< Psaumes 111 >
1 Louez l'Eternel. [Aleph] Je célébrerai l'Eternel de tout mon cœur, [Beth.] dans la compagnie des hommes droits, et dans l'assemblée.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 [Guimel.] Les œuvres de l'Eternel sont grandes, [Daleth.] Elles sont recherchées de tous ceux qui y prennent plaisir.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 [He.] Son œuvre n'est que majesté et magnificence, [Vau.] et sa justice demeure à perpétuité.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 [Zaïn.] Il a rendu ses merveilles mémorables. [Heth.] L'Eternel est miséricordieux et pitoyable.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 [Tet.] Il a donné à vivre à ceux qui le craignent; [Jod.] il s'est souvenu à toujours de son alliance.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 [Caph.] Il a manifesté à son peuple la force de ses œuvres, [Lamed.] en leur donnant l'héritage des nations.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 [Mem.] Les œuvres de ses mains ne sont que vérité et équité; [Nun.] tous ses commandements sont véritables;
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 [Samech.] Appuyés à perpétuité et à toujours, [Hajin.] étant faits avec fidélité et droiture.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 [Pe.] Il a envoyé la rédemption à son peuple; [Tsade.] il lui a donné une alliance éternelle; [Koph.] son nom est saint et terrible.
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 [Resh.] Ce qu'il y a de capital dans la sagesse c'est la crainte de l'Eternel: [Scin.] tous ceux qui s'adonnent à faire ce qu'elle prescrit sont bien sages; [Thau.] sa louange demeure à perpétuité.
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.