< Psaumes 122 >

1 Cantique de Mahaloth, de David. Je me suis réjoui à cause de ceux qui me disaient: nous irons à la maison de l'Eternel.
Salimo la Davide. Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Ndinakondwera atandiwuza kuti, “Tiyeni ku nyumba ya Yehova.”
2 Nos pieds se sont arrêté en tes portes, ô Jérusalem!
Mapazi athu akuyima mʼzipata zako, Iwe Yerusalemu.
3 Jérusalem, qui est bâtie comme une ville dont les habitants sont fort unis,
Yerusalemu anamangidwa ngati mzinda umene uli wothithikana pamodzi.
4 A laquelle montent les Tribus, les Tribus de l'Eternel, ce qui est un témoignage à Israël, pour célébrer le Nom de l’Eternel.
Kumeneko ndiye kumene kumapita mafuko, mafuko a Yehova, umboni wa kwa Israeli, kuti atamande dzina la Yehova.
5 Car c'est là qu'ont été posés les sièges pour juger, les sièges, [dis-je], de la maison de David.
Kumeneko anayikako mipando yaufumu yachiweruzo, mipando yaufumu ya nyumba ya Davide.
6 Priez pour la paix de Jérusalem; que ceux qui t'aiment jouissent de la prospérité.
Pemphererani mtendere wa Yerusalemu: “Iwo amene amakukonda iwe zinthu ziwayendere bwino.
7 Que la paix soit à ton avant-mur, et la prospérité dans tes palais.
Mukhale mtendere mʼkati mwa makoma ako, ndipo mʼnyumba zako zaufumu mukhale chitetezo.”
8 Pour l'amour de mes frères et de mes amis, je prierai maintenant pour ta paix.
Chifukwa cha abale anga ndi abwenzi anga ndidzati, “Mtendere ukhale mʼkati mwako.”
9 A cause de la maison de l'Eternel notre Dieu je procurerai ton bien.
Chifukwa cha Nyumba ya Yehova Mulungu wathu, ndidzakufunira zabwino.

< Psaumes 122 >