< Psaumes 68 >
1 Psaume de Cantique, de David, [donné] au maître chantre. Que Dieu se lève, et ses ennemis seront dispersés, et ceux qui le haïssent s'enfuiront de devant lui.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Adzuke Mulungu, adani ake amwazikane; adani ake athawe pamaso pake.
2 Tu les chasseras comme la fumée est chassée [par le vent]; comme la cire se fond devant le feu, [ainsi] les méchants périront devant Dieu.
Monga momwe mphepo imachotsera utsi; Inu muwawulutsire kutali. Monga phula limasungunukira pa moto, oyipa awonongeke pamaso pa Mulungu.
3 Mais les justes se réjouiront et s'égayeront devant Dieu, et tressailliront de joie.
Koma olungama asangalale ndi kukondwera pamaso pa Mulungu; iwo akondwere ndi kusangalala.
4 Chantez à Dieu, psalmodiez son Nom, exaltez celui qui est monté sur les cieux; son Nom, est l'Eternel; et égayez-vous en sa présence.
Imbirani Mulungu imbirani dzina lake matamando, mukwezeni Iye amene amakwera pa mitambo; dzina lake ndi Yehova ndipo sangalalani pamaso pake.
5 Il est le père des orphelins, et le juge des veuves; Dieu est dans la demeure de sa Sainteté.
Atate wa ana amasiye, mtetezi wa akazi amasiye, ndiye Mulungu amene amakhala mʼmalo oyera.
6 Dieu fait habiter en famille ceux qui étaient seuls; il délivre ceux qui étaient enchaînés, mais les revêches demeurent en une terre déserte.
Mulungu amakhazikitsa mtima pansi osungulumwa mʼmabanja, amatsogolera amʼndende ndi kuyimba; koma anthu osamvera amakhala ku malo owuma a dziko lapansi.
7 Ô Dieu! Quand tu sortis devant ton peuple, quand tu marchais par le désert; (Sélah)
Pamene munatuluka kutsogolera anthu anu, Inu Mulungu, pamene munayenda kudutsa chipululu,
8 La terre trembla, et les cieux répandirent leurs eaux à cause de la présence de Dieu, ce mont de Sinaï [trembla] à cause de la présence de Dieu, du Dieu d'Israël.
dziko lapansi linagwedezeka, miyamba inakhuthula pansi mvula, pamaso pa Mulungu, Mmodzi uja wa ku Sinai. Pamaso pa Mulungu, Mulungu wa Israeli.
9 Ô Dieu! tu as fait tomber une pluie abondante sur ton héritage; et quand il était las, tu l'as rétabli.
Munapereka mivumbi yochuluka, Inu Mulungu; munatsitsimutsa cholowa chanu cholefuka.
10 Ton troupeau s'y est tenu. Tu accommodes de tes biens celui qui est affligé, ô Dieu!
Anthu anu anakhala mʼmenemo ndipo munapatsa anthu osauka zimene zinkawasowa chifukwa cha ubwino wanu Mulungu.
11 Le Seigneur a donné de quoi parler; les messagers de bonnes nouvelles ont été une grande armée.
Ambuye analengeza mawu, ndipo gulu linali lalikulu la iwo amene anapita kukawafalitsa;
12 Les Rois des armées s'en sont fuis, ils s'en sont fuis, et celle qui se tenait à la maison a partagé le butin.
“Mafumu ndi ankhondo anathawa mwaliwiro; mʼmisasa anthu anagawana zolanda pa nkhondo.
13 Quand vous auriez couché entre les chenets arrangés, [vous serez comme] les ailes d'un pigeon couvert d'argent, et dont les ailes sont [comme] la couleur jaune du fin or.
Ngakhale mukugona pakati pa makola a ziweto, mapiko a nkhunda akutidwa ndi siliva, nthenga zake ndi golide wonyezimira.”
14 Quand le Tout-puissant dissipa les Rois en cet [héritage], il devint blanc, comme la neige qui est en Tsalmon.
Pamene Wamphamvuzonse anabalalitsa mafumu mʼdziko, zinali ngati matalala akugwa pa Zalimoni.
15 La montagne de Dieu est un mont de Basan; une montagne élevée, un mont de Basan.
Mapiri a Basani ndi mapiri aulemerero; mapiri a Basani, ndi mapiri a msonga zambiri.
16 Pourquoi lui insultez-vous, montagnes dont le sommet est élevé? Dieu a désiré cette montagne pour y habiter, et l'Eternel y demeurera à jamais.
Muyangʼaniranji mwansanje inu mapiri a msonga zambiri, pa phiri limene Mulungu analisankha kuti azilamulira, kumene Yehova mwini adzakhalako kwamuyaya?
17 La chevalerie de Dieu [se compte par] vingt-mille, par des milliers redoublés; le Seigneur est au milieu d'eux; c'est un Sinaï en Sainteté.
Magaleta a Mulungu ndi osawerengeka, ndi miyandamiyanda; Ambuye wabwera kuchokera ku Sinai, walowa mʼmalo ake opatulika.
18 Tu es monté en haut, tu as mené captifs les prisonniers, tu as pris des dons [pour les distribuer] entre les hommes, et même entre les rebelles, afin qu'ils habitent [dans le lieu] de l'Eternel Dieu.
Pamene Inu munakwera mmwamba, munatsogolera a mʼndende ambiri; munalandira mphatso kuchokera kwa anthu, ngakhale kuchokera kwa owukira, kuti Inu Mulungu, mukhale kumeneko.
19 Béni soit le Seigneur, qui tous les jours nous comble de ses biens; le [Dieu] Fort est notre délivrance; (Sélah)
Matamando akhale kwa Ambuye, kwa Mulungu Mpulumutsi wathu amene tsiku ndi tsiku amasenza zolemetsa zathu.
20 Le [Dieu] Fort nous est un [Dieu] Fort pour nous délivrer, et les issues de la mort sont à l'Eternel le Seigneur.
Mulungu wathu ndi Mulungu amene amapulumutsa; Ambuye Wamphamvuzonse ndiye amene amatipulumutsa ku imfa.
21 Certainement Dieu écrasera la tête de ses ennemis, le sommet de la tête chevelue de celui qui marche dans ses vices.
Ndithu Mulungu adzaphwanya mitu ya adani ake, zipewa za ubweya za iwo amene amapitiriza kuchita machimo awo.
22 Le Seigneur a dit: je ferai retourner [les miens] de Basan, je les ferai retourner du fond de la mer.
Ambuye akunena kuti, “Ndidzawabweretsa kuchokera ku Basani; ndidzawabweretsa kuchokera ku nyanja zozama.
23 Afin que ton pied et la langue de tes chiens s'enfoncent dans le sang des ennemis, [dans le sang] de chacun d'eux.
Kuti muviyike mapazi anu mʼmagazi a adani anu, pamene malilime a agalu anu akudyapo gawo lawo.”
24 Ô Dieu! Ils ont vu tes démarches dans le lieu saint, les démarches de mon [Dieu] Fort, mon Roi.
Mayendedwe aulemu a anthu anu aonekera poyera, Inu Mulungu; mayendedwe olemekeza Mulungu wanga ndi Mfumu yanga yokalowa mʼmalo opatulika.
25 Les chantres allaient devant, ensuite les joueurs d'instruments, [et] au milieu les jeunes filles, jouant du tambour.
Patsogolo pali oyimba nyimbo pakamwa, pambuyo pawo oyimba nyimbo ndi zipangizo; pamodzi ndi iwo pali atsikana akuyimba matambolini.
26 Bénissez Dieu dans les assemblées, [bénissez] le Seigneur, vous qui êtes de la source d'Israël.
Tamandani Mulungu mu msonkhano waukulu; tamandani Yehova mu msonkhano wa Israeli.
27 Là Benjamin le petit a dominé sur eux; les principaux de Juda ont été leur accablement de pierres: [là ont dominé] les principaux de Zabulon, [et] les principaux de Nephthali.
Pali fuko lalingʼono la Benjamini, kuwatsogolera, pali gulu lalikulu la ana a mafumu a Yuda, ndiponso pali ana a mafumu a Zebuloni ndi Nafutali.
28 Ton Dieu a ordonné ta force. Donne force, ô Dieu; c'est toi qui nous as fait ceci.
Kungani mphamvu zanu Mulungu; tionetseni nyonga zanu, Inu Mulungu, monga munachitira poyamba.
29 Dans ton Temple, à Jérusalem, les Rois t'amèneront des présents.
Chifukwa cha Nyumba yanu ku Yerusalemu, mafumu adzabweretsa kwa Inu mphatso.
30 Tance rudement les bêtes sauvages des roseaux, l'assemblée des forts taureaux, et les veaux des peuples, [et] ceux qui se montrent parés de lames d'argent. Il a dissipé les peuples qui ne demandent que la guerre.
Dzudzulani chirombo pakati pa mabango, gulu la ngʼombe zazimuna pakati pa ana angʼombe a mitundu ya anthu. Mochititsidwa manyazi, abweretse mitanda ya siliva. Balalitsani anthu a mitundu ina amene amasangalatsidwa ndi nkhondo.
31 De grands Seigneurs viendront d'Egypte; Cus se hâtera d'étendre ses mains vers Dieu.
Nthumwi zidzachokera ku Igupto; Kusi adzadzipereka yekha kwa Mulungu.
32 Royaumes de la terre, chantez à Dieu, psalmodiez au Seigneur; (Sélah)
Imbirani Mulungu Inu mafumu a dziko lapansi imbirani Ambuye matamando. (Sela)
33 [Psalmodiez] à celui qui est monté dans les cieux des cieux qui sont d'ancienneté; voilà, il fait retentir de sa voix un son véhément.
Kwa Iye amene amakwera pa mitambo yakalekale ya mmwamba amene amabangula ndi mawu amphamvu.
34 Attribuez la force à Dieu; sa magnificence est sur Israël, et sa force est dans les nuées.
Lengezani za mphamvu za Mulungu, amene ulemerero wake uli pa Israeli amene mphamvu zake zili mʼmitambo.
35 Ô Dieu! Tu es redouté à cause de tes Sanctuaires. Le [Dieu] Fort d'Israël est celui qui donne la force et la puissance à son peuple; Béni soit Dieu!
Ndinu woopsa, Inu Mulungu mʼmalo anu opatulika; Mulungu wa Israeli amapereka mphamvu ndi nyonga kwa anthu ake. Matamando akhale kwa Mulungu!