< Proverbes 28 >

1 Tout méchant fuit sans qu'on le poursuive; mais les justes seront assurés comme un jeune lion.
Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa, koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.
2 Il y a plusieurs gouverneurs, à cause des forfaits du pays, mais pour l'amour de l'homme avisé et intelligent, il y aura prolongation du même [Gouvernement.]
Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri, koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.
3 L'homme qui est pauvre, et qui opprime les chétifs, est [comme] une pluie, qui faisant du ravage [cause] la disette du pain.
Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.
4 Ceux qui abandonnent la Loi, louent le méchant; mais ceux qui gardent la Loi, leur font la guerre.
Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa, koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.
5 Les gens adonnés au mal n'entendent point ce qui est droit; mais ceux qui cherchent l'Eternel entendent tout.
Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama, koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.
6 Le pauvre qui marche en son intégrité, vaut mieux que le pervers [qui marche] par [deux] chemins, encore qu'il soit riche.
Munthu wosauka wa makhalidwe abwino aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.
7 Celui qui garde la Loi est un enfant prudent, mais celui qui entretient les gourmands, fait honte à son père.
Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu, koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.
8 Celui qui augmente son bien par usure et par surcroît, l'assemble pour celui qui en fera des libéralités aux pauvres.
Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.
9 Celui qui détourne son oreille pour ne point écouter la Loi, sa requête elle-même sera une abomination.
Wokana kumvera malamulo ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.
10 Celui qui fait égarer par un mauvais chemin ceux qui vont droit, tombera dans la fosse qu'il aura faite; mais ceux qui sont intègres hériteront le bien.
Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa adzagwera mu msampha wake womwe, koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.
11 L'homme riche pense être sage; mais le chétif qui est intelligent, le sondera.
Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru, koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.
12 Quand les justes se réjouissent, la gloire est grande, mais quand les méchants sont élevés, chacun se déguise.
Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu; koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.
13 Celui qui cache ses transgressions, ne prospérera point; mais celui qui les confesse, et les délaisse, obtiendra miséricorde.
Wobisa machimo ake sadzaona mwayi, koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.
14 Bienheureux est l'homme qui se donne frayeur continuellement; mais celui qui endurcit son cœur, tombera dans la calamité.
Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse, koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.
15 Le dominateur méchant sur un peuple pauvre, est un lion rugissant, et comme un ours quêtant sa proie.
Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.
16 Le Conducteur qui manque d'intelligence, fait beaucoup d'extorsions; [mais] celui qui hait le gain déshonnête, prolongera ses jours.
Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.
17 L'homme qui fait tort au sang d'une personne, fuira jusqu'en la fosse, sans qu'aucun le retienne.
Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake; wina aliyense asamuthandize.
18 Celui qui marche dans l'intégrité sera sauvé; mais le pervers qui marche par [deux] chemins, tombera tout à coup.
Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.
19 Celui qui laboure sa terre, sera rassasié de pain; mais celui qui suit les fainéants, sera accablé de misère.
Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.
20 L'homme fidèle abondera en bénédictions, mais celui qui se hâte de s'enrichir ne demeurera point impuni.
Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri, koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.
21 Il n'est pas bon d'avoir égard à l'apparence des personnes; car pour un morceau de pain, l'homme commettrait un crime.
Kukondera si kwabwino, ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.
22 L'homme qui a l'œil malin se hâte pour avoir des richesses, et il ne sait pas que la disette lui arrivera.
Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.
23 Celui qui reprend quelqu'un, sera à la fin plus chéri que celui qui flatte de sa langue.
Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.
24 Celui qui pille son père ou sa mère, et qui dit que ce n'est point un péché, est compagnon de l'homme dissipateur.
Amene amabera abambo ake kapena amayi ake namanena kuti “kumeneko sikulakwa,” ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.
25 Celui qui a le cœur enflé excite la querelle; mais celui qui s'assure sur l'Eternel, sera engraissé.
Munthu wadyera amayambitsa mikangano, koma amene amadalira Yehova adzalemera.
26 Celui qui se confie en son propre cœur, est un fou; mais celui qui marche sagement, sera délivré.
Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru, koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.
27 Celui qui donne au pauvre, n'aura point de disette; mais celui qui en détourne ses yeux, abondera en malédictions.
Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu, koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.
28 Quand les méchants s'élèvent, l'homme se cache; mais quand ils périssent, les justes se multiplient.
Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala, koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

< Proverbes 28 >