< Nombres 15 >
1 Puis l'Eternel parla à Moïse, en disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Parle aux enfants d'Israël, et leur dis: Quand vous serez entrés au pays où vous devez demeurer, lequel je vous donne;
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo,
3 Et que vous voudrez faire un sacrifice par feu à l'Eternel, un holocauste, ou un [autre] sacrifice, pour s'acquitter de quelque vœu, ou volontairement, ou dans vos fêtes solennelles, pour faire une offrande de bonne odeur à l'Eternel, du gros ou du menu bétail;
ndipo mukamadzapereka kwa Yehova, nsembe yotentha pa moto ya ngʼombe kapena nkhosa monga fungo lokoma kwa Yehova, kaya ndi nsembe yopsereza kapena nsembe zina, nsembe yapadera chifukwa cha lumbiro kapena nsembe yoperekedwa mwaufulu kapenanso yoperekedwa pa chikondwerero,
4 Celui qui offrira son offrande à l'Eternel, offrira avec elle un gâteau de fleur de farine d'une dixième, pétrie avec la quatrième partie d'un Hin d'huile;
munthu amene akubweretsa zopereka zake, azikapereka kwa Yehova chopereka chachakudya cholemera kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta wokwana lita imodzi.
5 Et la quatrième partie d'un Hin de vin pour l'aspersion que tu feras sur l'holocauste, ou sur [quelque autre] sacrifice pour chaque agneau.
Pamodzi ndi mwana wankhosa aliyense wa nsembe yopsereza kapena nsembe ina, muzikakonzanso lita imodzi la vinyo ngati chopereka cha chakumwa.’”
6 Que si c'est pour un bélier, tu feras un gâteau de deux dixièmes de fleur de farine, pétrie avec la troisième partie d'un Hin d'huile;
“Pamodzi ndi nkhosa yayimuna, muzikakonzanso chopereka cha chakudya cholemera makilogalamu awiri a ufa wosalala, wosakaniza ndi mafuta okwanira lita imodzi ndi theka,
7 Et la troisième partie d'un Hin de vin pour l'aspersion, que tu offriras en bonne odeur à l'Eternel.
ndi vinyo wokwanira lita imodzi ndi theka ngati chopereka cha chakumwa. Muzikapereka monga nsembe yopereka fungo lokoma kwa Yehova.
8 Et si tu sacrifies un veau en holocauste, ou [tel autre] sacrifice, pour s'acquitter de quelque vœu important, ou pour faire un sacrifice de prospérités à l'Eternel;
“‘Pamene mukukonza mwana wangʼombe wamwamuna kuti akhale nsembe yopsereza kapena nsembe ina iliyonse: ya lumbiro lapadera kapena nsembe yachiyanjano kwa Yehova,
9 On offrira avec le veau un gâteau de trois dixièmes de fleur de farine, pétrie avec la moitié d'un Hin d'huile.
pamodzi ndi mwana wangʼombe wamwamunayo muzibweretsa nsembe yachakudya yolemera makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta okwana malita awiri.
10 Et tu offriras la moitié d'un Hin de vin pour l'aspersion, en offrande faite par feu de bonne odeur à l'Eternel.
Komanso muzibweretsa vinyo wokwanira malita awiri monga chopereka chachakumwa. Imeneyi idzakhala chopereka chotentha pa moto kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova.
11 On en fera de même pour chaque taureau, chaque bélier, et chaque petit d'entre les brebis et d'entre les chèvres.
Ngʼombe yayimuna iliyonse kapena nkhosa yayimuna iliyonse, mwana wankhosa aliyense kapena mbuzi yayingʼono, zizikonzedwa motere.
12 Selon le nombre que vous en sacrifierez, vous ferez ainsi à chacun, selon leur nombre.
Ngakhale zingachuluke chotani, chitani izi kwa iliyonse ya nyamazo.
13 Tous ceux qui sont nés au pays feront ces choses de cette manière, en offrant un sacrifice fait par feu en bonne odeur à l'Eternel.
“‘Mbadwa iliyonse ya mu Israeli izichita zimenezi pamene ibweretsa nsembe yotentha pa moto kuti ikhale fungo lokoma kwa Yehova.
14 Que si quelque étranger, ou [quelque autre] parmi vous, qui faisant son séjour avec vous, en vos âges, fait un sacrifice par feu en bonne odeur à l'Eternel, il fera comme vous ferez.
Ku mibado yanu yonse ya mʼtsogolo, pamene mlendo kapena wina aliyense wokhala pakati panu apereka chopereka chotentha pa moto kuti chikhale fungo lokoma kwa Yehova, azichita mofanana ndi momwe inu mumachitira.
15 Ô assemblée! il y aura une même ordonnance pour vous et pour l'étranger qui fait son séjour [parmi vous], il y aura une même ordonnance perpétuelle en vos âges; il en sera de l'étranger comme de vous en la présence de l'Eternel.
Gulu lonse likhale ndi malamulo ofanana a inu kapena mlendo wokhala pakati panu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya kwa mibado imene ikubwera. Inuyo ndi mlendo mudzakhala wofanana pamaso pa Yehova.
16 Il y aura une même loi et un même droit pour vous et pour l'étranger qui fait son séjour parmi vous.
Mudzakhale ndi malamulo ndi miyambo yofanana, inuyo ndi mlendo wokhala pakati panu.’”
17 L'Eternel parla aussi à Moïse, en disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
18 Parle aux enfants d'Israël, et leur dis: Quand vous serez entrés au pays où je vous ferai entrer;
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo unene kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukutengeraniko
19 Et que vous mangerez du pain du pays, vous en offrirez à l'Eternel une offrande élevée.
ndipo mukakadya chakudya cha mʼdzikolo, mukapereke gawo lina kwa Yehova monga chopereka.
20 Vous offrirez en offrande élevée un gâteau pour les prémices de votre pâte; vous l'offrirez à la façon de l'offrande élevée prise de l'aire.
Pa buledi wanu woyamba, mukapereke mmodzi monga nsembe, ngati chopereka chochokera ku malo wopunthira tirigu.
21 Vous donnerez donc en vos âges à l'Eternel une offrande élevée, prise des prémices de votre pâte.
Pa mibado yanu yonse muzidzapereka chopereka ichi kwa Yehova kuchokera ku zakudya zanu zoyamba za mʼnthaka.
22 Et lorsque vous aurez péché par erreur, et que vous n'aurez pas fait tous ces commandements que l'Eternel a donnés à Moïse;
“‘Ndipo ngati muchimwa mosadziwa posasunga ena mwa malamulo awa amene Yehova wapereka kwa Mose,
23 Tout ce que l'Eternel vous a commandé par le moyen de Moïse, depuis le jour que l'Eternel a commencé de donner ses commandements, et dans la suite en vos âges;
lina lililonse mwa malamulo a Yehova amene wapereka kwa inu kudzera mwa Mose, kuyambira tsiku limene Yehova anawapereka mpaka mibado ya mʼtsogolo,
24 S'il arrive que la chose ait été faite par erreur, sans que l'assemblée l'ait aperçue, toute l'assemblée sacrifiera en holocauste en bonne odeur à l'Eternel, un veau pris du troupeau, avec son gâteau et son aspersion, selon l'ordonnance, et un jeune bouc en offrande pour le péché.
ndipo ngati zimenezi zachitika osati mwadala ndipo gulu lonse silinadziwe, zikatero gulu lonselo lipereke mwana wangʼombe wamwamuna monga nsembe yopsereza kuti likhale fungo lokoma kwa Yehova pamodzinso ndi chopereka chachakudya ndi chopereka cha chakumwa ndi mbuzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo potsata zimene zinalamulidwa.
25 Ainsi le Sacrificateur fera propitiation pour toute l'assemblée des enfants d'Israël, et il leur sera pardonné; parce que c'est une chose arrivée par erreur; et ils amèneront devant l'Eternel leur offrande qui doit être un sacrifice fait par feu à l'Eternel, et [l'offrande pour] leur péché, à cause de leur erreur.
Wansembe apereke nsembe yopepesera machimo a gulu lonse la Aisraeli, ndipo adzakhululukidwa, pakuti linali tchimo lochita mosadziwa. Ndipo chifukwa cha tchimo lawolo, abweretse kwa Yehova nsembe yotentha pa moto ndi nsembe yopepesera machimo.
26 Alors il sera pardonné à toute l'assemblée des enfants d'Israël, et à l'étranger qui fait son séjour parmi eux, parce que cela est arrivé à tout le peuple par erreur.
Gulu lonse la Aisraeli ndi alendo okhala pakati pawo adzakhululukidwa chifukwa anthu onsewo anachimwa mosadziwa.
27 Que si une personne seule a péché par erreur, elle offrira [en offrande pour] le péché une chèvre d'un an.
“‘Koma ngati munthu mmodzi achimwa mosadziwa, ayenera kubweretsa mbuzi yayikazi ya chaka chimodzi kuti ikhale nsembe yopepesera machimo.
28 Et le Sacrificateur fera propitiation pour la personne qui aura péché par erreur, de ce qu'elle aura péché par erreur devant l'Eternel, [et] faisant propitiation pour elle, il lui sera pardonné.
Wansembe apereke nsembe yopepesera machimowo pamaso pa Yehova chifukwa cha munthu yemwe anachimwa mosadziwayo. Nsembe yopepesera tchimo lakelo ikaperekedwa, munthuyo adzakhululukidwa.
29 Il y aura une même loi pour celui qui aura fait quelque chose par erreur, tant pour celui qui est né au pays des enfants d'Israël, que pour l'étranger qui fait son séjour parmi eux.
Lamulo lomweli ligwiritsidwe ntchito kwa aliyense wochimwa mosadziwa, kaya ndi mbadwa ya mu Israeli kapena mlendo.
30 Mais quant à celui qui aura péché par fierté, tant celui qui est né au pays, que l'étranger, il a outragé l'Eternel; cette personne-là sera retranchée du milieu de son peuple;
“‘Koma aliyense amene achimwa mwadala, kaya ndi mbadwa kapena mlendo, nachitira chipongwe Yehova, ameneyo achotsedwe ndithu pakati pa anthu ake.
31 Parce qu'il a méprisé la parole de l'Eternel, et qu'il a enfreint son commandement. Cette personne donc sera certainement retranchée; son iniquité est sur elle.
Popeza wanyoza mawu a Yehova ndi kuphwanya malamulo ake. Munthu ameneyo achotsedwe ndithu, kuchimwa kwake kudzakhala pa iyeyo.’”
32 Or les enfants d'Israël étant au désert, trouvèrent un homme qui ramassait du bois le jour du Sabbat.
Aisraeli ali mʼchipululu, munthu wina anapezeka akutola nkhuni tsiku la Sabata.
33 Et ceux qui le trouvèrent ramassant du bois, l'amenèrent à Moïse et à Aaron, et à toute l'assemblée.
Amene anamupeza akutola nkhunizo anabwera naye kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa gulu lonse
34 Et on le mit en garde; car il n'avait pas encore été déclaré ce qu'on lui devait faire.
ndipo anamutsekera mʼndende chifukwa sankadziwa choti achite naye.
35 Alors l'Eternel dit à Moïse: On punira de mort cet homme-là, et toute l'assemblée le lapidera hors du camp.
Pamenepo Yehova anawuza Mose kuti, “Munthu ameneyu ayenera kuphedwa. Gulu lonse liyenera kumugenda ndi miyala kunja kwa msasa.”
36 Toute l'assemblée donc le mena hors du camp, et ils le lapidèrent, et il mourut; comme l'Eternel l'avait commandé à Moïse.
Choncho gululo linamutengera kunja kwa msasa ndi kumupha pomugenda ndi miyala, monga momwe Yehova analamulira Mose.
37 Et l'Eternel parla à Moïse, en disant:
Yehova anawuza Mose kuti,
38 Parle aux enfants d'Israël, et leur dis: Qu'ils se fassent d'âge en âge des bandes aux pans de leurs vêtements, et qu'ils mettent sur les bandes des pans [de leurs vêtements] un cordon de couleur de pourpre.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pa mibado yanu yonse muzisokerera mphonje pa ngodya za zovala zanu ndipo pa ngodya ya mphonje iliyonse azisokererapo chingwe chobiriwira.
39 Ce cordon sera sur la bande, et en le voyant il vous souviendra de tous les commandements de l'Eternel, afin que vous les fassiez, et que vous ne suiviez point les pensées de votre cœur, ni les désirs de vos yeux, en suivant lesquels vous paillardez.
Mudzakhala ndi mphonje zimenezi kuti mukaziona muzikakumbukira malamulo onse a Yehova ndi kuwamvera kuti musamatsatenso zilakolako za mʼmitima mwanu ndi za maso anu.
40 Afin que vous vous souveniez de tous mes commandements, et que vous les fassiez, et que vous soyez saints à votre Dieu.
Motero mudzakumbukira kumvera malamulo anga ndipo mudzakhala opatulikira a Mulungu wanu.
41 Je suis l'Eternel votre Dieu, qui vous ai retirés du pays d'Egypte, pour être votre Dieu; je suis l'Eternel votre Dieu.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”