< Psaumes 70 >

1 Psaume de David, pour faire souvenir, [donné] au maître chantre. Ô Dieu! [hâte-toi] de me délivrer; ô Dieu! hâte-toi de venir à mon secours.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Pempho. Fulumirani Mulungu kundipulumutsa; Yehova bwerani msanga kudzandithandiza.
2 Que ceux qui cherchent mon âme soient honteux et rougissent; et que ceux qui prennent plaisir à mon mal soient repoussés en arrière, et soient confus.
Iwo amene akufunafuna moyo wanga achititsidwe manyazi ndi kusokonezedwa; onse amene akukhumba chiwonongeko changa abwezedwe mopanda ulemu.
3 Que ceux qui disent: Aha! Aha! retournent en arrière pour la récompense de la honte qu'ils m'ont faite.
Onse amene akunena kwa ine kuti, “Aha, aha,” abwerere chifukwa cha manyazi awo.
4 Que tous ceux qui te cherchent s'égayent et se réjouissent en toi; et que ceux qui aiment ta délivrance, disent toujours: Magnifié soit Dieu!
Koma onse amene akufunafuna Inu akondwere ndi kusangalala mwa Inu; iwo amene amakonda chipulumutso chanu nthawi zonse anene kuti, “Mulungu akuzike!”
5 Or je suis affligé et misérable; ô Dieu! hâte-toi de venir vers moi; tu es mon secours et mon libérateur; ô Eternel! ne tarde point.
Koma ine ndine wosauka ndi wosowa; bwerani msanga kwa ine Inu Mulungu. Inu ndinu thandizo langa ndi momboli wanga; Inu Yehova musachedwe.

< Psaumes 70 >