< Proverbes 31 >
1 Les paroles du Roi Lémuel et l'instruction que sa mère lui donna.
Nawa mawu a mfumu Lemueli wa ku Massa amene anamuphunzitsa amayi ake:
2 Quoi? mon fils? quoi, fils de mon ventre? eh quoi? mon fils, pour lequel j'ai tant fait de vœux?
Nʼchiyani mwana wanga? Nʼchiyani mwana wa mʼmimba mwanga? Nʼchiyani iwe mwana wanga amene ndinachita kupempha ndi malumbiro?
3 Ne donne point ta force aux femmes, et [ne mets point] ton étude à détruire les Rois.
Usapereke mphamvu yako kwa akazi. Usamayenda nawo amenewa popeza amawononga ngakhale mafumu.
4 Lémuel, ce n'est point aux Rois, ce n'est point aux Rois de boire le vin, ni aux Princes de boire la cervoise.
Iwe Lemueli si choyenera kwa mafumu, mafumu sayenera kumwa vinyo. Olamulira asamalakalake chakumwa choledzeretsa
5 De peur qu'ayant bu, ils n'oublient l'ordonnance, et qu'ils n'altèrent le droit de tous les pauvres affligés.
kuopa kuti akamwa adzayiwala malamulo a dziko, nayamba kukhotetsa zinthu zoyenera anthu osauka.
6 Donnez de la cervoise à celui qui s'en va périr, et du vin à celui qui est dans l'amertume de cœur;
Perekani chakumwa choledzeretsa kwa amene ali pafupi kufa, vinyo kwa amene ali pa mavuto woopsa;
7 Afin qu'il en boive, et qu'il oublie sa pauvreté, et ne se souvienne plus de sa peine.
amwe kuti ayiwale umphawi wawo asakumbukirenso kuvutika kwawo.
8 Ouvre ta bouche en faveur du muet, pour le droit de tous ceux qui s'en vont périr.
Yankhula mʼmalo mwa amene sangathe kudziyankhulira okha. Uwayankhulire anthu onse osiyidwa pa zonse zowayenera.
9 Ouvre ta bouche, fais justice, et fais droit à l'affligé et au nécessiteux.
Yankhula ndi kuweruza mwachilungamo. Uwateteze amphawi ndi osauka.
10 [Aleph.] Qui est-ce qui trouvera une vaillante femme? car son prix surpasse de beaucoup les perles.
Kodi mkazi wangwiro angathe kumupeza ndani? Ndi wokwera mtengo kuposa miyala yamtengowapatali.
11 [Beth.] Le cœur de son mari s'assure en elle, et il ne manquera point de dépouilles.
Mtima wa mwamuna wake umamukhulupirira ndipo mwamunayo sasowa phindu.
12 [Guimel.] Elle lui fait du bien tous les jours de sa vie, et jamais du mal.
Masiku onse a moyo wake mkaziyo amachitira mwamuna wake zabwino zokhazokha osati zoyipa.
13 [Daleth.] Elle cherche de la laine et du lin, et elle fait ce qu'elle veut de ses mains.
Iye amafunafuna ubweya ndi thonje; amagwira ntchito ndi manja ake mwaufulu.
14 [He.] Elle est comme les navires d'un marchand, elle amène son pain de loin.
Iye ali ngati sitima zapamadzi za anthu amalonda, amakatenga chakudya chake kutali.
15 [Vau.] Elle se lève lorsqu'il est encore nuit, elle distribue la nourriture nécessaire à sa maison, et elle [donne] à ses servantes leur tâche.
Iye amadzuka kusanache kwenikweni; ndi kuyamba kukonzera a pa banja pake chakudya ndi kuwagawira ntchito atsikana ake antchito.
16 [Zajin.] Elle considère un champ, et l'acquiert; et elle plante la vigne du fruit de ses mains.
Iye amalingalira za munda ndi kuwugula; ndi ndalama zimene wazipeza amalima munda wamphesa.
17 [Heth.] Elle ceint ses reins de force, et fortifie ses bras.
Iye amavala zilimbe nagwira ntchito mwamphamvu ndi manja ake.
18 [Teth.] Elle éprouve que son trafic est bon; sa lampe ne s'éteint point la nuit.
Iye amaona kuti malonda ake ndi aphindu, choncho nyale yake sizima usiku wonse.
19 [Jod.] Elle met ses mains au fuseau, et ses mains tiennent la quenouille.
Iye amadzilukira thonje ndipo yekha amagwira chowombera nsalu.
20 [Caph.] Elle tend sa main à l'affligé, et avance ses mains au nécessiteux.
Iye amachitira chifundo anthu osauka ndipo amapereka chithandizo kwa anthu osowa.
21 [Lamed.] Elle ne craint point la neige pour sa famille, car toute sa famille est vêtue de vêtements doubles.
Iye saopa kuti banja lake lifa ndi kuzizira pa nyengo yachisanu; pakuti onse amakhala atavala zovala zofunda.
22 [Mem.] Elle se fait des tours de lit; le fin lin et l'écarlate est ce dont elle s'habille.
Iye amadzipangira yekha zoyala pa bedi pake; amavala zovala zabafuta ndi zapepo.
23 [Nun.] Son mari est reconnu aux portes, quand il est assis avec les Anciens du pays.
Mwamuna wake ndi wodziwika pa chipata cha mzinda, ndipo amakhala pakati pa akuluakulu a mʼdzikomo.
24 [Samech.] Elle fait du linge, et le vend; et elle fait des ceintures, qu'elle donne au marchand.
Iye amasoka nsalu zabafuta nazigulitsa; amaperekanso mipango kwa anthu amalonda.
25 [Hajin.] La force et la magnificence est son vêtement, et elle se rit du jour à venir.
Mphamvu ndi ulemu zimakhala ngati chovala chake; ndipo amaseka osaopa zamʼtsogolo.
26 [Pe.] Elle ouvre sa bouche avec sagesse, et la Loi de la charité est sur sa langue.
Iye amayankhula mwanzeru, amaphunzitsa anthu mwachikondi.
27 [Tsade.] Elle contemple le train de sa maison, et ne mange point le pain de paresse.
Iye amayangʼanira makhalidwe a anthu a pa banja lake ndipo sachita ulesi ndi pangʼono pomwe.
28 [Koph.] Ses enfants se lèvent, et la disent bienheureuse; son mari [aussi], et il la loue, [en disant]:
Ana ake amamunyadira ndipo amamutcha kuti wodala; ndipo mwamuna wake, amamuyamikira nʼkumati,
29 [Resch.] Plusieurs filles ont été vaillantes; mais tu les surpasses toutes.
“Pali akazi ambiri amene achita zinthu zopambana koma iwe umawaposa onsewa.”
30 [Scin.] La grâce trompe, et la beauté s'évanouit; [mais] la femme qui craint l'Eternel, sera celle qui sera louée.
Nkhope yachikoka ndi yonyenga, ndipo kukongola nʼkosakhalitsa; koma mkazi amene amaopa Yehova ayenera kutamandidwa.
31 [Thau.] Donnez-lui des fruits de ses mains, et que ses œuvres la louent aux portes.
Mupatseni mphotho chifukwa cha zimene iye wachita ndipo ntchito zake zimutamande ku mabwalo.