< Jacques 3 >

1 Mes frères, qu'il n'y ait pas parmi vous tant de gens qui s'érigent en docteurs; vous savez que par là on s'expose à un arrêt plus sévère.
Abale anga, ambiri musakhale aphunzitsi chifukwa mumadziwa kuti aphunzitsife tidzaweruzidwa mowuma kuposa anthu ena onse.
2 Tous, en effet, nous bronchons fort. Si quelqu'un ne bronche pas en paroles, c'est un homme parfait, capable de tenir en bride son corps tout entier.
Tonsefe timapunthwa mʼnjira zambiri. Ngati wina salakwa poyankhula, ameneyo ndi munthu wangwiro, wodziwa kuyangʼanira bwino thupi lake lonse.
3 Si, pour nous faire obéir des chevaux, nous leur mettons le mors dans la bouche, nous gouvernons aussi leur corps tout entier.
Tikayika tizitsulo mʼkamwa mwa akavalo kuti atimvere, timatha kuwongolera thupi lake lonse.
4 Voyez encore les navires: tout grands qu'ils sont, et quoique poussés par des vents violents, ils sont dirigés au gré du pilote, par un bien petit gouvernail.
Taonani sitima zapamadzi. Ngakhale ndi zazikulu kwambiri ndipo zimakankhidwa ndi mphepo yamphamvu, zimawongoleredwa ndi tsigiro lalingʼono kulikonse kumene woyendetsayo akufuna kupita.
5 De même aussi la langue est un petit membre, et elle peut se vanter de grandes choses. Voyez quelle grande forêt un petit feu allume!
Momwemonso, lilime ndi kachiwalo kakangʼono ka thupi koma limadzitama kuti nʼkuchita zikuluzikulu. Tangoganizirani za nkhalango yayikulu imene ingapse ndi kalawi kamoto koyamba mochepa.
6 La langue aussi est un feu, le monde de la méchanceté: c'est la langue qui, parmi les membres, a l'art de souiller le corps tout entier, et d'enflammer tout le cours de la vie, étant enflammée elle-même du feu de la Géhenne. (Geenna g1067)
Lilime nalonso ndi moto, dziko la zoyipa pakati pa ziwalo za thupi. Limawononga munthu yense wathunthu. Limayika zonse za moyo wake pa moto, ndipo moto wake ndi wochokera ku gehena. (Geenna g1067)
7 Toute espèce de bêtes sauvages et d'oiseaux, de reptiles et d'animaux marins se domptent, et ont été domptés par l'espèce humaine,
Mitundu yonse ya nyama, ya mbalame, ya zokwawa ndi ya zolengedwa za mʼnyanja, zikuwetedwa ndipo munthu wakhala akuziweta,
8 mais la langue, aucun homme ne peut la dompter: c'est un fléau qu'on ne peut arrêter; elle est pleine d'un venin mortel.
koma palibe munthu amene angaweta lilime. Lilime ndipo silitha kupuma, ndi lodzaza ndi ululu wakupha.
9 Avec la langue, nous bénissons le Seigneur, notre Père; et avec la langue, nous maudissons les hommes, qui sont faits à la ressemblance de Dieu:
Ndi lilime lomwelo timatamanda Ambuye ndi Atate athu, komanso ndi lilime lomwelo timalalatira anthu, amene anapangidwa mʼchifanizo cha Mulungu.
10 de la même bouche sortent la bénédiction et la malédiction! Il ne faut pas, mes frères, qu'il en soit ainsi:
Mʼkamwa momwemo mutuluka matamando ndi kulalata. Abale anga, zisamatero ayi.
11 est-ce que la source jette par la même ouverture le doux et l'amer?
Kodi madzi abwino ndi a mchere angatuluke pa kasupe mmodzi?
12 est-ce qu'un figuier, mes frères, peut donner des olives, ou une vigne des figues? de l'eau salée ne peut non plus donner de l'eau douce.
Abale anga, kodi mtengo wa mkuyu nʼkubala mphesa, kapena mtengo wampesa nʼkubala nkhuyu? Kasupe wa madzi a mchere sangatulutsenso madzi abwino.
13 Y a-t-il parmi vous quelque homme sage et instruit, qu'il montre par sa bonne conduite qu'il agit avec la douceur de la sagesse.
Ndani mwa inu amene ndi wanzeru ndi womvetsa zinthu? Mulekeni aonetse ndi makhalidwe ake abwino kuti nzeru ndiye zikutsogolera kudzichepetsa kwake ndi zochita zake
14 Si vous avez dans le coeur un zèle amer et un esprit de dispute, ne vous glorifiez pas de votre sagesse, vous parleriez contre toute vérité.
Koma ngati muli ndi mtima wakaduka ndi odzikonda, musadzitamandire kapena kukana choonadi.
15 Ce n'est point là la sagesse qui vient d'en haut; c'est une sagesse terrestre, animale, diabolique,
“Nzeru” zotere sizochokera kumwamba koma ndi za mʼdziko lapansi, si zauzimu koma ndi za ziwanda.
16 car là où il y a zèle et esprit de dispute, il y a du désordre et toutes sortes de mauvaises choses;
Pakuti pamene pali kaduka ndi kudzikonda pomweponso pamakhala chisokonezo ndi zochitika zoyipa zonse.
17 tandis que la sagesse qui vient d'en haut est premièrement pure, ensuite paisible, douce, traitable, pleine de miséricorde et de bons fruits, sans partialité, sans hypocrisie:
Koma nzeru imene imachoka kumwamba, poyamba ndi yangwiro, ndi yokonda mtendere, yoganizira za ena, yogonjera, yodzaza ndi chifundo ndi chipatso chabwino, yosakondera ndi yoona mtima.
18 le fruit de justice se sème dans la paix par ceux qui apportent la paix.
Anthu amtendere amene amadzala mtendere amakolola chilungamo.

< Jacques 3 >