< Proverbes 7 >
1 Mon fils, garde mes paroles, et mets en réserve par-devers toi mes commandements.
Mwana wanga, mvera mawu anga; usunge bwino malamulo angawa.
2 Garde mes commandements, et tu vivras, et garde mon enseignement comme la prunelle de tes yeux.
Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo; samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.
3 Lie-les à tes doigts, écris-les sur la table de ton cœur.
Uchite ngati wawamangirira pa zala zako, ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.
4 Dis à la sagesse: Tu es ma sœur; et appelle la prudence, ta parente.
Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,” ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”
5 Afin qu'elles te gardent de la femme étrangère, et de la foraine, qui se sert de paroles flatteuses.
Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.
6 Comme je regardais à la fenêtre de ma maison par mes treillis,
Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga ndinasuzumira pa zenera.
7 Je vis entre les sots, et je considérai entre les jeunes gens un jeune homme dépourvu de sens,
Ndinaona pakati pa anthu opusa, pakati pa anyamata, mnyamata wina wopanda nzeru.
8 Qui passait par une rue, près du coin d'une certaine femme, et qui tenait le chemin de sa maison;
Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo, kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.
9 Sur le soir à la fin du jour, lorsque la nuit devenait noire et obscure.
Inali nthawi yachisisira madzulo, nthawi ya usiku, kuli mdima.
10 Et voici, une femme vint au-devant de lui, parée en femme de mauvaise vie, et pleine de ruse;
Ndipo mkaziyo anadzakumana naye, atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.
11 Bruyante et débauchée, et dont les pieds ne demeurent point dans sa maison;
(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve, iye ndi wosakhazikika pa khomo.
12 Etant tantôt dehors, et tantôt dans les rues, et se tenant aux aguets à chaque coin de rue.
Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika, ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).
13 Elle le prit, et le baisa; et avec un visage effronté, lui dit:
Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,
14 J'ai chez moi des sacrifices de prospérité; j'ai aujourd'hui payé mes vœux.
“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano. Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.
15 C'est pourquoi je suis sortie au-devant de toi, pour te chercher soigneusement, et je t'ai trouvé.
Choncho ndinabwera kudzakumana nawe; ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!
16 J'ai garni mon lit d'un tour de réseau, entrecoupé de fil d'Egypte.
Pa bedi panga ndayalapo nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.
17 Je l'ai parfumé de myrrhe, d'aloès et de cinnamome.
Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.
18 Viens, enivrons-nous de plaisir jusqu'au matin, réjouissons-nous en amours.
Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa; tiye tisangalatsane mwachikondi!
19 Car mon mari n'est point en sa maison; il s'en est allé en voyage bien loin.
Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako; wapita ulendo wautali:
20 Il a pris avec soi un sac d'argent; il retournera en sa maison au jour assigné.
Anatenga thumba la ndalama ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”
21 Elle l'a fait détourner par beaucoup de douces paroles, et l'a attiré par la flatterie de ses lèvres.
Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo; amukopa ndi mawu ake oshashalika.
22 Il s'en est aussitôt allé après elle, comme le bœuf s'en va à la boucherie, et comme le fou, aux ceps pour être châtié;
Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo ngati ngʼombe yopita kukaphedwa, monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,
23 Jusqu'à ce que la flèche lui ait transpercé le foie; comme l'oiseau qui se hâte vers le filet, ne sachant point qu'on l'a tendu contre sa vie.
mpaka muvi utalasa chiwindi chake, chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe, osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.
24 Maintenant donc, enfants, écoutez-moi, et soyez attentifs à mes discours.
Tsono ana inu, ndimvereni; mvetsetsani zimene ndikunena.
25 Que ton cœur ne se détourne point vers les voies de cette femme, et qu'elle ne te fasse point égarer dans ses sentiers.
Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu; musasochere potsata njira zake.
26 Car elle a fait tomber plusieurs blessés à mort, et tous ceux qu'elle a tués étaient forts.
Paja iye anagwetsa anthu ambiri; wapha gulu lalikulu la anthu.
27 Sa maison sont les voies du sépulcre, qui descendent aux cabinets de la mort. (Sheol )
Nyumba yake ndi njira yopita ku manda, yotsikira ku malo a anthu akufa. (Sheol )