< Zacharie 7 >
1 Puis il arriva la quatrième année du Roi Darius, que la parole de l'Eternel fut [adressée] à Zacharie le quatrième jour du neuvième mois, [qui est le mois de] Kisleu.
Pa chaka chachinayi cha Mfumu Dariyo, pa tsiku lachinayi la Kisilevi, mwezi wachisanu ndi chinayi, Yehova anayankhula ndi Zekariya.
2 lorsqu'on eut envoyé Saretser, et Réguem-mélec et ses gens, à la maison du [Dieu] Fort, pour supplier l'Eternel.
Anthu a ku Beteli anali atatuma Sarezeri ndi Regemu-Meleki pamodzi ndi anthu awo, kuti akapemphe chifundo kwa Yehova
3 Et pour parler aux Sacrificateurs de la maison de l'Eternel des armées, et aux Prophètes, en disant: Pleurerai-je au cinquième mois, me tenant séparé, comme j'ai déjà fait pendant plusieurs années?
pokafunsa kwa ansembe a ku Nyumba ya Yehova Wamphamvuzonse ndi aneneri kuti, “Kodi ine ndizilira ndi kusala zakudya pa mwezi wachisanu, monga mmene ndakhala ndikuchitira pa zaka zambiri?”
4 Et la parole de l'Eternel me fut [adressée], en disant:
Pamenepo Yehova Wamphamvuzonse anayankhula nane kuti,
5 Parle à tout le peuple du pays, et aux Sacrificateurs, et [leur] dis: Quand vous avez jeûné, et pleuré au cinquième [mois], et au septième, il y a déjà soixante et dix ans, avez-vous célébré ce jeûne pour l’amour de moi?
“Funsa anthu onse a mʼdziko ndi ansembe kuti, ‘Pamene munkasala zakudya pa mwezi wachisanu ndi wachisanu ndi chiwiri pa zaka 70 zapitazi, kodi munkasala chifukwa cha Ine?
6 Et quand vous buvez et mangez, n'est-ce pas vous qui mangez, et vous qui buvez?
Ndipo pamene munkadya ndi kumwa, kodi simunkachita zimenezi podzisangalatsa nokha?
7 Ne sont-ce pas les paroles que l'Eternel a fait entendre par le moyen des Prophètes qui ont été ci-devant, lorsque Jérusalem était habitée et paisible, elle et ses villes qui sont autour d'elle, et lors qu'on habitait vers le midi, et dans la plaine?
Kodi awa si mawu amene Yehova ankanena kudzera mwa aneneri oyamba aja pamene Yerusalemu ndi mizinda yake yozungulira anali pa mtendere ndi pa ulemerero, ndi pamene Negevi ndi ku madera akumadzulo a mʼmbali mwa phiri munali anthu?’”
8 Puis la parole de l'Eternel fut [adressée] à Zacharie, en disant:
Ndipo Yehova anayankhulanso ndi Zekariya kuti,
9 Ainsi avait parlé l'Eternel des armées, en disant: Faites ce qui est vraiment juste, et exercez la miséricorde et la compassion chacun envers son frère.
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Muziweruza molungama; muzichitirana chifundo ndi kumverana chisoni.
10 Et ne faites point de tort à la veuve, ni à l'orphelin, ni à l'étranger, ni à l'affligé, et ne méditez aucun mal dans vos cœurs chacun contre son frère.
Musamazunze akazi amasiye kapena ana amasiye, alendo kapena osauka. Musamaganizirane zoyipa mʼmitima mwanu.’
11 Mais ils n'y ont point voulu entendre, et ont tiré l'épaule en arrière, et ils ont appesanti leurs oreilles pour ne point ouïr.
“Koma makolo anu anakana kumvera uthenga umenewu; anawumitsa mtima nandifulatira, natseka makutu awo kuti asamve.
12 Et ils ont rendu leur cœur [dur comme] le diamant, pour ne point écouter la Loi, et les paroles que l'Eternel des armées envoyait par son Esprit, par le moyen des Prophètes qui ont été ci-devant; c'est pourquoi il y a eu une grande indignation de par l'Eternel des armées.
Anawumitsa mitima yawo ngati mwala wa sangalabwi ndipo sanamvere lamulo kapena mawu amene Yehova Wamphamvuzonse anawatumiza mwa Mzimu wake kudzera mwa aneneri oyamba aja. Kotero Yehova Wamphamvuzonse anakwiya kwambiri.
13 Et il est arrivé, que comme quand on leur a crié, ils n'ont point écouté; ainsi, quand ils ont crié, je n'ai point écouté, a dit l'Eternel des armées.
“‘Pamene ndinawayitana, iwo sanamvere; choncho pamene iwo anandiyitana, Ine sindinamverenso,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.
14 Et je les ai dispersés [comme] par un tourbillon parmi toutes les nations qu'ils ne connaissaient point, et le pays a été désolé après eux, tellement qu'il n'y a eu personne qui y passât, ni repassât, et on a mis le pays désirable en désolation.
‘Ndinawamwaza ndi kamvuluvulu pakati pa mitundu yonse ya anthu, kumene anali alendo. Dziko lawo linatsala litasakazidwa kwambiri kotero kuti palibe amene amabwera kapena kupitamo. Umu ndi mmene anasandutsira dziko labwino kukhala chipululu.’”