< Psaumes 96 >
1 Chantez à l'Eternel un nouveau cantique; vous toute la terre chantez à l'Eternel.
Imbirani Yehova nyimbo yatsopano; Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.
2 Chantez à l'Eternel, bénissez son Nom, prêchez de jour en jour sa délivrance.
Imbirani Yehova, tamandani dzina lake; lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.
3 Racontez sa gloire parmi les nations, [et] ses merveilles parmi tous les peuples.
Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko, ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.
4 Car l'Eternel [est] grand, et digne d'être loué; il [est] redoutable par-dessus tous les dieux;
Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda; ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.
5 Car tous les dieux des peuples [ne sont que des] idoles; mais l'Eternel a fait les cieux.
Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano, koma Yehova analenga mayiko akumwamba.
6 La majesté et la magnificence [marchent] devant lui; la force et l'excellence sont dans son sanctuaire.
Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake, mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.
7 Familles des peuples rendez à l'Eternel, rendez à l'Eternel la gloire et la force.
Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina, perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.
8 Rendez à l'Eternel la gloire due à son Nom; apportez l'oblation, et entrez dans ses parvis.
Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake; bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.
9 Prosternez-vous devant l'Eternel avec une sainte magnificence; vous tous les habitants de la terre tremblez tout étonnés, à cause de la présence de sa face.
Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake; njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.
10 Dites parmi les nations: l'Eternel règne; même la terre habitable est affermie, [et] elle ne sera point ébranlée; il jugera les peuples en équité.
Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.” Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe; Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.
11 Que les cieux se réjouissent, et que la terre s'égaye! Que la mer et ce qui est contenu en elle bruie!
Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere; nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;
12 Que les champs s'égayent, avec tout ce qui est en eux. Alors tous les arbres de la forêt chanteront de joie,
minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo. Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;
13 Au-devant de l'Eternel, parce qu'il vient, parce qu'il vient pour juger la terre; il jugera en justice le monde habitable, et les peuples selon sa fidélité.
idzayimba pamaso pa Yehova, pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi; adzaweruza dziko lonse mwachilungamo ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.