< Hébreux 7 >

1 En effet, ce Melchisédec, roi de Salem, sacrificateur du Dieu Très-Haut, qui alla au-devant d'Abraham, lorsqu'il revenait de la défaite des rois, — qui le bénit
Melikizedeki ameneyu anali mfumu ya ku Salemu, ndiponso wansembe wa Mulungu Wammwambamwamba. Anakumana ndi Abrahamu pamene ankabwerera kuchokera ku nkhondo atagonjetsa mafumu aja, Melikizedeki anakumana naye namudalitsa.
2 et reçut d'Abraham la dîme de tout le butin, — qui est d'abord roi de justice, d'après l'interprétation de son nom, puis roi de Salem, c’est-à-dire, roi de paix,
Ndipo Abrahamu anamupatsa chakhumi cha zonse anafunkha. Choyamba dzina la Melikizedeki likutanthauza, “Mfumu ya chilungamo,” kenakanso, “Mfumu ya Salemu,” kutanthauza, “Mfumu ya mtendere.”
3 — qui est sans père, sans mère, sans aïeux, sans commencement de jours ni fin de vie, — qui est enfin tout à fait semblable au Fils de Dieu, ce Melchisédec, dis-je, demeure sacrificateur à perpétuité.
Alibe abambo kapena mayi, alibe chiyambi kapena chitsiriziro cha moyo wake. Iye ali ngati Mwana wa Mulungu ndipo akupitirira kukhala wansembe wamuyaya.
4 Considérez combien est grand ce personnage, à qui le patriarche même, Abraham, donna une dîme prise sur le meilleur du butin.
Mukuona tsono kuti munthuyo anali wamkulu ndithu, pakuti Abrahamu kholo lathu anamupatsa chakhumi cha zimene anafunkha.
5 Ceux des fils de Lévi, qui reçoivent la sacrificature, ont l'ordre, d'après la Loi, de lever la dîme sur le peuple, c’est-à-dire, sur leurs frères, quoique ceux-ci soient issus d'Abraham;
Tsono lamulo likuti, ana a Levi amene amakhala ansembe azilandira chakhumi kuchokera kwa Aisraeli, abale awo ngakhale kuti abale awowo ndi ochokera kwa Abrahamu.
6 et un homme qui n'appartenait point à leur famille, a levé la dîme sur Abraham! et il a béni celui qui avait les promesses!
Melikizedeki sanali wochokera kwa Levi, komabe analandira chakhumi kuchokera kwa Abrahamu nadalitsa Abrahamuyo amene analandira malonjezo a Mulungu.
7 Or, c'est sans contredit l'inférieur qui est béni par le supérieur.
Mosakayika konse, munthu amene amadalitsa ndi wamkulu kuposa amene akudalitsidwayo.
8 De plus, ici, ce sont des hommes mortels qui perçoivent les dîmes; là, c'est un personnage dont il est attesté qu'il est éternellement vivant.
Ansembe amene amalandira chakhumi amafa, choncho Melikizedeki ndi wamkulu kuwaposa iwo chifukwa Malemba amamuchitira umboni kuti ndi wamoyo.
9 Et Lévi même, qui perçoit la dîme, la lui a, pour ainsi dire, payée en la personne d'Abraham,
Wina angathe kunena kuti Levi, amene amalandira chakhumi, anapereka chakhumicho kudzera mwa Abrahamu,
10 car il était encore dans les reins de son père, lorsque Melchisédec alla au-devant de ce patriarche.
chifukwa pamene Melikizedeki anakumana ndi Abrahamu nʼkuti Levi ali mʼthupi la kholo lake.
11 Si donc la perfection avait pu être réalisée par le moyen du sacerdoce lévitique (car le peuple a reçu une législation qui repose sur ce sacerdoce), qu'était-il encore besoin qu'il parût un autre sacrificateur «selon l’ordre de Melchisédec, » et non selon l'ordre d'Aaron?
Kukanatheka kukhala wangwiro mwa unsembe wa Levi, pakuti Malamulo anapatsidwa kwa anthu mwa unsembe wa Levi, nʼchifukwa chiyani panafunikanso wansembe wina kuti abwere, wofanana ndi Melikizedeki, osati Aaroni?
12 Une fois le sacerdoce changé, la Loi l'est aussi nécessairement.
Pakuti pamene unsembe usintha, malamulonso amayenera kusintha.
13 Le sacerdoce est effectivement changé, car celui à qui s'appliquent ces paroles, appartient à une tribu dont aucun membre n'a été attaché au service de l'autel:
Ambuye athu Yesu, amene mawuwa akunena za Iye, anali wa fuko lina, ndipo palibe aliyense wochokera fuko lakelo amene anatumikira pa guwa lansembe.
14 il est notoire que notre Seigneur est sorti de la tribu de Juda, à laquelle Moïse n'a point attribué le sacerdoce.
Pakuti nʼzodziwika bwino kuti Ambuye athu anachokera fuko la Yuda. Kunena za fuko limeneli, Mose sananenepo kanthu za ansembe.
15 Ce changement est plus évident encore, quand on voit apparaître un autre sacrificateur qui, de même que Melchisédec,
Ndipo zimene tanenazi zimamveka bwino ngati tiona kuti pafika wansembe wina wofanana ndi Melikizedeki.
16 est institué, non selon la règle d'une ordonnance charnelle, mais en vertu d'une vie qui ne finit point,
Yesu sanakhale wansembe chifukwa cha malamulo monga mwa mabadwidwe ake koma mwamphamvu ya moyo wosatha.
17 car voici le témoignage qui lui est rendu: «Tu es sacrificateur pour l’éternité, selon l'ordre de Melchisédec.» (aiōn g165)
Pakuti Mulungu anamuchitira umboni kuti, “Iwe ndi wansembe wamuyaya, monga mwa dongosolo la unsembe wa Melikizedeki.” (aiōn g165)
18 Il y a bien abrogation d'une ordonnance antérieure, à cause de son impuissance et de son inutilité
Choncho lamulo loyamba lachotsedwa chifukwa linali lofowoka ndi lopanda phindu.
19 (car la Loi n'a rien amené à la perfection), et introduction, d'autre part, d'une meilleure espérance qui nous rapproche de Dieu.
Tsono Malamulo sangathe kusandutsa chilichonse kukhala changwiro, koma mʼmalo mwake mwalowa chiyembekezo chabwino, chimenechi timayandikira nacho kwa Mulungu.
20 Et Jésus est le garant d'une alliance d'autant supérieure à la première,
Izi sizinachitiketu wopanda lumbiro. Ena ankakhala ansembe popanda lumbiro.
21 que son sacerdoce n'a pas été institué sans l'intervention du serment. (aiōn g165)
Koma Yesu ankakhala wansembe ndi lumbiro pamene Mulungu anati, “Ambuye analumbira ndipo sangasinthe maganizo ake, ‘Iwe ndi wansembe wamuyaya.’” (aiōn g165)
22 Tandis que les Lévites ont été établis sacrificateurs sans serment, Jésus l'a été avec serment par celui qui lui a dit: «Le Seigneur l'a juré, et il ne s'en repentira point: tu es sacrificateur éternellement, selon l’ordre de Melchisédec.»
Chifukwa cha lumbiroli, Yesu wakhala Nkhoswe ya Pangano lopambana.
23 De plus, ils forment, eux, une succession de sacrificateurs, parce que la mort les empêche de l'être toujours;
Tsono ansembe akale aja analipo ambiri, popeza imfa imawalepheretsa kupitiriza ntchitoyi.
24 mais lui, parce qu'il subsiste «éternellement, » il possède le sacerdoce qui ne se transmet point. (aiōn g165)
Koma Yesu popeza ndi wamuyaya, unsembe wake ndi wosatha. (aiōn g165)
25 C'est pour cela aussi qu'il peut sauver parfaitement ceux qui vont à Dieu par lui, étant toujours vivant pour intercéder en leur faveur.
Chifukwa chake Iye amapulumutsa kwathunthu amene amabwera kwa Mulungu kudzera mwa Iyeyo. Iye ali ndi moyo nthawi zonse kuti adziwapempherera iwo.
26 C'était bien là le souverain sacrificateur qu'il nous fallait: saint, innocent, sans tache, hors du contact des pécheurs et élevé au-dessus des cieux;
Uyu ndi Mkulu wa ansembe amene tikumufuna chifukwa ndi woyera, wopanda choyipa kapena chodetsa chilichonse, wosiyana ndi anthu ochimwa, ndiponso wokwezedwa kuposa zonse zakumwambaku.
27 qui ne fût pas obligé, comme les souverains sacrificateurs, d'offrir chaque jour des victimes, d'abord pour ses propres péchés, puis pour ceux du peuple; car ceci, il l'a fait une fois pour toutes en s'offrant lui-même.
Kusiyana ndi akulu a ansembe ena aja, Yesu sanafunike kupereka nsembe tsiku ndi tsiku poyamba chifukwa cha machimo ake, ndipo kenaka chifukwa cha machimo a anthu ena. Iye anadzipereka nsembe chifukwa cha machimo awo kamodzi kokha pamene anadzipereka yekha.
28 La Loi, en effet, institue souverains sacrificateurs des hommes sujets à la faiblesse; mais la parole du serment intervenue après la Loi institue souverain sacrificateur un Fils qui est parvenu pour jamais à la perfection. (aiōn g165)
Pakuti lamulo limasankha anthu amene ndi ofowoka kukhala akulu a ansembe; koma lumbiro, lomwe linabwera pambuyo pa lamulo, linasankha Mwana, amene anapangidwa kukhala wangwiro kwamuyaya. (aiōn g165)

< Hébreux 7 >