< Nombres 31 >

1 L'Eternel parla aussi à Moïse, en disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Fais la vengeance des enfants d'Israël sur les Madianites, puis tu seras recueilli vers tes peuples.
“Uwabwezere zoyipa Amidiyani chifukwa cha zimene anachitira Aisraeli. Ukatha kuchita zimenezi, iwe udzamwalira.”
3 Moïse donc parla au peuple, en disant: Que quelques-uns d'entre vous s'équipent pour aller à la guerre, et qu'ils aillent contre Madian, pour exécuter la vengeance de l'Eternel sur Madian.
Ndipo Mose anati kwa Aisraeli, “Perekani zida kwa ena mwa anthu anu kuti akamenyane ndi Amidiyani ndi kuwabwezera choyipa mʼmalo mwa Yehova.
4 Vous enverrez à la guerre mille [hommes] de chaque Tribu, de toutes les tribus d'Israël.
Mutumize ku nkhondoko amuna 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.”
5 On donna donc d'entre les milliers d'Israël mille hommes de chaque Tribu, qui furent douze mille hommes équipés pour la guerre.
Choncho amuna okwana 12,000 anatenga zida kukonzekera nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse la Aisraeli.
6 Et Moïse les envoya à la guerre, [savoir] mille de chaque Tribu, et avec eux Phinées, fils d'Eiéazar le Sacrificateur, qui avait les vaisseaux du Sanctuaire, et les trompettes de retentissement en sa main.
Mose anawatumiza ku nkhondo, anthu 1,000 kuchokera ku fuko lililonse pamodzi ndi Finehasi mwana wa Eliezara wansembe amene ananyamula zipangizo zochokera ku malo wopatulika ndi malipenga okaliza.
7 Ils marchèrent donc en guerre contre Madian, comme l'Eternel l'avait commandé à Moïse, et ils en tuèrent tous les mâles.
Iwo anamenyana ndi Amidiyani monga momwe Yehova analamulira Mose ndipo anapha mwamuna aliyense.
8 Ils tuèrent aussi les Rois de Madian, outre les autres qui y furent tués, [savoir] Evi, Rékem, Tsur, Hur, et Rébah, cinq Rois de Madian; ils firent aussi passer au fil de l'épée Balaam fils de Béhor.
Mwa anthu ophedwawo munali Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu asanu a Amidiyani. Ndipo anaphanso ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori.
9 Et les enfants d'Israël emmenèrent prisonniers les femmes de Madian, avec leurs petits enfants, et pillèrent tout leur gros et menu bétail, et tout ce qui était en leur puissance.
Aisraeli anagwira ukapolo amayi a Chimidiyani ndi ana awo ndipo analandanso ngʼombe, ziweto zawo zina zonse ndi katundu wawo yense.
10 Ils brûlèrent au feu toutes leurs villes, leurs demeures, et tous leurs châteaux;
Anawotcha mizinda yonse imene Amidiyani ankakhalamo pamodzi ndi misasa yawo yonse.
11 Et ils prirent tout le butin et tout le pillage, tant des hommes que du bétail.
Anatenga zonse zimene analanda ku nkhondoko, anthu ndi zoweta zomwe.
12 Puis ils amenèrent les prisonniers, le pillage, et le butin, à Moïse et à Eléazar le Sacrificateur, et à l'assemblée des enfants d'Israël, au camp dans les campagnes de Moab, qui sont près du Jourdain de Jéricho.
Ndipo anabwera nawo akapolowo ndi zolanda ku nkhondozo kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa gulu lonse la Aisraeli ku misasa yawo ku chigwa cha Mowabu, mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani ku Yeriko.
13 Alors Moïse et Eléazar le Sacrificateur, et tous les principaux de l'assemblée sortirent au devant d'eux hors du camp.
Mose, wansembe Eliezara ndi atsogoleri onse a gululo anapita kukakumana nawo kunja kwa misasa.
14 Et Moïse se mit en grande colère contre les Capitaines de l'armée, les chefs des milliers, et les chefs des centaines, qui retournaient de cet exploit de guerre.
Mose anakwiya nawo akuluakulu a magulu a ankhondowo: olamulira 1,000 ndi olamulira 100, amene ankachokera ku nkhondo.
15 Et Moïse leur dit: N'avez-vous pas gardé en vie toutes les femmes?
Iye anafunsa kuti, “Kodi nʼchifukwa chiyani mwawaleka amoyo amayi onsewa?”
16 Voici ce sont elles qui à la parole de Balaam, ont donné [occasion] aux enfants d'Israël de pécher contre l'Eternel au fait de Péhor [ce qui attira] la plaie sur l'assemblée de l'Eternel.
Paja iwo ndi amene ankatsatira uphungu wa Balaamu ndiponso ndi amene anachititsa Aisraeli kuti asiye Yehova pa zimene zinachitika ku Peori, kotero mliri unagwera anthu a Yehova.
17 Or maintenant tuez tous les mâles d'entre les petits enfants, et tuez toute femme qui aura eu compagnie d'homme.
Tsopano iphani munthu wamwamuna aliyense. Ndiponso iphani mayi aliyense amene anagonapo ndi mwamuna,
18 Mais vous garderez en vie toutes les jeunes filles qui n'ont point eu compagnie d'homme.
koma sungani mtsikana aliyense amene sanagonepo ndi mwamuna.
19 Au reste, demeurez sept jours hors du camp. Quiconque tuera quelqu'un, et quiconque touchera quelqu'un qui aura été tué, se purifiera le troisième et le septième jour, tant vous que vos prisonniers.
“Inu nonse amene mwaphapo wina wake, kapena kukhudza aliyense amene anaphedwa mukhale kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri. Pa tsiku lachitatu mudziyeretse nokha pamodzi ndi akapolo anu.
20 Vous purifierez aussi tous vos vêtements, et tout ce qui sera fait de peau, et tous ouvrages de poil de chèvre, et toute vaisselle de bois.
Muyeretsenso zovala zanu ndi china chilichonse chopangidwa ndi chikopa, ubweya wa mbuzi kapenanso ndi mtengo.”
21 Et Eléazar le Sacrificateur dit aux hommes de guerre qui étaient allés à la bataille: Voici l'ordonnance et la Loi que l'Eternel a commandée à Moïse.
Tsono wansembe Eliezara anati kwa asilikali amene anapita ku nkhondo aja, “Lamulo limene Yehova anapereka kwa Mose ndi ili:
22 En général l'or, l'argent, l'airain, le fer, l'étain, le plomb;
Golide, siliva, mkuwa, chitsulo, chiwaya, mtovu
23 Tout ce qui peut passer par le feu, vous le ferez passer par le feu, et il sera net; seulement on le purifiera avec l'eau d'aspersion; mais vous ferez passer par l'eau toutes les choses qui ne passent point par le feu.
ndi china chilichonse chimene sichingapse ndi moto muchidutsitse pa moto, ndipo chidzayeretsedwa. Komanso chiyeretsedwe ndi madzi oyeretsa. Ndipo chilichonse chimene chingapse ndi moto muchidutsitse mʼmadzimo.
24 Vous laverez aussi vos vêtements le septième-jour, et vous serez nets, puis vous entrerez au camp.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muchape zovala zanu ndipo mudzayera. Mukatero mutha kulowa mu msasa.”
25 Et l'Eternel parla à Moïse, en disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
26 Fais le compte du butin, et de tout ce qu'on a emmené, tant des personnes que des bêtes, toi et Eléazar le Sacrificateur, et les chefs des pères de l'assemblée.
“Iwe ndi wansembe Eliezara ndiponso akuluakulu a mabanja a anthuwa, muwerenge anthu onse ndi ziweto zomwe zinagwidwa ku nkhondo.
27 Et partage par moitié le butin entre les combattants qui sont allés à la guerre, et toute l'assemblée.
Mugawe zolanda ku nkhondozo magawo awiri, lina la ankhondo amene anapita ku nkhondo, lina la anthu onse.
28 Tu lèveras aussi pour l'Eternel un tribut des gens de guerre qui sont allés à la bataille, [savoir] de cinq cents un, tant des personnes que des bœufs, des ânes et des brebis.
Pa gawo la ankhondowo, mutengeko gawo la Yehova, pa zofunkha 500 zilizonse mutengeko chimodzi, pa akapolo, ngʼombe, bulu ndi nkhosa.
29 On le prendra de leur moitié, et tu le donneras à Eléazar le Sacrificateur, en offrande élevée à l'Eternel.
Utenge zimenezo pa theka la gawo la ankhondowo ndipo upereke kwa wansembe Eliezara kuti zikhale zopereka zanu kwa Yehova.
30 Et de l'[autre] moitié qui appartient aux enfants d'Israël, tu en prendras à part de cinquante un, tant des personnes que des bœufs, des ânes, des brebis et de tous [autres] animaux, et tu le donneras aux Lévites qui ont la charge de garder le pavillon de l'Eternel.
Kuchokera pa theka la gawo la Aisraeli, utengeko cholanda chimodzi pa makumi asanu aliwonse, pa anthu, ngʼombe, abulu, nkhosa, mbuzi kapena zoweta zina. Uzipereke kwa Alevi amene ntchito yawo ndi yosamalira tenti ya Yehova.”
31 Et Moïse et Eléazar le Sacrificateur firent comme l'Eternel l'avait commandé à Moïse.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara anachita monga Yehova analamulira Mose.
32 Or le butin, qui était resté du pillage que le peuple qui était allé à la guerre, avait fait, était de six cent soixante et quinze mille brebis;
Zotsala pa zolanda ku nkhondo zimene ankhondowo anatenga zinali nkhosa 675,000,
33 De soixante et douze mille bœufs;
Ngʼombe 72,000,
34 De soixante et un mille ânes.
abulu 61,000,
35 Et quant aux femmes qui n'avaient point eu compagnie d'homme, [elles étaient] en tout trente-deux mille âmes.
ndi atsikana omwe sanagonepo ndi mwamuna 32,000.
36 Et la moitié du butin, [savoir] la part de ceux qui étaient allés à la guerre, montait à trois cent trente-sept mille cinq cents brebis.
Gawo la ankhondo amene anapita ku nkhondo linali: nkhosa 337,500,
37 Dont le tribut pour l'Eternel, quant aux brebis, fut de six cent soixante et quinze.
mwa zimenezi gawo la Yehova linali 675;
38 Et à trente-six mille bœufs; dont le tribut pour l'Eternel, quant aux bœufs, fut de soixante et douze bœufs.
ngʼombe zinalipo 36,000 ndipo gawo la Yehova linali 72;
39 Et à trente mille cinq cents ânes; dont le tribut pour l'Eternel, quant aux ânes, fut de soixante et un ânes.
abulu analipo 30,500 ndipo gawo la Yehova linali 61;
40 Et à seize mille personnes; dont le tribut pour l'Eternel fut de trente-deux personnes.
anthu analipo 16,000 ndipo gawo la Yehova linali 32.
41 Et Moïse donna à Eléazar le Sacrificateur le tribut de l'offrande élevée de l'Eternel, comme l'Eternel le lui avait commandé.
Mose anapereka kwa wansembe Eliezara gawo limene linali loyenera kupereka kwa Yehova monga momwe Yehova analamulira Mose.
42 Et de l'autre moitié qui appartenait aux enfants d'Israël, laquelle Moïse avait tirée des hommes qui étaient allés à la guerre.
Pa gawo la Aisraeli, Mose anapatula theka limodzi kuchotsa pa zolanda ku nkhondo zonse zimene zinabwera ndi ankhondo aja.
43 Or de cette moitié qui fut pour l'assemblée, et qui montait à trois cent trente-sept mille cinq cents brebis;
Tsono gawo la Aisraeli linali ili: nkhosa 337,500,
44 A trente-six mille bœufs;
ngʼombe 36,000,
45 A trente mille cinq cents ânes;
abulu 30,500,
46 Et à seize mille personnes;
anthu 16,000.
47 De cette moitié, [dis-je], qui appartenait aux enfants d'Israël, Moïse prit à part de cinquante un, tant des personnes que des bêtes, et les donna aux Lévites qui avaient la charge de garder le pavillon de l'Eternel, comme l'Eternel le lui avait commandé.
Kuchoka pa gawo la Aisraelilo, Mose anatengapo chimodzi pa zolanda ku nkhondo makumi asanu aliwonse, anthu ndi nyama, ndipo anazipereka kwa Alevi amene ankayangʼanira tenti ya Yehova monga Yehova analamulira Mose.
48 Et les capitaines qui avaient charge des milliers de l'armée, tant les chefs des milliers, que les chefs des centaines, s'approchèrent de Moïse,
Pamenepo omwe ankayangʼanira magulu a ankhondo olamulira 1,000 ndi olamulira 100 anabwera kwa Mose,
49 Et lui dirent: Tes serviteurs ont fait le compte des gens de guerre qui sont sous notre charge, et il ne s'en manque pas un seul.
iwo anati kwa iye, “Ife anthu anu tawerenga ankhondo amene timawalamulira. Palibe munthu ndi mmodzi yemwe amene wasowa.
50 C'est pourquoi nous offrons l'offrande de l'Eternel, chacun ce qu'il s'est trouvé avoir, des joyaux d'or, des jarretières, des bracelets, des anneaux, des pendants d'oreilles, et des colliers, afin de faire propitiation pour nos personnes devant l'Eternel.
Ndipo tabweretsa zopereka kwa Yehova zimene munthu aliyense anapeza: ziwiya zagolide, zibangiri, zigwinjiri, mphete zosindikizira, ndolo ndi mikanda kuti tichitire mwambo wopepesera machimo pamaso pa Yehova.”
51 Et Moïse et Eléazar le Sacrificateur reçurent d'eux l'or, [savoir] toute pièce d'ouvrage.
Ndipo Mose ndi wansembe Eliezara analandira kuchokera kwa atsogoleriwo golide pamodzi ndi zipangizo zonse zosula.
52 Et tout l'or de l'offrande élevée qui fut présenté à l'Eternel de la part des chefs de milliers et des chefs de centaines, [montait à] seize mille sept cent cinquante sicles.
Golide yense wochokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 zomwe Mose ndi Eliezara anapereka ngati mphatso kwa Yehova zinali zolemera makilogalamu 200.
53 [Or] les gens de guerre retinrent chacun pour soi ce qu'ils avaient pillé.
Wankhondo aliyense anatenga zomwe analanda yekha ku nkhondo.
54 Moïse donc et Eléazar le Sacrificateur prirent des chefs de milliers et [des chefs] de centaines cet or-là, et l'apportèrent au Tabernacle d'assignation, [en] mémorial pour les enfants d'Israël, devant l'Eternel.
Mose ndi Eliezara wansembe analandira golide kuchokera kwa atsogoleri a 1,000 ndi atsogoleri a 100 ndi kukamuyika mu tenti ya msonkhano ngati chikumbutso cha Aisraeli pamaso pa Yehova.

< Nombres 31 >