< Proverbes 21 >

1 Le cœur du Roi est en la main de l'Eternel [comme] des ruisseaux d'eaux, il l'incline à tout ce qu'il veut.
Mtima wa mfumu uli ngati mtsinje wamadzi mʼdzanja la Yehova; Iye amautsongolera pa chilichonse chimene akufuna.
2 Chaque voie de l'homme lui semble droite; mais l'Eternel pèse les cœurs.
Makhalidwe a munthu amaoneka olungama kwa mwini wakeyo, koma Yehova ndiye amayesa mtima wake.
3 Faire ce qui est juste et droit, est une chose que l'Eternel aime mieux que des sacrifices.
Za chilungamo ndi zolondola ndi zomwe zimakondweretsa Yehova kuposa kupereka nsembe.
4 Les yeux élevés, et le cœur enflé, est le labourage des méchants, qui n'est que péché.
Maso odzikuza ndi mtima wonyada, zimatsogolera anthu oyipa ngati nyale nʼchifukwa chake amachimwa.
5 Les pensées d'un homme diligent le conduisent à l'abondance, mais tout étourdi tombe dans l'indigence.
Zolinga za munthu wakhama zimachulukitsa zinthu zake; koma aliyense wochita zinthu mofulumira amadzakhala wosauka.
6 Travailler à avoir des trésors par une langue trompeuse, c'est une vanité poussée au loin par ceux qui cherchent la mort.
Chuma chochipeza ndi mawu onyenga ndi chosakhalitsa ndipo chimakola anthu mu msampha wa imfa.
7 Le fourragement des méchants les abattra, parce qu'ils auront refusé de faire ce qui est droit.
Chiwawa cha anthu oyipa chidzawawononga, pakuti iwo amakana kuchita zolungama.
8 Quand un homme marche de travers, il s'égare; mais l'œuvre de celui qui est pur, est droite.
Njira ya munthu wolakwa ndi yokhotakhota, koma makhalidwe a munthu wosalakwa ndi olungama.
9 Il vaut mieux habiter au coin d'un toit, que dans une maison spacieuse avec une femme querelleuse.
Nʼkwabwino kukhala wekha pa ngodya ya denga la nyumba, kuposa kukhala mʼnyumba pamodzi ndi mkazi wolongolola.
10 L'âme du méchant souhaite le mal, et son prochain ne trouve point de grâce devant lui.
Munthu woyipa amalakalaka zoyipa; sachitira chifundo mnansi wake wovutika.
11 Quand on punit le moqueur, le niais devient sage; et quand on instruit le sage, il reçoit la science.
Munthu wonyoza akalangidwa, anthu opusa amapeza nzeru; koma munthu wanzeru akalangizidwa, amapeza chidziwitso.
12 Le juste considère prudemment la maison du méchant, quand les méchants sont renversés dans la misère.
Zolingalira za munthu woyipa nʼzosabisika pamaso pa Yehova, ndipo Iye adzawononga woyipayo.
13 Celui qui bouche son oreille pour n'ouïr point le cri du chétif, criera aussi lui-même, et on ne lui répondra point.
Amene atsekera mʼkhutu mwake wosauka akamalira, nayenso adzalira koma palibe adzamuyankhe.
14 Le don fait en secret apaise la colère, et le présent mis au sein apaise une véhémente fureur.
Mphatso yoperekedwa mseri imathetsa mkwiyo, ndipo chiphuphu choperekedwa mobisa chimathetsa mphamvu ya ukali woopsa.
15 C'est une joie au juste de faire ce qui est droit; mais c'est une frayeur aux ouvriers d'iniquité.
Chilungamo chikachitika anthu olungama amasangalala, koma anthu oyipa amaopsedwa nazo.
16 L'homme qui se détourne du chemin de la prudence aura sa demeure dans l'assemblée des trépassés.
Munthu amene amachoka pa njira ya anthu anzeru adzapezeka mʼgulu la anthu akufa.
17 L'homme qui aime à rire, sera indigent; et celui qui aime le vin et la graisse, ne s'enrichira point.
Aliyense wokonda zisangalalo adzasanduka mʼmphawi, ndipo wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
18 Le méchant sera l'échange du juste; et le perfide, au lieu des hommes intègres.
Anthu oyipa adzakhala chowombolera cha anthu olungama ndipo osakhulupirika chowombolera anthu olungama mtima.
19 Il vaut mieux habiter dans une terre déserte, qu'avec une femme querelleuse et qui se dépite.
Nʼkwabwino kukhala mʼchipululu kuposa kukhala ndi mkazi wolongolola ndi wopsa mtima msanga.
20 La provision désirable, et l'huile, est dans la demeure du sage; mais l'homme fou l'engloutit.
Munthu wanzeru samwaza chuma chake, koma wopusa amachiwononga.
21 Celui qui s'adonne soigneusement à la justice, et à la miséricorde, trouvera la vie, la justice, et la gloire.
Amene amatsata chilungamo ndi kukhulupirika, amapeza moyo ndi ulemerero.
22 Le sage entre dans la ville des forts, et rabaisse la force de sa confiance.
Munthu wanzeru amagonjetsa mzinda wa anthu amphamvu ndi kugwetsa linga limene iwo amalidalira.
23 Celui qui garde sa bouche et sa langue, garde son âme de détresse.
Amene amagwira pakamwa pake ndi lilime lake sapeza mavuto.
24 Un superbe arrogant s'appelle un moqueur, qui fait tout avec colère et fierté.
Munthu wonyada ndi wodzikuza amamutcha, “Mnyodoli,” iye amachita zinthu modzitama kwambiri.
25 Le souhait du paresseux le tue; car ses mains ont refusé de travailler.
Chilakolako cha munthu waulesi chidzamupha yekha chifukwa manja ake amangokhala goba osagwira ntchito.
26 Il y a tel qui tout le jour ne fait que souhaiter; mais le juste donne, et n'épargne rien.
Tsiku lonse anthu oyipa amasirira zambiri, koma anthu olungama amapereka mowolowamanja.
27 Le sacrifice des méchants est une abomination; combien plus s'ils l'apportent avec une méchante intention?
Nsembe ya anthu oyipa imamunyansa Yehova, nanji akayipereka ndi cholinga choyipa!
28 Le témoin menteur périra; mais l'homme qui écoute, parlera avec gain de cause.
Mboni yonama idzawonongeka, koma mawu a munthu wakumva adzakhala nthawi zonse.
29 L'homme méchant a un air impudent; mais l'homme juste dresse ses voies.
Munthu woyipa amafuna kudzionetsa ngati wolimba mtima, koma munthu wowongoka amaganizira njira zake.
30 Il n'y a ni sagesse, ni intelligence, ni conseil contre l'Eternel.
Palibe nzeru, palibe kumvetsa bwino, palibenso uphungu, zimene zingapambane Yehova.
31 Le cheval est équipé pour le jour de la bataille, mais la délivrance vient de l'Eternel.
Kavalo amamukonzera tsiku la nkhondo, koma ndi Yehova amene amapambanitsa.

< Proverbes 21 >