< Psaumes 147 >

1 Louez l'Eternel; car c'est une chose bonne de psalmodier à notre Dieu, car c'est une chose agréable; [et] la louange en est bienséante.
Tamandani Yehova. Nʼkwabwino kwambiri kuyimba nyimbo zamatamando kwa Mulungu wathu, nʼkokondweretsa ndi koyenera kumutamanda!
2 L'Eternel est celui qui bâtit Jérusalem; il rassemblera ceux d'Israël qui sont dispersés çà et là.
Yehova akumanga Yerusalemu; Iye akusonkhanitsa amʼndende a Israeli.
3 Il guérit ceux qui sont brisés de cœur, et il bande leurs plaies.
Akutsogolera anthu osweka mtima ndi kumanga mabala awo.
4 Il compte le nombre des étoiles; il les appelle toutes par leur nom.
Amadziwa chiwerengero cha nyenyezi, ndipo iliyonse amayitchula dzina.
5 Notre Seigneur est grand et d'une grande puissance, son intelligence est incompréhensible.
Yehova ndi wamkulu ndi wamphamvu kwambiri; nzeru zake zilibe malire.
6 L'Eternel maintient les débonnaires, [mais] il abaisse les méchants jusqu’en terre.
Yehova amagwiriziza anthu odzichepetsa, koma amagwetsa pansi anthu oyipa.
7 Chantez à l'Eternel avec action de grâces, vous entre-répondant les uns aux autres; psalmodiez avec la harpe à notre Dieu;
Imbirani Yehova ndi mayamiko; imbani nyimbo kwa Mulungu ndi pangwe.
8 Qui couvre de nuées les cieux; qui apprête la pluie pour la terre; qui fait produire le foin aux montagnes;
Iye amaphimba mlengalenga ndi mitambo; amapereka mvula ku dziko lapansi ndi kumeretsa udzu mʼmapiri.
9 Qui donne la pâture au bétail, et aux petits du corbeau, qui crient.
Iye amapereka chakudya kwa ngʼombe ndi kwa ana a makwangwala pamene akulira chakudya.
10 Il ne prend point de plaisir en la force du cheval; il ne fait point cas des jambières de l'homme.
Chikondwerero chake sichili mʼmphamvu za kavalo, kapena mʼmiyendo ya anthu amphamvu.
11 L'Eternel met son affection en ceux qui le craignent, en ceux qui s'attendent à sa bonté.
Yehova amakondwera ndi amene amamuopa, amene chiyembekezo chawo chili mʼchikondi chake chosasinthika.
12 Jérusalem, loue l'Eternel; Sion, loue ton Dieu.
Lemekeza Yehova, iwe Yerusalemu; tamanda Mulungu wako, iwe Ziyoni,
13 Car il a renforcé les barres de tes portes; il a béni tes enfants au milieu de toi.
pakuti Iye amalimbitsa mipiringidzo ya zipata zako ndi kudalitsa anthu ako mwa iwe.
14 C'est lui qui rend paisibles tes contrées, et qui te rassasie de la mœlle du froment.
Iye amabweretsa mtendere mʼmalire mwako ndi kukukhutitsa ndi ufa wa tirigu wosalala.
15 C'est lui qui envoie sa parole sur la terre, [et] sa parole court avec beaucoup de vitesse.
Iyeyo amapereka lamulo pa dziko lapansi; mawu ake amayenda mwaliwiro.
16 C'est lui qui donne la neige comme [des flocons] de laine, et qui répand la bruine comme de la cendre.
Amagwetsa chisanu ngati ubweya ndi kumwaza chipale ngati phulusa.
17 C'est lui qui jette sa glace comme par morceaux; et qui est-ce qui pourra durer devant sa froidure?
Amagwetsa matalala ngati miyala. Kodi ndani angathe kupirira kuzizira kwake?
18 Il envoie sa parole, et les fait fondre; il fait souffler son vent, [et] les eaux s'écoulent.
Amatumiza mawu ake ndipo chisanucho chimasungunuka; amawombetsa mphepo ndipo madzi amayenda.
19 Il déclare ses paroles à Jacob, et ses statuts et ses ordonnances à Israël.
Iye anawulula mawu ake kwa Yakobo, malamulo ake ndi zophunzitsa zake kwa Israeli.
20 Il n'a pas fait ainsi à toutes les nations, c'est pourquoi elles ne connaissent point ses ordonnances. Louez l'Eternel.
Sanachitepo zimenezi kwa mtundu wina uliwonse wa anthu; anthu enawo sadziwa malamulo ake. Tamandani Yehova.

< Psaumes 147 >