< Psaumes 60 >

1 Mictam de David, [propre] pour enseigner, [et donné] au maître chantre, [pour le chanter] sur Susan-heduth. Touchant la guerre qu'il eut contre la Syrie de Mésopotamie, et contre la Syrie de Tsoba; et touchant ce que Joab retournant défit douze mille Iduméens dans la vallée du sel. Ô Dieu! tu nous as rejetés, tu nous as dispersés, tu t'es courroucé; retourne-toi vers nous.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere. Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza. Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!
2 Tu as ébranlé la terre, et l'as mise en pièces; répare ses fractures, car elle est affaissée.
Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba, konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.
3 Tu as fait voir à ton peuple des choses dures, tu nous as abreuvés de vin d'étourdissement.
Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto; inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.
4 [Mais depuis] tu as donné une bannière à ceux qui te craignent, afin de l'élever en haut pour l'amour de ta vérité; (Sélah)
Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera kuti tisonkhanireko pothawa uta.
5 Afin que ceux que tu aimes soient délivrés. Sauve-moi par ta droite, et exauce-moi.
Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja, kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.
6 Dieu a parlé dans son Sanctuaire; je me réjouirai; je partagerai Sichem, et je mesurerai la vallée de Succoth.
Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika: “Mwakupambana ndidzagawa Sekemu ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.
7 Galaad sera à moi, Manassé aussi sera à moi, et Ephraïm sera la force de mon chef, Juda sera mon législateur.
Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso; Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera, Yuda ndi ndodo yanga yaufumu
8 Moab sera le bassin où je me laverai; je jetterai mon soulier à Edom; Ô Palestine, triomphe à cause de moi.
Mowabu ndi mbale yanga yosambira, pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga, pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”
9 Qui sera-ce qui me conduira en la ville munie? Qui sera-ce qui me conduira jusques en Edom?
Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa? Ndani adzanditsogolera ku Edomu?
10 Ne sera-ce pas toi, ô Dieu! qui nous avais rejetés, et qui ne sortais plus, ô Dieu! avec nos armées.
Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.
11 Donne-nous du secours [pour sortir] de détresse; car la délivrance [qu'on attend] de l'homme est vanité.
Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu, pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.
12 Nous ferons des actions de valeur [avec le secours de] Dieu, et il foulera nos ennemis.
Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano ndipo tidzapondaponda adani athu.

< Psaumes 60 >