< Psaumes 109 >
1 Psaume de David, [donné] au maître chantre. Ô Dieu de ma louange, ne te tais point.
Kwa mtsogoleri wamayimbidwe. Salimo la Davide. Mulungu amene ndimakutamandani, musakhale chete,
2 Car la bouche du méchant, et la bouche [remplie] de fraudes se sont ouvertes contre moi, [et] m'ont parlé, en usant d'une langue trompeuse.
pakuti anthu oyipa ndi achinyengo atsekula pakamwa pawo kutsutsana nane; iwo ayankhula motsutsana nane ndi malilime abodza.
3 Et des paroles pleines de haine m'ont environné, et ils me font la guerre sans cause.
Andizungulira ndi mawu audani, amandinena popanda chifukwa.
4 Au lieu que je les aimais, ils ont été mes ennemis; mais moi, je n'ai fait que prier [en leur faveur].
Mʼmalo mwa chikondi changa amandineneza, koma ine ndine munthu wapemphero.
5 Et ils m'ont rendu le mal pour le bien, et la haine pour l'amour que je leur portais.
Iwo amandibwezera zoyipa mʼmalo mwa zabwino, ndi udani mʼmalo mwa chikondi changa.
6 Etablis le méchant sur lui, et fais que l'adversaire se tienne à sa droite.
Sankhani munthu woyipa kuti amutsutse iye; lolani wotsutsa ayime ku dzanja lake lamanja.
7 Quand il sera jugé, fais qu'il soit déclaré méchant, et que sa prière soit regardée comme un crime.
Pamene aweruzidwa, apezeke kuti ndi wolakwa, ndipo mapemphero ake amutsutse.
8 Que sa vie soit courte, et qu'un autre prenne sa charge.
Masiku ake akhale owerengeka; munthu wina atenge malo ake a utsogoleri.
9 Que ses enfants soient orphelins, et sa femme veuve;
Ana ake akhale amasiye ndipo mkazi wake akhale wopanda mwamuna.
10 Et que ses enfants soient entièrement vagabonds, et qu'ils mendient et quêtent [en sortant] de leurs maisons détruites.
Ana ake akhale oyendayenda ndi opemphapempha; apirikitsidwe kuchoka pa mabwinja a nyumba zawo.
11 Que le créancier usant d'exaction attrape tout ce qui est à lui, et que les étrangers butinent tout son travail.
Wokongoza alande zonse zimene ali nazo; alendo afunkhe ntchito za manja ake.
12 Qu'il n'y ait personne qui étende sa compassion sur lui, et qu'il n'y ait personne qui ait pitié de ses orphelins.
Pasapezeke ndi mmodzi yemwe womukomera mtima kapena kumvera chisoni ana ake amasiye.
13 Que sa postérité soit exposée à être retranchée; que leur nom soit effacé dans la race qui le suivra.
Zidzukulu zake zithe nʼkufa, mayina awo afafanizidwe mu mʼbado wotsatirawo.
14 Que l'iniquité de ses pères revienne en mémoire à l'Eternel, et que le péché de sa mère ne soit point effacé.
Mphulupulu za makolo ake zikumbukiridwe pamaso pa Yehova; tchimo la amayi ake lisadzafafanizidwe.
15 Qu'ils soient continuellement devant l'Eternel; et qu'il retranche leur mémoire de la terre;
Machimo awo akhale pamaso pa Yehova nthawi zonse, kuti Iye achotse chikumbutso chawo pa dziko lapansi.
16 Parce qu'il ne s'est point souvenu d'user de miséricorde, mais il a persécuté l'homme affligé et misérable, dont le cœur est brisé, et cela pour le faire mourir.
Pakuti iye sanaganizirepo zochita chifundo, koma anazunza mpaka kuwapha anthu osauka ndi osweka mtima.
17 Puisqu'il a aimé la malédiction, que la malédiction tombe sur lui; et parce qu'il n'a point pris plaisir à la bénédiction, que la bénédiction aussi s'éloigne de lui.
Anakonda kutemberera, matembererowo abwerere kwa iye; sanakondwe nʼkudalitsa anthu ena, choncho madalitso akhale kutali naye.
18 Et qu'il soit revêtu de malédiction comme de sa robe, et qu'elle entre dans son corps comme de l'eau, et dans ses os comme de l'huile.
Anavala kutemberera ngati chovala; kutemberera kunalowa mʼthupi lake ngati madzi, kulowa mʼmafupa ake ngati mafuta.
19 Qu'elle lui soit comme un vêtement dont il se couvre, et comme une ceinture, dont il se ceigne continuellement.
Matemberero akhale ngati chofunda chodzikutira nacho, ngati lamba wovala tsiku ndi tsiku.
20 Telle soit de part l'Eternel la récompense de mes adversaires, et de ceux qui parlent mal de moi.
Awa akhale malipiro ochokera kwa Yehova pa onditsutsa anga, kwa iwo amene amayankhula zoyipa za ine.
21 Mais toi, Eternel Seigneur, agis avec moi pour l'amour de ton Nom; [et] parce que ta miséricorde est tendre, délivre-moi.
Koma Inu Ambuye Wamphamvuzonse, muchite nane molingana ndi dzina lanu, chifukwa cha ubwino wa chikondi chanu, pulumutseni.
22 Car je suis affligé et misérable, et mon cœur est blessé au-dedans de moi.
Pakuti ndine wosauka ndi wosowa, ndipo mtima wanga ukuwawa mʼkati mwanga.
23 Je m'en vais comme l'ombre quand elle décline, et je suis chassé comme une sauterelle.
Ndikuzimirira ngati mthunzi wa kumadzulo, ndapirikitsidwa ngati dzombe.
24 Mes genoux sont affaiblis par le jeûne, et ma chair s'est amaigrie, au lieu qu'elle était en bon point.
Mawondo anga afowoka chifukwa cha kusala zakudya, thupi langa lawonda ndi mutu wanga womwe.
25 Encore leur suis-je en opprobre; quand ils me voient ils branlent la tête.
Ndine chinthu chotonzedwa kwa otsutsana nane; akandiona, amapukusa mitu yawo.
26 Eternel mon Dieu! aide-moi, [et] délivre-moi selon ta miséricorde.
Thandizeni Inu Yehova Mulungu wanga; pulumutseni molingana ndi chikondi chanu.
27 Afin qu'on connaisse que c'est ici ta main, et que toi, ô Eternel! tu as fait ceci.
Adaniwo adziwe kuti limeneli ndi dzanja lanu, kuti Inu Yehova mwachita zimenezi.
28 Ils maudiront, mais tu béniras; ils s'élèveront, mais ils seront confus, et ton serviteur se réjouira.
Angathe kutemberera, koma Inu mudzadalitsa; pamene iwo andiputa adzachititsidwa manyazi, koma mtumiki wanu adzasangalala.
29 Que mes adversaires soient revêtus de confusion, et couverts de leur honte comme d'un manteau.
Onditsutsa adzavekedwa mnyozo, ndipo adzadzifunditsa manyazi ngati chovala.
30 Je célébrerai hautement de ma bouche l'Eternel, et je le louerai au milieu de plusieurs nations.
Ndi pakamwa panga ndidzathokoza Yehova kwambiri; ndidzamutamanda mʼgulu lalikulu la anthu.
31 De ce qu'il se tient à la droite du misérable, pour le délivrer de ceux qui condamnent son âme.
Popeza Iye amayima ku dzanja lamanja la munthu wosowayo, kupulumutsa moyo wake kwa iwo amene agamula molakwa.