< Psaumes 78 >
1 Maskil d'Asaph. Mon peuple, écoute ma Loi, prêtez vos oreilles aux paroles de ma bouche.
Ndakatulo ya Asafu. Inu anthu anga imvani chiphunzitso changa; mvetserani mawu a pakamwa panga.
2 J'ouvrirai ma bouche en similitudes: je manifesterai les choses notables du temps d'autrefois.
Ndidzatsekula pakamwa panga mʼmafanizo, ndidzayankhula zinthu zobisika, zinthu zakalekale
3 Lesquelles nous avons ouïes et connues, et que nos pères nous on racontées.
zimene tinazimva ndi kuzidziwa, zimene makolo athu anatiwuza.
4 Nous ne les cèlerons point à leurs enfants, [et] ils raconteront à la génération à venir les louanges de l'Eternel, et sa force, et ses merveilles qu'il a faites.
Sitidzabisira ana awo, tidzafotokozera mʼbado wotsatira ntchito zotamandika za Yehova, mphamvu zake, ndi zozizwitsa zimene Iye wachita.
5 Car il a établi le témoignage en Jacob, et il a mis la Loi en Israël; et il donna charge à nos pères de les faire entendre à leurs enfants.
Iye anapereka mawu wodzichitira umboni kwa Yakobo ndi kukhazikitsa lamulo mu Israeli, zimene analamulira makolo athu kuphunzitsa ana awo,
6 Afin que la génération à venir, les enfants, [dis-je], qui naîtraient, les connut, [et] qu'ils se missent en devoir de les raconter à leurs enfants;
kotero kuti mʼbado wotsatira uthe kuzidziwa, ngakhale ana amene sanabadwe, ndi kuti iwo akafotokozere ana awonso.
7 Et afin qu'ils missent leur confiance en Dieu, et qu'ils n'oubliassent point les exploits du [Dieu] Fort, et qu'ils gardassent ses commandements.
Choncho iwo adzakhulupirira Mulungu ndipo sadzayiwala ntchito zake koma adzasunga malamulo ake.
8 Et qu'ils ne fussent point, comme leurs pères, une génération revêche et rebelle, une génération qui n'a point soumis son cœur, et l'esprit de laquelle n'a point été fidèle au [Dieu] Fort.
Iwo asadzakhale monga makolo awo, mʼbado wosamvera ndi wowukira, umene mitima yake inali yosamvera Mulungu, umene mizimu yake inali yosakhulupirika kwa Iye.
9 Les enfants d'Ephraïm armés entre les archers, ont tourné le dos le jour de la bataille.
Anthu a ku Efereimu, ngakhale ananyamula mauta, anathawabe pa nthawi ya nkhondo;
10 Ils n'ont point gardé l'alliance de Dieu, et ont refusé de marcher selon sa Loi.
iwo sanasunge pangano la Mulungu ndipo anakana kukhala mʼmoyo wotsatira lamulo lake.
11 Et ils ont mis en oubli ses exploits et ses merveilles qu'il leur avait fait voir.
Anayiwala zimene Iye anachita, zozizwitsa zimene anawaonetsa.
12 Il a fait des miracles en la présence de leurs pères au pays d'Egypte, au territoire de Tsohan.
Iyeyo anachita zodabwitsa makolo athu akuona, mʼdziko la Igupto, mʼchigawo cha Zowani.
13 Il a fendu la mer, et les a fait passer au travers, et il a fait arrêter les eaux comme un monceau [de pierre].
Anagawa nyanja pakati ndi kudutsitsapo iwowo, Iye anachititsa madzi kuyima chilili ngati khoma.
14 Et il les a conduits de jour par la nuée, et toute la nuit par une lumière de feu.
Anawatsogolera ndi mtambo masana ndi kuwala kwa moto usiku wonse.
15 Il a fendu les rochers au désert, et leur a donné abondamment à boire, comme [s'il eût puisé] des abîmes.
Iye anangʼamba miyala mʼchipululu ndi kuwapatsa madzi ochuluka ngati a mʼnyanja zambiri;
16 Il a fait, dis-je, sortir des ruisseaux de la roche, et en a fait découler des eaux comme des rivières.
Anatulutsa mitsinje kuchokera mʼmingʼalu ya miyala ndi kuyenda madzi ngati mitsinje.
17 Toutefois ils continuèrent à pécher contre lui, irritant le Souverain au désert.
Komabe iwowo anapitiriza kumuchimwira Iye, kuwukira Wammwambamwamba mʼchipululu.
18 Et ils tentèrent le [Dieu] Fort dans leurs cœurs, en demandant de la viande qui flattât leur appétit.
Ananyoza Mulungu mwadala pomuwumiriza kuti awapatse chakudya chimene anachilakalaka.
19 Ils parlèrent contre Dieu, disant: le [Dieu] Fort nous pourrait-il dresser une table en ce désert?
Iwo anayankhula motsutsana naye ponena kuti, “Kodi Mulungu angatipatse chakudya mʼchipululu?
20 Voilà, [dirent-ils], il a frappé le rocher, et les eaux en sont découlées, et il en est sorti des torrents abondamment, mais pourrait-il aussi nous donner du pain? apprêterait-il bien de la viande à son peuple?
Iye atamenya thanthwe madzi anatuluka, ndipo mitsinje inadzaza ndi madzi. Koma iye angatipatsenso ife chakudya? Kodi angapereke nyama kwa anthu akewa?”
21 C'est pourquoi l'Eternel les ayant ouïs, se mit en grande colère, et le feu s'embrasa contre Jacob, et sa colère s'excita contre Israël.
Yehova atawamva anakwiya kwambiri; moto wake unayaka kutsutsana ndi Yakobo, ndipo mkwiyo wake unauka kutsutsana ndi Israeli,
22 Parce qu'ils n'avaient point cru en Dieu, et ne s'étaient point confiés en sa délivrance.
pakuti iwo sanakhulupirire Mulungu kapena kudalira chipulumutso chake.
23 Bien qu'il eût donné commandement aux nuées d'en haut, et qu'il eût ouvert les portes des cieux;
Komabe Iye anapereka lamulo kwa mitambo mmwamba ndi kutsekula makomo a mayiko akumwamba;
24 Et qu'il eût fait pleuvoir la manne sur eux afin qu'ils en mangeassent, et qu'il leur eût donné le froment des cieux;
anagwetsa mana kuti anthu adye, anawapatsa tirigu wakumwamba.
25 Tellement que chacun mangeait du pain des puissants. Il leur envoya donc de la viande pour s'en rassasier.
Anthu anadya buledi wa angelo, Iye anawatumizira chakudya chonse chimene akanatha kudya.
26 Il excita dans les cieux le vent d'Orient, et il amena par sa force le vent du midi.
Anamasula mphepo ya kummwera kuchokera kumwamba, ndi kutsogolera mphepo ya kummwera mwa mphamvu zake.
27 Et il fit pleuvoir sur eux de la chair comme de la poussière, et des oiseaux volants, en une quantité pareille au sable de la mer.
Iye anawagwetsera nyama ngati fumbi, mbalame zowuluka ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja.
28 Et il la fit tomber au milieu de leur camp, [et] autour de leurs pavillons.
Anazibweretsa kwa iwo mʼkati mwa misasa yawo, kuzungulira matenti awo onse.
29 Et ils en mangèrent, et en furent pleinement rassasiés, car il avait accompli leur souhait.
Iwo anadya mpaka anatsala nazo zochuluka pakuti Iye anawapatsa zimene anazilakalaka.
30 [Mais] ils n'en avaient pas encore perdu l'envie, et leur viande était encore dans leur bouche.
Koma iwowo anasiya kudya chakudya anachilakalakacho, chakudya chili mʼkamwa mwawobe,
31 Quand la colère de Dieu s'excita contre eux, et qu'il mit à mort les gras d'entre eux, et abattit les gens d'élite d'Israël.
mkwiyo wa Mulungu unawayakira; Iye anapha amphamvu onse pakati pawo, kugwetsa anyamata abwino kwambiri mu Israeli.
32 Nonobstant cela, ils péchèrent encore, et n'ajoutèrent point de foi à ses merveilles.
Ngakhale zinali chomwechi, iwo anapitirira kuchimwa; ngakhale anaona zozizwitsa zakezo iwowo sanakhulupirirebe.
33 C'est pourquoi il consuma soudainement leurs jours, et leurs années promptement.
Kotero Mulungu anachepetsa masiku awo kuti azimirire ngati mpweya. Iye anachepetsa zaka zawo kuti zithere mʼmasautso.
34 Quand il les mettait à mort, alors ils le recherchaient, ils se repentaient, et ils cherchaient le [Dieu] Fort dès le matin.
Mulungu atawapha, iwo amamufunafuna Iyeyo; iwo ankatembenukiranso kwa Iye mwachangu.
35 Et ils se souvenaient que Dieu était leur rocher, et que le [Dieu] Fort et Souverain était celui qui les délivrait.
Ankakumbukira kuti Mulungu ndiye Thanthwe lawo, kuti Mulungu Wammwambamwamba ndiye Mpulumutsi wawo.
36 Mais ils faisaient beau semblant de leur bouche, et ils lui mentaient de leur langue;
Komabe ankamuthyasika ndi pakamwa pawo, kumunamiza ndi malilime awo;
37 Car leur cœur n'était point droit envers lui, et ils ne furent point fidèles en son alliance.
Mitima yawo sinali yokhazikika pa Iye, iwo sanakhulupirike ku pangano lake.
38 Toutefois, comme il est pitoyable, il pardonna leur iniquité, tellement qu'il ne les détruisit point, mais il apaisa souvent sa colère, et n'émut point toute sa fureur.
Komabe Iye anali wachifundo; anakhululukira mphulupulu zawo ndipo sanawawononge. Nthawi ndi nthawi Iye anabweza mkwiyo wake ndipo sanawutse ukali wake wonse.
39 Et il se souvint qu'ils n'étaient que chair, qu'un vent qui passe, et qui ne revient point.
Iye anakumbukira kuti iwo anali anthu chabe, mphepo yopita imene sibwereranso.
40 Combien de fois l'ont-ils irrité au désert, et combien de fois l'ont-ils ennuyé dans ce lieu inhabitable?
Nthawi zambiri iwo ankamuwukira Iye mʼchipululu ndi kumumvetsa chisoni mʼdziko lopanda kanthu!
41 Car coup sur coup ils tentaient le [Dieu] Fort; et bornaient le Saint d'Israël.
Kawirikawiri iwo ankamuyesa Mulungu; ankamuputa Woyera wa Israeli.
42 Ils ne se sont point souvenus de sa main, ni du jour qu'il les avait délivrés de la main de celui qui les affligeait.
Sanakumbukire mphamvu zake, tsiku limene Iye anawawombola kwa ozunza,
43 [Ils ne se sont point souvenus] de celui qui avait fait ses signes en Egypte, et ses miracles au territoire de Tsohan:
tsiku limene Iyeyo anaonetsa poyera zizindikiro zozizwitsa zake mu Igupto, zozizwitsa zake mʼchigawo cha Zowani.
44 Et qui avait changé en sang leurs rivières et leurs ruisseaux, afin qu'ils n'en pussent point boire.
Iye anasandutsa mitsinje yawo kukhala magazi; Iwo sanathe kumwa madzi ochokera mʼmitsinje yawo.
45 Et qui avait envoyé contre eux une mêlée de bêtes, qui les mangèrent; et des grenouilles, qui les détruisirent.
Iye anawatumizira magulu a ntchentche zimene zinawawononga, ndiponso achule amene anawasakaza.
46 Et qui avait donné leurs fruits aux vermisseaux, et leur travail aux sauterelles.
Iye anapereka mbewu zawo kwa ziwala, zokolola zawo kwa dzombe.
47 Qui avait détruit leurs vignes par la grêle, et leurs sycomores par les orages.
Iye anawononga mphesa zawo ndi matalala ndiponso mitengo yawo yankhuyu ndi chisanu.
48 Et qui avait livré leur bétail à la grêle, et leurs troupeaux aux foudres étincelantes.
Iye anapereka ngʼombe zawo ku matalala, zoweta zawo ku zingʼaningʼani.
49 Qui avait envoyé sur eux l'ardeur de sa colère, grande colère, indignation et détresse, [qui sont] un envoi de messagers de maux.
Anakhuthula moto wa ukali wake pa iwo, anawapsera mtima nawakwiyira nʼkuwabweretsera masautso. Zimenezi zinali ngati gulu la angelo osakaza.
50 Qui avait dressé le chemin à sa colère, et n'avait point retiré leur âme de la mort; et qui avait livré leur bétail à la mortalité.
Analolera kukwiya, sanawapulumutse ku imfa koma anawapereka ku mliri.
51 Et qui avait frappé tout premier-né en Egypte, les prémices de la vigueur dans les tentes de Cam.
Anakantha ana oyamba kubadwa a Igupto, zipatso zoyamba kucha za mphamvu zawo mʼmatenti a Hamu
52 Qui avait fait partir son peuple comme des brebis; et qui l'avait mené par le désert comme un troupeau.
Koma Iye anatulutsa anthu ake ngati ziweto; anawatsogolera ngati nkhosa kudutsa mʼchipululu.
53 Et qui les avait conduits sûrement, et sans qu ils eussent aucune frayeur, là où la mer couvrit leurs ennemis.
Anawatsogolera bwinobwino kotero kuti analibe mantha koma nyanja inamiza adani awo.
54 Et qui les avait introduits en la contrée de sa Sainteté, [savoir] en cette montagne que sa droite a conquise.
Kotero anawafikitsa ku malire a dziko lake loyera, ku dziko lamapiri limene dzanja lake lamanja linawatengera.
55 Et qui avait chassé de devant eux les nations qu'il leur a fait tomber en lot d'héritage, et avait fait habiter les Tribus d'Israël dans les tentes de ces nations.
Iye anathamangitsa mitundu ya anthu patsogolo pawo ndipo anapereka mayiko awo kwa Aisraeli kuti akhale awo; Iye anakhazikitsa mafuko a Israeli mʼnyumba zawo.
56 Mais ils ont tenté et irrité le Dieu Souverain, et n'ont point gardé ses témoignages.
Koma iwo anayesa Mulungu ndi kuwukira Wammwambamwamba; sanasunge malamulo ake.
57 Et ils se sont retirés en arrière, et se sont portés infidèlement, ainsi que leurs pères; ils se sont renversés comme un arc qui trompe.
Anakhala okanika ndi osakhulupirika monga makolo awo, anapotoka monga uta wosakhulupirika.
58 Et ils l'ont provoqué à la colère par leurs hauts lieux, et l'ont ému à la jalousie par leurs images taillées.
Anakwiyitsa Iyeyo ndi malo awo opembedzera mafano; anawutsa nsanje yake ndi mafano awo.
59 Dieu l'a ouï, et s'est mis en grande colère, et il a fort méprisé Israël.
Pamene Mulungu anamva zimenezi, anakwiya kwambiri; Iye anakana Israeli kwathunthu.
60 Et il a abandonné le pavillon de Silo, le Tabernacle où il habitait entre les hommes.
Anasiya nyumba ya ku Silo, tenti imene Iyeyo anayimanga pakati pa anthu.
61 Et il a livré en captivité sa force et son ornement entre les mains de l'ennemi.
Anatumiza mphamvu zake ku ukapolo, ulemerero wake mʼmanja mwa adani.
62 Et il a livré son peuple à l'épée et s'est mis en grande colère contre son héritage.
Anapereka anthu ake ku lupanga; anakwiya kwambiri ndi cholowa chake.
63 Le feu a consumé leurs gens d'élite, et leurs vierges n'ont point été louées.
Moto unanyeketsa anyamata awo, ndipo anamwali awo analibe nyimbo za ukwati;
64 Leurs Sacrificateurs sont tombés par l'épée, et leurs veuves ne les ont point pleuré.
ansembe awo anaphedwa ndi lupanga, ndipo amayi awo amasiye sanathe kulira.
65 Puis le Seigneur s'est réveillé comme un homme qui se serait endormi, et comme un puissant homme qui s'écrie ayant encore le vin dans la tête.
Kenaka Ambuye anakhala ngati akudzuka kutulo, ngati munthu wamphamvu wofuwula chifukwa cha vinyo.
66 Et il a frappé ses adversaires par derrière, et les a mis en opprobre perpétuel.
Iye anathamangitsa adani ake; anawachititsa manyazi ku nthawi zonse.
67 Mais il a dédaigné le Tabernacle de Joseph, et n'a point choisi la Tribu d'Ephraïm.
Kenaka Iye anakana matenti a Yosefe, sanasankhe fuko la Efereimu;
68 Mais il a choisi la Tribu de Juda, la montagne de Sion, laquelle il aime;
Koma anasankha fuko la Yuda, phiri la Ziyoni limene analikonda.
69 Et il a bâti son Sanctuaire comme [des bâtiments] haut élevés, et l'a établi comme la terre qu'il a fondée pour toujours.
Iye anamanga malo ake opatulika ngati zitunda, dziko limene analikhazikitsa kwamuyaya.
70 Et il a choisi David, son serviteur, et l'a pris des parcs des brebis;
Anasankha Davide mtumiki wake ndi kumuchotsa pakati pa makola ankhosa;
71 [Il l'a pris, dis-je, ] d'après les brebis qui allaitent, et l'a amené pour paître Jacob son peuple, et Israël son héritage.
kuchokera koyangʼanira nkhosa anamubweretsa kuti akhale mʼbusa wa anthu ake, Yakobo, wa Israeli cholowa chake.
72 Aussi les a-t-il fait repus selon l'intégrité de son cœur, et conduits par la sage direction de ses mains.
Ndipo Davide anawaweta ndi mtima wolungama; ndi manja aluso anawatsogolera.