< Nombres 26 >

1 Or il arriva après cette plaie-là, que l'Eternel parla à Moïse, et à Eléazar, fils d'Aaron, le Sacrificateur, en disant:
Utatha mliri Yehova anati kwa Mose ndi Eliezara mwana wa Aaroni,
2 Faites le dénombrement de toute l'assemblée des enfants d'Israël, depuis l'âge de vingt ans, et au dessus, selon les maisons de leurs pères, [savoir] de tous ceux d'Israël qui peuvent aller à la guerre.
“Werengani Aisraeli onse mwa mabanja awo, onse a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo omwe angathe kugwira ntchito ya usilikali mʼgulu lankhondo la Israeli.”
3 Moïse donc et Eléazar le Sacrificateur leur parlèrent dans les campagnes de Moab, auprès du Jourdain de Jéricho, en disant:
Kotero mu zigwa za Mowabu pafupi ndi mtsinje wa Yorodani ku Yeriko, Mose ndi wansembe Eliezara anayankhula nawo kuti,
4 [Qu'on fasse le dénombrement] depuis l'âge de vingt ans, et au dessus, comme l'Eternel l'avait commandé à Moïse et aux enfants d'Israël, quand ils furent sortis du pays d'Egypte.
“Werengani amuna a zaka makumi awiri kapena kuposera pamenepo, monga momwe Yehova walamulira Mose.” Aisraeli omwe anachokera ku Igupto ndi awa:
5 Ruben fut le premier-né d'Israël; et les enfants de Ruben furent Hénoc; [de lui sortit] la famille des Hénokites; de Pallu, la famille des Palluites.
Zidzukulu za Rubeni, mwana woyamba wamwamuna wa Israeli, zinali izi: kuchokera mwa Hanoki, fuko la Ahanoki; kuchokera mwa Palu, fuko la Apalu;
6 De Hetsron, la famille des Hetsronites; de Carmi, la famille des Carmites.
kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Karimi, fuko la Akarimi.
7 Ce sont là les familles des Rubénites, et ceux qui furent dénombrés étaient quarante-trois mille sept cent trente.
Awa anali mafuko a Rubeni: onse amene anawerengedwa analipo 43,730.
8 Et les enfants de Pallu, Eliab.
Mwana wa Palu anali Eliabu,
9 Et les enfants d'Eliab, Némuel, Dathan et Abiram. Ce Dathan et cet Abiram, qui étaient de ceux qu'on appelait pour tenir l'assemblée, se mutinèrent contre Moïse et contre Aaron en l'assemblée de Coré, lorsqu'on se mutina contre l'Eternel;
ndipo ana a Eliabu anali Nemueli, Datani ndi Abiramu. Datani ndi Abiramu anali gulu la akuluakulu aja amene anawukira Mose ndi Aaroni ndipo analinso mʼgulu la otsatira Kora pamene anawukira Yehova.
10 Et lorsque la terre ouvrit sa bouche et les engloutit. Mais Coré fut enveloppé en la mort de ceux qui étaient assemblés avec lui, quand le feu consuma les deux cent cinquante hommes; et ils furent pour signe.
Nthaka inangʼambika ndi kuwameza pamodzi ndi Kora, kotero kuti gulu lawo linafa pamene moto unapsereza anthu 250 aja, nasanduka chenjezo.
11 Mais les enfants de Coré ne moururent point.
Koma ana a Kora sanafe nawo.
12 Les enfants de Siméon selon leurs familles. De Némuel, la famille des Némuélites; de Jamin, la famille des Jaminites; de Jakin, la famille des Jakinites;
Zidzukulu za Simeoni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Nemueli, fuko la Anemuele; kuchokera mwa Yamini, fuko la Ayamini; kuchokera mwa Yakini fuko la Ayakini;
13 De Zérah, la famille des Zarhites; de Saül, la famille des Saülites.
kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera; kuchokera mwa Sauli, fuko la Asauli.
14 Ce sont là les familles des Siméonites; qui furent vingt-deux mille deux cents.
Awa anali mafuko a Simeoni. Iwowa analipo amuna 22,200.
15 Les enfants de Gad selon leurs familles. De Tséphon, la famille des Tséphonites; de Haggi, la famille des Haggites; de Suni, la famille des Sunites;
Zidzukulu za Gadi mwa mafuko awo ndi izi: kuchokera mwa Zefoni, fuko la Azefoni; kuchokera mwa Hagi, fuko la Ahagi; kuchokera mwa Suni, fuko la Asuni;
16 D'Ozni, la famille des Oznites; deHéri, la famille des Hérites;
kuchokera mwa Ozini, fuko la Aozini; kuchokera mwa Eri, fuko la Aeri;
17 D'Arod, la famille des Arodites; d'Aréel, la famille des Aréélites.
kuchokera mwa Arodi, fuko la Aarodi; kuchokera mwa Arieli, fuko la a Areli.
18 Ce sont là les familles des enfants de Gad, selon leur dénombrement, qui fut de quarante mille cinq cents.
Awa ndiwo anali mafuko a Gadi. Onse amene anawerengedwa analipo 40,500.
19 Les enfants de Juda, Her, et Onan; mais Her et Onan moururent au pays de Canaan.
Eri ndi Onani anali ana aamuna a Yuda, koma anafera mu Kanaani.
20 Ainsi les enfants de Juda [distingués] par leurs familles, furent, de Séla, la famille des Sélanites; de Pharès, la famille des Pharésites; de Zara, la famille des Zarhites.
Zidzukulu za Yuda monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Sela, fuko la Asera; kuchokera mwa Perezi, fuko la Aperezi; kuchokera mwa Zera, mbumba ya Zera.
21 Et les enfants de Pharès furent, de Hetsron, la famille des Hetsronites; et de Hamul, la famille des Hamulites.
Zidzukulu za Perezi zinali izi: kuchokera mwa Hezironi, fuko la Ahezironi; kuchokera mwa Hamuli, fuko la Ahamuli.
22 Ce sont là les familles de Juda, selon leur dénombrement, qui fut de soixante et seize mille cinq cents.
Awa ndiwo anali mafuko a Yuda. Amene anawerenga analipo 76,500.
23 Les enfants d'Issacar selon leurs familles. De Tolah, la famille des Tolahites; de Puva, la famille des Puvites.
Zidzukulu za Isakara monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Tola, fuko la Atola; kuchokera mwa Puwa, fuko la Apuwa;
24 De Jasub, la famille des Jasubites; de Simron, la famille des Simronites.
kuchokera mwa Yasubu, fuko la Ayasubu. Kuchokera mwa Simironi, fuko la Asimironi.
25 Ce sont là les familles d'Issacar, selon leur dénombrement, qui fut de soixante-quatre mille trois cents.
Awa ndi amene anali a fuko la Isakara. Amene anawerengedwa analipo 64,300.
26 Les enfants de Zabulon, selon leurs familles. De Séred, la famille des Sérédites; d'Elon, la famille des Elonites; de Jahléel, la famille des Jahléélites.
Zidzukulu za Zebuloni mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Seredi, fuko la Aseredi; kuchokera mwa Eloni, fuko la Aeloni; kuchokera mwa Yahaleeli, fuko la Ayahaleeli.
27 Ce sont là les familles des Zabulonites, selon leur dénombrement, qui fut de soixante mille cinq cents.
Awa ndiwo anali mafuko a Zebuloni. Amene anawerengedwa analipo 60,500.
28 Les enfants de Joseph, selon leurs familles, furent Manassé et Ephraïm.
Zidzukulu za Yosefe mwa mafuko awo kupyolera mwa Manase ndi Efereimu zinali izi:
29 Les enfants de Manassé. De Makir, la famille des Makirites; et Makir engendra Galaad; de Galaad, la famille des Galaadites.
Zidzukulu za Manase: kuchokera mwa Makiri, fuko la Amakiri (Makiri anali abambo ake a Giliyadi); kuchokera mwa Giliyadi, fuko la Agiliyadi.
30 Ce sont ici les enfants de Galaad; de Ihézer, la famille des Ihézérites; de Hélek, la famille des Hélékites.
Izi ndizo zinali zidzukulu za Giliyadi; kuchokera mwa Iyezeri, fuko la Aiyezeri; kuchokera mwa Heleki, fuko la Aheleki;
31 D'Asriel, la famille des Asriélites; de Sékem, la famille des Sékémites.
kuchokera mwa Asirieli, fuko la Aasirieli; kuchokera mwa Sekemu, fuko la Asekemu;
32 De Semidah, la famille des Semidahites; de Hépher, la famille des Héphrites.
kuchokera mwa Semida, fuko la Asemida; kuchokera mwa Heferi, fuko la Aheferi.
33 r Tsélophcad, fils de Hépher, n'eut point de fils, mais des filles: et les noms des filles de Tsélophcad sont Mahla, Noha, Hogla, Milca, et Tirtsa.
(Zelofehadi mwana wa Heferi analibe ana aamuna koma ana aakazi okha, amene mayina awo anali: Mala, Nowa, Hogila, Milika ndi Tiriza.)
34 Ce sont là les familles de Manassé, et leur dénombrement fut de cinquante-deux mille sept cents.
Awa ndiwo anali mafuko a Manase. Amene anawerengedwa analipo 52,700.
35 Ce sont ici les enfants d'Ephraïm, selon leurs familles. De Suthélah, la famille des Suthélahites; de Béker, la famille des Bakrites; de Tahan, la famille des Tahanites.
Zidzukulu za Efereimu monga mwa mafuko awo zinali izi; kuchokera mwa Sutela, fuko la Asutela; kuchokera mwa Bekeri, fuko la Abekeri; kuchokera mwa Tahani, fuko la Atahani.
36 Et ce sont ici les enfants de Suthélah; de Héran, la famille des Héranites.
Zidzukulu za Sutela zinali izi: kuchokera mwa Erani, fuko la Aerani.
37 Ce sont là les familles des enfants d'Ephraïm, selon leur dénombrement, qui furent trente-deux mille cinq cents. Ce sont là les enfants de Joseph, selon leurs familles.
Awa ndiwo anali mafuko a Efereimu. Amene anawerengedwa analipo 32,500. Zimenezi zinali zidzukulu za Yosefe monga mwa mafuko awo.
38 Les enfants de Benjamin, selon leurs familles. De Bélah, la famille des Balhites; d'Asbel, la famille des Asbélites; d'Ahiram, la famille des Ahiramites.
Zidzukulu za Benjamini monga mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Bela, fuko la Abela; kuchokera mwa Asibeli, fuko la Aasibeli; kuchokera mwa Ahiramu, fuko la Ahiramu;
39 De Séphupham, la famille des Séphuphamites; de Hupham, la famille des Huphamites.
kuchokera mwa Sufamu, fuko la Asufamu; kuchokera mwa Hufamu, fuko la Ahufamu;
40 Et les enfants de Bélah furent Ard et Nahaman; d'Ard, la famille des Ardites; et de Nahaman, la famille des Nahamanites.
Zidzukulu za Bela kupyolera mwa Aridi ndi Naamani zinali izi: kuchokera mwa Aridi, fuko la Aaridi; kuchokera mwa Naamani, fuko la Anaamani;
41 Ce sont là les enfants de Benjamin, selon leurs familles; et leur dénombrement fut de quarante-cinq mille six cents.
Awa ndiwo anali mabanja a Benjamini. Amene nawerengedwa analipo 45,600.
42 Ce sont ici les enfants de Dan, selon leurs familles. De Suham, la famille des Suhamites; ce sont là les familles de Dan, selon leurs familles.
Zidzukulu za Dani mwa mabanja awo zinali izi: kuchokera mwa Suhamu fuko la Asuhamu. Izi zinali zidzukulu za Dani.
43 Toutes les familles des Suhamites, selon leur dénombrement, furent soixante-quatre mille, et quatre cents.
Onse a fuko la Asuhamu amene anawerengedwa analipo 64,400.
44 Les enfants d'Aser, selon leurs familles. De Jimna, la famille des Jimnaïtes; de Jisui, la famille des Jisuites; de Bériah, la famille des Bériahites.
Zidzukulu za Aseri monga mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Imina, fuko la Aimuna; kuchokera mwa Isivi, fuko la Ayisivi; kuchokera mwa Beriya, fuko la Aberiya;
45 Des enfants de Bériah, de Héber, la famille des Hébrites; de Malkiel, la famille des Malkiélites.
ndipo kupyolera mwa zidzukulu za Beriya: kuchokera mwa Heberi, fuko la Aheberi; kuchokera mwa Malikieli, fuko la Amalikieli;
46 Et le nom de la fille d'Aser, fut Sérah.
(Aseri anali ndi mwana wamkazi dzina lake Sera)
47 Ce sont là les familles des enfants d'Aser, selon leur dénombrement, qui furent cinquante-trois mille quatre cents.
Awa ndiwo anali mafuko a Aseri. Onse amene anawerengedwa analipo 53,400.
48 Les enfants de Nephthali, selon leurs familles. De Jahtséel, la famille des Jahtséélites; de Guni, la famille des Gunites.
Zidzukulu za Nafutali mwa mafuko awo zinali izi: kuchokera mwa Yahazeeli, fuko la Ayahazeeli; kuchokera mwa Guni, fuko la Aguni;
49 De Jetser la famille des Jitsrites; de Sillem, la famille des Sillémites.
kuchokera mwa Yezeri, fuko la Ayezeri; kuchokera mwa Silemu, fuko la Asilemu.
50 Ce sont là les familles de Nephthali, selon leurs familles, et leur dénombrement fut de quarante-cinq mille quatre cents.
Awa ndiwo anali mafuko a Nafutali. Onse amene anawerengedwa analipo 45,400.
51 Ce sont là les dénombrés des enfants d'Israël, qui furent six cent et un mille sept cent trente.
Chiwerengero chonse cha amuna mu Israeli chinalipo 601,730.
52 Et l'Eternel parla à Moïse, en disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
53 Le pays sera partagé à ceux-ci par héritage, selon le nombre des noms.
“Uwagawire dziko anthu awa kuti likhale cholowa chawo molingana ndi chiwerengero cha mayina awo.
54 A ceux qui sont en plus grand nombre tu donneras plus d'héritage, et à ceux qui sont en plus petit nombre tu donneras moins d'héritage; on donnera à chacun son héritage selon le nombre de ses dénombrés.
Gulu lalikulu ulipatse cholowa chachikulu, ndipo lochepa cholowa chocheperapo. Gulu lililonse lilandire cholowa chake molingana ndi chiwerengero cha amene anawerengedwa.
55 Toutefois que le pays soit divisé par sort, [et] qu'ils prennent leur héritage selon les noms des Tribus de leurs pères.
Dzikolo uligawe pochita maere. Alandire cholowa chawocho potsata mayina a mafuko a makolo awo.
56 L'héritage de chacun sera selon que le sort le montrera, et on aura égard au plus grand et au plus petit nombre.
Cholowa chawo uchigawe pakati pa fuko lalikulu ndi lalingʼono mwa maere.”
57 Et ce sont ici les dénombrés de Lévi selon leurs familles; de Guerson, la famille des Guersonites; de Kéhath, la famille des Kéhathites; de Mérari, la famille des Mérarites.
Alevi omwe anawerengedwa monga mwa mafuko awo ndi awa: kuchokera mwa Geresoni, fuko la Ageresoni; kuchokera mwa Kohati, fuko la Akohati; kuchokera mwa Merari, fuko la Amerari.
58 Ce sont donc ici les familles de Lévi; la famille des Libnites, la famille des Hébronites, la famille des Mahlites, la famille des Musites, la famille des Corhites. Or Kéhath engendra Hamram.
Awanso anali mabanja a Alevi: banja la Alibini, banja la Ahebroni, banja la Amali, banja la Amusi, fuko la Kora banja la Akohati, (Kohati anali abambo a Amramu.
59 Et le nom de la femme de Hamram, fut Jokébed, fille de Lévi, qui naquit à Lévi en Egypte, et elle enfanta à Hamram, Aaron, Moïse, et Marie leur sœur.
Dzina la mkazi wa Amramu linali Yokobedi, mdzukulu wa Levi, yemwe anabadwa mwa Alevi mu Igupto. Yokobedi anaberekera Amramu Aaroni, Mose ndi Miriamu mlongo wawo.
60 Et à Aaron naquirent Nadab, Abihu, Eléazar et Ithamar.
Aaroni anali abambo a Nadabu, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
61 Et Nadab et Abihu moururent en offrant du feu étranger devant l'Eternel.
Koma Nadabu ndi Abihu anafa pamene anapereka nsembe pamaso pa Yehova ndi moto wachilendo).
62 Et tous les dénombrés des Lévites furent vingt-trois mille, tous mâles, depuis l'âge d'un mois, et au dessus, qui ne furent point dénombrés avec les [autres] enfants d'Israël, car on ne leur donna point d'héritage entre les enfants d'Israël.
Alevi onse aamuna a mwezi umodzi kapena kuposera pamenepa analipo 23,000. Iwowo sanawerengedwe pamodzi ndi Aisraeli ena chifukwa sanalandire cholowa pakati pawo.
63 Ce sont là ceux qui furent dénombrés par Moïse et Eléazar le Sacrificateur, qui firent le dénombrement des enfants d'Israël aux campagnes de Moab, près du Jourdain de Jéricho.
Awa ndi amene anawerengedwa ndi Mose ndi Eliezara wansembe pamene ankawerenga Aisraeli pa zigwa za ku Mowabu mʼmbali mwa Yorodani ku Yeriko.
64 Entre lesquels il ne s'en trouva aucun de ceux qui avaient été dénombrés par Moïse et Aaron Sacrificateur, quand ils firent le dénombrement des enfants d'Israël au désert de Sinaï.
Mwa anthu amenewa panalibe ndi mmodzi yemwe amene anali mʼgulu la Aisraeli omwe Mose ndi wansembe Aaroni anawawerenga mʼchipululu cha Sinai;
65 Car l'Eternel avait dit d'eux, que certainement ils mourraient au désert; et ainsi il n'en resta pas un, excepté Caleb, fils de Jéphunné, et Josué, fils de Nun.
Chifukwa Yehova anali atawuza Aisraeliwo kuti adzafera ndithu mʼchipululu, ndipo palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsala kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni.

< Nombres 26 >