< Proverbes 16 >

1 Les préparations du cœur sont à l'homme; mais le discours de la langue est de par l'Eternel.
Zolinga za mu mtima ndi za munthu, koma kwa Yehova ndiye kumachokera yankho.
2 Chacune des voies de l'homme lui semble pure; mais l'Eternel pèse les esprits.
Zochita zonse za munthu zimaoneka zabwino pamaso pake, koma Yehova ndiye amasanthula zolinga zako.
3 Remets tes affaires à l'Eternel, et tes pensées seront bien ordonnées.
Pereka ntchito zako zonse mʼmanja mwa Yehova, ndipo zolinga zako zidzachitikadi.
4 L'Eternel a fait tout pour soi-même; et même le méchant pour le jour de la calamité.
Yehova amachita zonse ndi cholinga chake, ngakhale anthu oyipa kuti aone tsiku latsoka.
5 L'Eternel a en abomination tout homme hautain de cœur; de main en main il ne demeurera point impuni.
Munthu aliyense wodzikuza amamunyansa Yehova. Koma dziwani izi: Iwo sadzakhala osalangidwa.
6 Il y aura propitiation pour l'iniquité par la miséricorde et la vérité; et on se détourne du mal par la crainte de l'Eternel.
Chifukwa cha chikondi chosasinthika ndi kukhulupirika, munthu amakhululukidwa machimo ake; chifukwa cha kuopa Yehova munthu amapewa zoyipa.
7 Quand l'Eternel prend plaisir aux voies de l'homme, il apaise envers lui ses ennemis mêmes.
Pamene makhalidwe a munthu akondweretsa Yehova, ngakhale adani ake amakhala naye mwa mtendere.
8 Il vaut mieux un peu de bien avec justice, qu'un gros revenu là où l'on n'a point de droit.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono zozipeza mwachilungamo, kusiyana ndi kukhala ndi zinthu zambiri zozipeza popanda chilungamo.
9 Le cœur de l'homme délibère de sa voie; mais l'Eternel conduit ses pas.
Mtima wa munthu umalingalira zochita, koma Yehova ndiye amakhazikitsa njira zake.
10 Il y a divination aux lèvres du Roi, et sa bouche ne se fourvoiera point du droit.
Mawu a mfumu ali ngati mawu ochokera kwa Mulungu; ndipo pakamwa pake sipalakwa poweruza mlandu.
11 La balance et le trébuchet justes sont de l'Eternel, et tous les poids du sachet sont son œuvre.
Miyeso ndi masikelo achilungamo zimachokera kwa Yehova; miyala yonse yoyesera ya mʼthumba anayipanga ndi Yehova.
12 Ce doit être une abomination aux Rois de faire injustice, parce que le trône est établi par la justice.
Kuchita zoyipa kumanyansa mafumu, pakuti chilungamo ndiye maziko a ufumu wake.
13 Les Rois [doivent prendre] plaisir aux lèvres de justice, et aimer celui qui profère des choses justes.
Mawu owona amakondweretsa mfumu. Iyo imakonda munthu woyankhula choonadi.
14 Ce sont autant de messagers de mort que la colère du Roi; mais l'homme sage l'apaisera.
Ukali wa mfumu ndi mthenga wa imfa, koma munthu wanzeru amawupepesa ukaliwo.
15 C'est vie que le visage serein du Roi, et sa faveur est comme la nuée portant la pluie de la dernière saison.
Kuwala kwa nkhope ya mfumu kumapatsa moyo; ndipo kukoma mtima kwake kuli ngati mitambo ya mvula nthawi ya chilimwe.
16 Combien est-il plus précieux que le fin or, d'acquérir de la sagesse; et combien est-il plus excellent que l'argent, d'acquérir de la prudence?
Nʼkwabwino kwambiri kupeza nzeru kupambana golide. Kukhala womvetsa bwino zinthu nʼkwabwino kupambana ndi kukhala ndi siliva.
17 Le chemin relevé des hommes droits, c'est de se détourner du mal; celui-là garde son âme qui prend garde à son train.
Msewu wa munthu wowongoka mtima umapewa zoyipa; wopenyetsetsa kumene akupita amasunga moyo wake.
18 L'orgueil va devant l'écrasement; et la fierté d'esprit devant la ruine.
Kunyada kumafikitsa ku chiwonongeko, ndipo munthu wodzikuza adzagwa.
19 Mieux vaut être humilié d'esprit avec les débonnaires, que de partager le butin avec les orgueilleux.
Nʼkwabwino kukhala ndi mtima wodzichepetsa pakati pa anthu oponderezedwa, kusiyana ndi kugawana zolanda ndi anthu onyada.
20 Celui qui prend garde à la parole, trouvera le bien; et celui qui se confie en l'Eternel, est bienheureux.
Munthu womvera malangizo zinthu zimamuyendera bwino, ndipo wodala ndi amene amadalira Yehova.
21 On appellera prudent le sage de cœur; et la douceur des lèvres augmente la doctrine.
A mtima wanzeru amatchedwa ozindikira zinthu, ndipo mawu ake okoma amawonjezera nzeru.
22 La prudence est à ceux qui la possèdent une source de vie; mais l'instruction des fous est une folie.
Kumvetsa zinthu ndi kasupe wa moyo kwa iwo amene ali nako, koma uchitsiru umabweretsa chilango kwa zitsiru.
23 Le cœur sage conduit prudemment sa bouche, et ajoute doctrine sur ses lèvres.
Mtima wanzeru umathandiza munthu kuyankhula mwa nzeru, ndipo mawu ake amawonjezera nzeru.
24 Les paroles agréables sont des rayons de miel, douceur à l'âme, et santé aux os.
Mawu okometsera ali ngati chisa cha njuchi, amakoma mu mtima ndipo amalimbitsa thupi.
25 II y a telle voie qui semble droite à l'homme, mais dont la fin sont les voies de la mort.
Pali njira ina yooneka ngati yowongoka kwa munthu koma kumatsiriziro kwake ndi imfa.
26 L'âme de celui qui travaille, travaille pour lui-même, parce que sa bouche se courbe devant lui.
Njala ya munthu wantchito imamuthandiza kulimbikira; njalayo imamukakamiza kuchitapo kanthu.
27 Le méchant creuse le mal, et il y a comme un feu brûlant sur ses lèvres.
Munthu wopanda pake amakonzekera kuchita zoyipa ndipo mawu ake ali ngati moto wopsereza.
28 L'homme qui use de renversements, sème des querelles, et le rapporteur met le plus grand ami en division.
Munthu woyipa mtima amayambitsa mikangano, ndipo miseche imalekanitsa anthu okondana kwambiri.
29 L'homme violent attire son compagnon, et le fait marcher par une voie qui n'est pas bonne.
Munthu wandewu amakopa mnansi wake, ndipo amamuyendetsa njira imene si yabwino.
30 Il fait signe des yeux pour machiner des renversements, et remuant ses lèvres il exécute le mal.
Amene amatsinzinira maso ake amalingalira zinthu zokhota; amene amachita msunamo amakonzeka kuchita zoyipa.
31 Les cheveux blancs sont une couronne d'honneur; et elle se trouvera dans la voie de la justice.
Imvi zili ngati chipewa chaufumu chaulemerero; munthu amazipeza akakhala moyo wolungama.
32 Celui qui est tardif à colère, vaut mieux que l'homme fort; et celui qui est le maître de son cœur, vaut mieux que celui qui prend des villes.
Munthu wosapsa mtima msanga amaposa munthu wankhondo, munthu wowugwira mtima wake amaposa amene amalanda mzinda.
33 On jette le sort au giron, mais tout ce qui en doit arriver, est de par l'Eternel.
Maere amaponyedwa pa mfunga, koma ndiye Yehova amene amalongosola zonse.

< Proverbes 16 >