< 1 Corinthiens 9 >

1 Ne suis-je pas libre? Ne suis-je pas apôtre? N'ai-je pas vu Jésus, notre Seigneur? N'êtes-vous pas mon ouvrage dans le Seigneur?
Kodi sindine mfulu? Kodi sindine mtumwi? Kodi sindinamuone Ambuye athu Yesu? Kodi inu sindiye zotsatira za ntchito yanga mwa Ambuye?
2 Si, pour d'autres, je ne suis pas apôtre, au moins le suis-je pour vous; car vous êtes le sceau de mon apostolat dans le Seigneur:
Ngakhale kwa ena sindingakhale mtumwi, mosakayika ndine mtumwi kwa inu! Poti inu ndi chizindikiro cha utumwi wanga mwa Ambuye.
3 voilà ma réponse à mes détracteurs.
Kwa iwo wofuna kundizenga milandu ndimawayankha kuti:
4 N'avons-nous pas le droit de manger et de boire à nos frais?
Kodi ife tilibe ulamuliro wakudya ndi kumwa?
5 N'avons-nous pas le droit de mener avec nous une soeur en qualité de femme, comme font les autres apôtres, et les frères du Seigneur, et Céphas?
Kodi ife tilibe ulamuliro wotenga mkazi wokhulupirira nʼkumayenda naye monga amachitira atumwi ena ndi abale awo a Ambuye ndiponso Kefa?
6 Barnabas et moi, sommes-nous les seuls qui n'ayons pas le droit de ne point travailler?
Kodi kapena ine ndekha ndi Barnaba ndiye tikuyenera kugwira ntchito kuti tipeze zotisowa?
7 Qui jamais a porté les armes à ses propres frais? Plante-t-on une vigne pour n'en pas manger le fruit? Fait-on paître un troupeau, sans se nourrir de son lait?
Ndani angagwire ntchito ya usilikali namadzipezera yekha zofunika zonse? Kodi ndani amadzala mpesa koma wosadyako zipatso zake? Ndani amaweta nkhosa koma wosamwako mkaka wake?
8 Ce que je dis là, n'est-il que dans les usages humains? La Loi ne le dit-elle pas aussi?
Kodi moti zimene ndikunenazi ndimaganizo a umunthu chabe? Kodi Malamulo sakunena chimodzimodzinso?
9 N'est-il pas écrit dans la loi de Moïse: «Tu n'emmuselleras pas le boeuf qui foule le grain?» Est-ce que Dieu se met en peine des boeufs?
Popeza analemba mʼMalamulo a Mose kuti, “Musamange ngʼombe pakamwa pamene ikupuntha tirigu.” Kodi pamene Mulungu ananena zimenezi ankalabadira za ngʼombe zokha?
10 Ne le dit-il pas bien certainement à cause de nous? Certainement, c'est pour nous qu'il a été écrit que le laboureur doit labourer avec espoir, et que celui qui foule le grain, doit le fouler dans l'espérance d'y avoir part.
Ndithu Iyeyo amanena za ifenso, kodi si choncho? Inde, izi anazilemba chifukwa cha ife, pakuti wolima ndiponso wopuntha, onsewo amagwira ntchito mwachiyembekezo chodzagawana zokololazo.
11 Si nous avons semé pour vous les biens spirituels, est-ce beaucoup de recueillir vos biens temporels?
Ngati tidzala mbewu yauzimu pakati panu, kodi ndi chovuta kwambiri kuti tikolole zosowa zathu kuchokera kwa inu?
12 Si d'autres jouissent de ce droit sur vous, ne l’avons-nous pas à plus forte raison? Eh bien! nous n'avons point usé de ce droit: nous nous résignons à tout pour ne créer aucun obstacle à l'évangile de Christ.
Ngati ena ali ndi ufulu wothandizidwa ndi inu, kodi ife sitikuyenera kukhala nawo ufulu ochulukirapo? Koma ife sitinagwiritse ntchito ufulu umenewu. Mʼmalo mwake timangodzichitira chilichonse posafuna kutsekereza ena kumva Uthenga Wabwino wa Khristu.
13 Ne savez-vous pas que ceux qui font le service sacré vivent du temple? que ceux qui sont occupés à l'autel, ont part à l'autel?
Kodi simukudziwa kuti wogwira ntchito mʼNyumba ya Mulungu amapeza chakudya chawo mʼNyumbamo, ndipo kuti otumikira pa guwa lansembe amagawana zimene zaperekedwa pa guwa lansembelo.
14 De même, le Seigneur a prescrit à ceux qui annoncent l’évangile, de vivre de l'évangile.
Chomwechonso Ambuye akulamula kuti wolalikira Uthenga Wabwino azilandira thandizo lawo polalikira Uthenga Wabwinowo.
15 Pour moi, je n'ai profité d'aucun de ces avantages. Je n'écris point cela dans le but d'obtenir rien de semblable; mieux me vaudrait mourir que de me laisser enlever ce sujet de gloire.
Koma ine sindinagwiritse ntchito ufulu woterewu. Sindikulemba izi ndi chiyembekezo choti mundichitire zoterezi. Kuli bwino ndife kusiyana nʼkuti wina alande zomwe ndimazinyadira.
16 Car si j'annonce l'évangile, je n'ai point là de sujet de gloire; c'est une nécessité qui m'est imposée: malheur à moi si je n'annonce pas l'évangile!
Komatu ndikamalalikira Uthenga Wabwino, sindingadzitamandire popeza ndimawumirizidwa kulalikira. Tsoka kwa ine ngati sindilalikira Uthenga Wabwino!
17 Si je le fais de bon coeur, j'en ai la récompense; si je le fais à regret, la charge ne m'en est pas moins confiée.
Ngati ndikugwira ntchitoyi mwakufuna kwanga, ndili ndi mphotho; koma ngati si mwakufuna kwanga, ndiye kuti ntchitoyi ndi Ambuye anandipatsa.
18 Quelle est donc ma récompense? C'est, en annonçant l'évangile, de l'annoncer gratuitement, sans user aucunement du droit que l'évangile me donne.
Tsono mphotho yanga ndi chiyani? Ndi iyi: kuti polalikira Uthenga Wabwino ndiwupereke kwaulere komanso kuti ndisagwiritse ntchito ufulu wanga polalikira uthengawo.
19 Étant libre de tous, je me suis fait esclave de tous, pour gagner un plus grand nombre:
Ngakhale ndine mfulu ndipo sindine kapolo wa munthu, ndimadzisandutsa kapolo wa aliyense kuti ndikope ambiri mmene ndingathere.
20 j'ai été avec les Juifs, comme un juif, afin de gagner les Juifs; avec ceux qui sont sous la loi, comme si j'eusse été sous la loi, quoique, personnellement, je ne sois pas sous la loi, afin de gagner ceux qui sont sous la loi;
Kwa Ayuda ndimakhala ngati Myuda kuti ndikope Ayuda. Kwa olamulidwa ndi Malamulo ndimakhala ngati wolamulidwa nawo (ngakhale kuti sindine wolamulidwa ndi Malamulowo) kuti ndikope amene amalamulidwa ndi Malamulo.
21 avec ceux qui sont sans loi, comme si j'avais été sans loi, — quoique je ne sois point sans la loi de Dieu, étant sous la loi de Christ, — pour gagner ceux qui sont sans loi.
Kwa amene alibe Malamulo ndimakhala wopanda Malamulo (ngakhale kuti sindine wopanda Malamulo a Mulungu koma ndili pansi pa ulamuliro wa Khristu) kuti ndikope wopanda Malamulo.
22 J'ai été faible avec les faibles, afin de gagner les faibles; je me suis fait tout à tous, afin, de toutes les manières, d'en sauver quelques-uns.
Kwa ofowoka ndimakhala wofowoka, kuti ndikope ofowoka. Ndimachita zinthu zilizonse kwa anthu onse kuti mwanjira ina iliyonse ndipulumutse ena.
23 Je fais tout à cause de l'évangile, afin d'y avoir part moi-même.
Ndimachita zonsezi chifukwa cha Uthenga Wabwino, kuti ndigawane nawo madalitso ake.
24 Ne savez-vous pas que dans les courses du stade, tous courent, mais qu'un seul remporte le prix? Courez de même, afin de remporter le prix.
Kodi simukudziwa kuti pa mpikisano wa liwiro onse amathamanga ndithu, koma mmodzi yekha ndiye amalandira mphotho? Motero thamangani kuti mupate mphotho.
25 Tous ceux qui combattent dans les jeux, observent une tempérance parfaite: eux, pour remporter une couronne périssable; nous, pour une couronne impérissable.
Aliyense wochita mpikisano amakonzekera mwamphamvu. Amachita izi kuti alandire mphotho yankhata yamaluwa yomwe imafota. Koma ife timachita izi kuti tilandire mphotho yosafota.
26 Eh bien! moi, je cours de même, et ce n'est pas à l'aventure; je frappe de même, et ce n'est pas en l'air;
Choncho sindithamanga monga wothamanga wopanda cholinga; komanso sindichita mpikisano wankhonya monga munthu amene amangomenya mophonya.
27 mais je frappe mon corps et je le traite en esclave, de peur qu'après avoir prêché aux autres, je ne sois moi-même rejeté.
Ine ndimazunza thupi langa ndi kulisandutsa kapolo kuti nditatha kulalikira ena, ineyo ndingadzapezeke wosayenera kulandira nawo mphotho.

< 1 Corinthiens 9 >