu uyu malo anu.’ Pamenepo inu mudzachita manyazi, pokakhala malo wotsika.
10 Mais, lorsqu'on t'invite, va te mettre à la dernière place, et, quand celui qui t'a invité viendra, il te dira: «Cher ami, monte plus haut; » alors ce sera pour toi un honneur aux yeux des autres convives.
Koma akakuyitanani, khalani pa malo otsika, kuti amene anakuyitanani uja adzakuwuzeni kuti, ‘Bwenzi, bwera udzakhale pa malo aulemu pano.’ Pamenepo inu mudzalandira ulemu pamaso pa alendo anzanu onse.
11 Car quiconque s'élève, sera abaissé; et quiconque s'abaisse, sera élevé.»
Pakuti aliyense wodzikuza adzamuchepetsa, ndipo aliyense wodzichepetsa adzamukweza.”
12 Il disait aussi à celui qui l'avait invité: «Quand tu donnes à dîner ou à souper, n'invite ni tes amis, ni tes frères, ni tes parents, ni tes voisins riches, de peur qu'ils ne t'invitent aussi a leur tour et ne te rendent la pareille.
Kenaka Yesu anati kwa mwini malo uja, “Ukakonza chakudya chamasana kapena chamadzulo, usamayitane abwenzi ako, abale ako, anthu afuko lako kapena anzako achuma; ngati iwe utero, iwo adzakuyitananso, choncho udzalandiriratu mphotho yako.
13 Mais, quand tu donnes un repas, invite les pauvres, les estropiés, les boiteux, les aveugles,
Koma ukakonza phwando, itana anthu osauka, ofa ziwalo, olumala ndi osaona.
14 et tu seras heureux de ce qu'ils ne peuvent te le rendre: cela te sera rendu à la résurrection des justes.»
Pamenepo udzakhala wodala, chifukwa iwo sangakubwezere kanthu, koma Mulungu ndiye adzakubwezera pa chiukitso cha olungama.”
15 Un des convives, qui avait entendu ces recommandations, lui dit: «Heureux celui qui sera a table dans le royaume de Dieu!»
Mmodzi mwa amene amadya naye atamva izi, anati kwa Yesu, “Ndi wodala munthu amene adzadye nawo mu ufumu wa Mulungu.”
16 Jésus lui dit: «Un homme donna un grand souper, et y convia beaucoup de monde.
Yesu anayankha kuti, “Munthu wina ankakonza phwando lalikulu ndipo anayitana alendo ambiri.
17 A l'heure du souper, il envoya son serviteur dire aux invités: «Venez, car tout est prêt.»
Nthawi yaphwando itakwana anatuma wantchito wake kuti akawuze onse amene anayitanidwa kuti, ‘Bwerani, pakuti zonse zakonzeka.’
18 Et ils se mirent à s'excuser tout d'une voix. Le premier lui dit: «J'ai acheté un champ, et je suis forcé de sortir pour le voir; je te prie de m'excuser.»
“Koma onse anayamba kupereka zifukwa mofanana. Woyamba anati, ‘Ine ndangogula kumene munda, ndipo ndikuyenera kupita kuti ndikawuone. Pepani mundikhululukire.’
19 Un autre dit: «J'ai acheté cinq paires de boeufs, et je vais les essayer; je te prie de m'excuser.»
“Wina anati, ‘Ndangogula kumene ngʼombe khumi zokoka ngolo ndipo kupita kukaziyesa. Pepani mundikhululukire.’
20 Un autre dit: «Je viens de me marier, ainsi je n'y puis aller.»
“Wina anatinso, ‘Ine ndangokwatira kumene, choncho sinditha kubwera.’
21 Le serviteur étant de retour, rapporta ces refus à son maître. Alors le maître de la maison, irrité, dit à son serviteur: «Va vite dans les places et dans les rues de la ville, et amène ici les pauvres, les estropiés, les aveugles, les boiteux.»
“Wantchitoyo anabwera ndikudzamuwuza bwana wakeyo zimenezi. Pamenepo mphwandoyo anapsa mtima ndipo analamula wantchito wakeyo kuti, ‘Pita msangamsanga kunja mʼmisewu ndi mʼmakwalala a mu mzinda ndipo ukabweretse osauka, ofa ziwalo, osaona ndi olumala.’
22 Le serviteur de retour, dit: «Maître, tes ordres ont été exécutés, et il y a encore de la place.»
“Wantchitoyo anati, ‘Bwana, zimene munanena zachitika koma malo akanalipobe.’
23 Et le maître dit à son serviteur: «Va dans les chemins et le long des haies, et presse les gens d'entrer, afin que ma maison soit pleine;
“Ndipo mbuye uja anawuza wantchito wake kuti, ‘Pita kunja ku misewu ikuluikulu ndi kunja kwa mpanda ndipo ukawawuze kuti alowe, kuti nyumba yanga idzaze.
24 car je vous déclare qu'aucun de ceux qui avaient été conviés, ne goûtera de mon souper.»
Ine ndikukuwuzani inu kuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anayitanidwa adzalawa phwandolo.’”
25 Comme une foule considérable cheminait avec Jésus, il se retourna, et lui dit:
Gulu lalikulu la anthu linkayenda naye Yesu ndipo atatembenukira kwa iwo anati,
26 «Si quelqu'un vient à moi, et ne hait pas son père, sa mère, sa femme, ses enfants, ses frères et ses soeurs, bien plus, s'il ne hait pas sa propre vie, il ne peut être mon disciple;
“Ngati wina aliyense abwera kwa Ine ndipo sadana ndi abambo ndi amayi ake, mkazi wake ndi ana, abale ake ndi alongo ake, inde ngakhale moyo wake omwe, iye sangakhale ophunzira wanga.
27 et quiconque ne porte pas sa croix et ne me suit pas, ne peut être mon disciple.
Ndipo aliyense amene sasenza mtanda wake ndi kunditsata Ine sangakhale ophunzira wanga.
28 Car quel est celui d'entre vous, qui, voulant bâtir une tour, ne s'asseye premièrement pour calculer la dépense, et pour voir s'il a de quoi en venir à bout?
“Taganizani, ngati wina mwa inu akufuna kumanga nsanja, kodi iye sayamba wakhala pansi ndi kuganizira za mtengo wake kuti aone ngati ali ndi ndalama zokwanira kuti atsirizire?
29 de peur qu'après avoir posé les fondements de l'édifice, il ne puisse l'achever, et que tous ceux qui le verront ne se mettent à se moquer de lui,
Pakuti ngati ayika maziko ndi kulephera kutsiriza, aliyense amene adzayiona adzamuseka,
30 et à dire: «Cet homme a commencé à bâtir, et il n'a pu achever.»
nanena kuti, ‘Munthu uyu anayamba kumanga koma sanathe kutsiriza.’
31 Ou bien, quel est le roi, qui, étant sur le point d'aller livrer bataille à un autre roi, ne s'asseye premièrement pour délibérer, et pour voir s'il peut, avec dix mille hommes, marcher à la rencontre d'un ennemi qui s'avance contre lui avec vingt mille?
“Kapena mfumu imene ikupita ku nkhondo kukamenyana ndi mfumu ina, kodi siyamba yakhala pansi ndi kulingalira ngati ingathe ndi anthu 10,000 kulimbana ndi amene akubwera ndi 20,000?
32 Autrement, pendant que celui-ci est encore éloigné, il lui envoie une ambassade pour négocier la paix.
Ngati singathe, idzatuma nthumwi pomwe winayo ali kutali ndi kukapempha mgwirizano wamtendere.
33 De même, quiconque d'entre vous ne renonce pas à tout ce qu'il possède, ne peut être mon disciple.
Mʼnjira yomweyo, wina aliyense wa inu amene sasiya zonse ali nazo sangakhale ophunzira wanga.
34 C'est donc une bonne chose que le sel; mais si le sel aussi devient insipide, avec quoi lui donnera-t-on de la saveur?
“Mchere ndi wabwino, koma ngati usukuluka adzawukoleretsanso ndi chiyani?
35 Il n'est bon ni pour la terre ni pour le fumier: on le jette dehors. Que celui qui a des oreilles pour entendre, entende.»
Suyeneranso ngakhale mʼnthaka kapena kudzala la manyowa; umatayidwa kunja. “Amene ali ndi makutu akumva, amve.”