< Proverbes 1 >
1 Les Proverbes de Salomon, fils de David, et Roi d'Israël.
Iyi ndi miyambi ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israeli:
2 Pour connaître la sagesse et l'instruction, pour entendre les discours d'intelligence;
Ndi yothandiza kuti munthu adziwe nzeru ndi malangizo; kuti amvetse mawu a matanthauzo ozama;
3 Pour recevoir une leçon de bon sens, de justice, de jugement et d'équité.
kuti alandire malangizo othandiza kuti achite zinthu mwanzeru, akhale wangwiro, wachilungamo ndiponso wosakondera.
4 Pour donner du discernement aux simples, et de la connaissance et de l'adresse aux jeunes gens.
Ndi yothandiza munthu wamba kuti aphunzire nzeru za kuchenjera, achinyamata kudziwa zinthu bwino ndi kulingalira.
5 Le sage écoutera, et deviendra mieux appris, et l'homme intelligent acquerra de la prudence;
Munthu wanzeru amvetse bwino miyamboyi kuti awonjezere kuphunzira kwake, ndi munthu womvetsa zinthu bwino apatepo luso,
6 Afin d'entendre les discours sentencieux, et ce qui est élégamment dit; les paroles des sages, et leurs énigmes.
kuti azimvetsa miyambi ndi mafanizo, mawu a anthu anzeru ndi mikuluwiko.
7 La crainte de l'Eternel est la principale science; [mais] les fous méprisent la sagesse et l'instruction.
Kuopa Yehova ndiye chiyambi cha nzeru. Zitsiru zimanyoza nzeru ndi malangizo.
8 Mon fils, écoute l'instruction de ton père, et n'abandonne point l'enseignement de ta mère.
Mwana wanga, mvera malangizo a abambo ako ndipo usakane mawu okuwongolera a amayi ako.
9 Car ce seront des grâces enfilées ensemble autour de ta tête, et des colliers autour de ton cou.
Ali ngati sangamutu yokongola ya maluwa pamutu pako ndiponso ali ngati mkanda mʼkhosi mwako.
10 Mon fils, si les pécheurs te veulent attirer, ne t'y accorde point.
Mwana wanga, ngati anthu oyipa afuna kukukopa usamawamvere.
11 S'ils disent: Viens avec nous, dressons des embûches pour tuer; épions secrètement l'innocent, quoiqu'il ne nous en ait point donné de sujet;
Akadzati, “Tiye kuno; tikabisale kuti tiphe anthu, tikabisalire anthu osalakwa;
12 Engloutissons-les tout vifs, comme le sépulcre; et tout entiers, comme ceux qui descendent en la fosse; (Sheol )
tiwameze amoyo ngati manda, ndi athunthu ngati anthu otsikira mʼdzenje. (Sheol )
13 Nous trouverons toute sorte de biens précieux, nous remplirons nos maisons de butin;
Motero tidzapeza zinthu zosiyanasiyana zamtengowapatali ndi kudzaza nyumba zathu ndi zolanda;
14 Tu y auras ton lot parmi nous, il n'y aura qu'une bourse pour nous tous.
Bwera, chita nafe maere, ndipo tidzagawana chuma chathu tonse.”
15 Mon fils, ne te mets point en chemin avec eux; retire ton pied de leur sentier.
Mwana wanga, usayende nawo pamodzi, usatsagane nawo mʼnjira zawozo.
16 Parce que leurs pieds courent au mal, et se hâtent pour répandre le sang.
Iwowatu amangofuna zoyipa zokhazokha, amathamangira kukhetsa magazi.
17 Car [comme] c'est sans sujet que le rets est étendu devant les yeux de tout ce qui a des ailes;
Nʼkopanda phindu kutchera msampha mbalame zikuona!
18 Ainsi ceux-ci dressent des embûches contre le sang de ceux-là, et épient secrètement leurs vies.
Koma anthu amenewa amangobisalira miyoyo yawo yomwe; amangodzitchera okha msampha!
19 Tel est le train de tout homme convoiteux de gain [déshonnête], lequel enlèvera la vie de ceux qui y sont adonnés.
Awa ndiwo mathero a anthu opeza chuma mwankhanza; chumacho chimapha mwiniwake.
20 La souveraine Sapience crie hautement au dehors, elle fait retentir sa voix dans les rues.
Nzeru ikufuwula mu msewu, ikuyankhula mokweza mawu mʼmisika;
21 Elle crie dans les carrefours, là où on fait le plus de bruit, aux entrées des portes, elle prononce ses paroles par la ville:
ikufuwula pa mphambano ya misewu, ikuyankhula pa zipata za mzinda kuti,
22 Sots, [dit-elle], jusques à quand aimerez-vous la sottise? Et jusqu'à quand les moqueurs prendront-ils plaisir à la moquerie, et les fous auront-ils en haine la science?
“Kodi inu anthu osachangamukanu, mudzakondwera ndi kusachangamuka mpaka liti? Nanga anthu onyogodola adzakondabe kunyogodola mpaka liti? Kapena opusa adzadana ndi nzeru mpaka liti?
23 Etant repris par moi, convertissez-vous; voici, je vous donnerai de mon Esprit en abondance, et je vous ferai connaître mes paroles.
Tamverani mawu anga a chidzudzulo. Ine ndikukuwuzani maganizo anga ndi kukudziwitsani mawu anga.
24 Parce que j'ai crié, et que vous avez refusé [d'ouïr]; parce que j'ai étendu ma main, et qu'il n'y a eu personne qui y prit garde;
Popeza ndinakuyitanani koma inu munakana kumvera. Ndinayesa kukuthandizani koma panalibe amene anasamala.
25 Et parce que vous avez rejeté tout mon conseil, et que vous n'avez point agréé que je vous reprisse;
Uphungu wanga munawunyoza. Kudzudzula kwanga simunakusamale.
26 Aussi je me rirai de votre calamité, je me moquerai quand votre effroi surviendra.
Ndiye inenso ndidzakusekani mukadzakhala mʼmavuto; ndidzakunyogodolani chikadzakugwerani chimene mumachiopacho.
27 Quand votre effroi surviendra comme une ruine, et que votre calamité viendra comme un tourbillon; quand la détresse et l'angoisse viendront sur vous;
Chiwonongeko chikadzakugwerani ngati namondwe, tsoka likadzakufikirani ngati kamvuluvulu, mavuto ndi masautso akadzakugwerani.
28 Alors on criera vers moi, mais je ne répondrai point; on me cherchera de grand matin, mais on ne me trouvera point.
“Tsono mudzandiyitana koma sindidzayankha; mudzandifunafuna, koma simudzandipeza.
29 Parce qu'ils auront haï la science, et qu'ils n'auront point choisi la crainte de l'Eternel.
Popeza iwo anadana ndi chidziwitso ndipo sanasankhe kuopa Yehova,
30 Ils n'ont point aimé mon conseil; ils ont dédaigné toutes mes répréhensions.
popeza iwo sanasamale malangizo anga ndipo ananyoza chidzudzulo changa.
31 Qu'ils mangent donc le fruit de leur voie, et qu'ils se rassasient de leurs conseils.
Tsono adzadya zipatso zoyenera mayendedwe awo ndi kukhuta ndi ntchito zimene anachita kwa ena.
32 Car l'aise des sots les tue, et la prospérité des fous les perd.
Pakuti anthu osachangamuka amaphedwa chifukwa cha kusochera kwawo, ndipo zitsiru zimadziwononga zokha chifukwa cha mphwayi zawo.
33 Mais celui qui m'écoutera, habitera en sûreté, et sera à son aise sans être effrayé d'aucun mal.
Koma aliyense wondimvera adzakhala mwa bata; adzakhala mosatekeseka posaopa chilichonse.”