< Proverbes 15 >

1 La réponse douce apaise la fureur; mais la parole fâcheuse excite la colère.
Kuyankha kofatsa kumathetsa mkwiyo, koma mawu ozaza amautsa ukali.
2 La langue des sages embellit la science; mais la bouche des fous profère la folie.
Munthu wanzeru amayankhula zinthu za nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamatulutsa za uchitsiru.
3 Les yeux de l'Eternel sont en tous lieux, contemplant les méchants et les bons.
Maso a Yehova ali ponseponse, amayangʼana pa oyipa ndi abwino omwe.
4 La langue qui corrige [le prochain], est [comme] l'arbre de vie; mais celle où il y a de la perversité, est un rompement d'esprit.
Kuyankhula kodekha kuli ngati mtengo wopatsa moyo, koma kuyankhula kopotoka kumapweteka mtima.
5 Le fou méprise l'instruction de son père; mais celui qui prend garde à la répréhension, deviendra bien-avisé.
Chitsiru chimanyoza mwambo wa abambo ake, koma wochenjera amasamala chidzudzulo.
6 Il y a un grand trésor dans la maison du juste; mais il y a du trouble dans le revenu du méchant.
Munthu wolungama amakhala ndi chuma chambiri, zimene woyipa amapindula nazo zimamugwetsa mʼmavuto.
7 Les lèvres des sages répandent partout la science; mais le cœur des fous ne fait pas ainsi.
Pakamwa pa anthu anzeru pamafalitsa nzeru; koma mitima ya zitsiru sitero.
8 Le sacrifice des méchants est en abomination à l'Eternel; mais la requête des hommes droits lui est agréable.
Nsembe za anthu oyipa zimamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi pemphero la anthu owona mtima.
9 La voie du méchant est en abomination à l'Eternel; mais il aime celui qui s'adonne soigneusement à la justice.
Ntchito za anthu oyipa zimamunyansa Yehova koma amakonda amene amafunafuna chilungamo.
10 Le châtiment est fâcheux à celui qui quitte le [droit] chemin; [mais] celui qui hait d'être repris, mourra.
Amene amasiya njira yabwino adzalangidwa koopsa. Odana ndi chidzudzulo adzafa.
11 Le sépulcre et le gouffre sont devant l'Eternel; combien plus les cœurs des enfants des hommes? (Sheol h7585)
Manda ndi chiwonongeko ndi zosabisika pamaso pa Yehova, nanji mitima ya anthu! (Sheol h7585)
12 Le moqueur n'aime point qu'on le reprenne, et il n'ira [jamais] vers les sages.
Wonyoza sakonda kudzudzulidwa; iye sapita kwa anthu anzeru.
13 Le cœur joyeux rend la face belle, mais l'esprit est abattu par l'ennui du cœur.
Mtima wokondwa umachititsa nkhope kukhala yachimwemwe, koma mtima wosweka umawawitsa moyo.
14 Le cœur de l'homme prudent cherche la science; mais la bouche des fous se repaît de folie.
Mtima wa munthu wozindikira zinthu umafunafuna nzeru, koma pakamwa pa zitsiru pamadya uchitsiru wawo.
15 Tous les jours de l'affligé sont mauvais; mais quand on a le cœur gai, c'est un banquet perpétuel.
Munthu woponderezedwa masiku ake onse amakhala oyipa, koma mtima wachimwemwe umakhala pa chisangalalo nthawi zonse.
16 Un peu de bien vaut mieux avec la crainte de l'Eternel, qu'un grand trésor avec lequel il y a du trouble.
Kuli bwino kukhala ndi zinthu pangʼono nʼkumaopa Yehova, kusiyana ndi kukhala ndi chuma chambiri uli pamavuto.
17 Mieux vaut un repas d'herbes, où il y a de l'amitié, qu'un repas de bœuf bien gras, où il y a de la haine.
Kuli bwino kudyera ndiwo zamasamba pamene pali chikondi, kusiyana ndi kudyera nyama yangʼombe yonenepa pamene pali udani.
18 L'homme furieux excite la querelle; mais l'homme tardif à colère apaise la dispute.
Munthu wopsa mtima msanga amayambitsa mikangano, koma munthu woleza mtima amathetsa ndewu.
19 La voie du paresseux est comme une haie de ronces; mais le chemin des hommes droits est relevé.
Njira ya munthu waulesi ndi yowirira ndi mtengo waminga, koma njira ya munthu wolungama ili ngati msewu waukulu.
20 L'enfant sage réjouit le père; mais l'homme insensé méprise sa mère.
Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake, koma mwana wopusa amanyoza amayi ake.
21 La folie est la joie de celui qui est dépourvu de sens; mais l'homme prudent dresse ses pas pour marcher.
Uchitsiru umakondweretsa munthu wopanda nzeru, koma munthu womvetsa zinthu amayenda mowongoka.
22 Les résolutions deviennent inutiles où il n'y a point de conseil; mais il y a de la fermeté dans la multitude des conseillers.
Popanda uphungu zolinga zako munthu zimalephereka, koma pakakhala aphungu ambiri zolinga zimatheka.
23 L'homme a de la joie dans les réponses de sa bouche; et la parole dite en son temps combien est-elle bonne?
Munthu amakondwera ndi kuyankha koyenera, ndipo mawu onena pa nthawi yake ndi okoma.
24 Le chemin de la vie tend en haut pour l'homme prudent, afin qu'il se retire du sépulcre qui est en bas. (Sheol h7585)
Munthu wanzeru amatsata njira yopita ku moyo kuti apewe malo okhala anthu akufa. (Sheol h7585)
25 L'Eternel démolit la maison des orgueilleux, mais il établit la borne de la veuve.
Yehova amapasula nyumba ya munthu wonyada koma amasamalira malo a mkazi wamasiye.
26 Les pensées du malin sont en abomination à l'Eternel; mais celles de ceux qui sont purs, sont des paroles agréables.
Maganizo a anthu oyipa amamunyansa Yehova, koma mawu a anthu oyera mtima amamusangalatsa.
27 Celui qui est entièrement adonné au gain déshonnête, trouble sa maison; mais celui qui hait les dons, vivra.
Munthu wofuna phindu mwachinyengo amavutitsa banja lake, koma wodana ndi ziphuphu adzakhala ndi moyo.
28 Le cœur du juste médite ce qu'il doit répondre; mais la bouche des méchants profère des choses mauvaises.
Munthu wolungama amaganizira za mmene ayankhire, koma pakamwa pa munthu woyipa pamatulutsa mawu oyipa.
29 L'Eternel est loin des méchants; mais il exauce la requête des justes.
Yehova amakhala kutali ndi anthu oyipa, koma amamva pemphero la anthu olungama.
30 La clarté des yeux réjouit le cœur; et la bonne renommée engraisse les os.
Kuwala kwa maso kumasangalatsa mtima ndipo uthenga wabwino umalimbitsa munthu.
31 L'oreille qui écoute la répréhension de vie, logera parmi les sages.
Womvera mawu a chidzudzulo amene apatsa moyo adzakhala pakati pa anthu anzeru.
32 Celui qui rejette l'instruction a en dédain son âme; mais celui qui écoute la répréhension, s'acquiert du sens.
Amene amanyoza mwambo amadzinyoza yekha, koma womvera mawu a chidzudzulo amapeza nzeru zomvetsa zinthu.
33 La crainte de l'Eternel est une instruction de sagesse, et l'humilité va devant la gloire.
Kuopa Yehova kumaphunzitsa munthu nzeru, ndipo kudzichepetsa ndi ulemu chili patsogolo ndi kudzichepetsa.

< Proverbes 15 >