< Psaumes 58 >
1 Mictam de David, [donné] au maître chantre, [pour le chanter] sur Al-tasheth. En vérité, vous gens de l'assemblée, prononcez-vous ce qui est juste? Vous fils des hommes, jugez-vous avec droiture.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama? Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?
2 Au contraire, vous tramez des injustices dans votre cœur; vous balancez la violence de vos mains en la terre.
Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama, ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.
3 Les méchants se sont égarés dès la matrice, ils ont erré dès le ventre [de leur mère], en parlant faussement.
Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera; kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.
4 Ils ont un venin semblable au venin du serpent, [et] ils sont comme l'aspic sourd, qui bouche son oreille;
Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka, ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.
5 Qui n'écoute point la voix des enchanteurs, [la voix] du charmeur fort expert en charmes.
Imene simva liwu la munthu wamatsenga, ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.
6 Ô Dieu, brise-leur les dents dans leur bouche! Eternel, romps les dents mâchelières des lionceaux.
Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu, Yehova khadzulani mano a mikango!
7 Qu'ils s'écoulent comme de l'eau, et qu'ils se fondent! que [chacun d'eux] bande [son arc, mais] que ses flèches soient comme si elles étaient rompues!
Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.
8 Qu'il s'en aille comme un limaçon qui se fond! qu'ils ne voient point le soleil non plus que l'avorton d'une femme!
Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda; ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.
9 Avant que vos chaudières aient senti le feu des épines, l'ardeur de la colère, semblable à un tourbillon, enlèvera [chacun d'eux] comme de la chair crue.
Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku, kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.
10 Le juste se réjouira quand il aura vu la vengeance; il lavera ses pieds au sang du méchant.
Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango, pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.
11 Et chacun dira: quoi qu'il en soit, il y a une récompense pour le juste; quoi qu'il en soit, il y a un Dieu qui juge en la terre.
Ndipo anthu adzanena kuti, “Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho; zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”