< Malachie 1 >

1 La charge de la parole de l'Eternel contre Israël, par le moyen de Malachie.
Uthenga: Mawu a Yehova kwa Israeli kudzera mwa Malaki.
2 Je vous ai aimés, a dit l'Eternel; et vous avez dit: En quoi nous as-tu aimés? Esaü n'était-il pas frère de Jacob, dit l'Eternel? Or j'ai aimé Jacob;
Yehova akuti, “Ine ndakukondani. Koma inu mukufunsa kuti, ‘Kodi mwatikonda motani?’” Yehova akuti, “Kodi Esau sanali mʼbale wake wa Yakobo? Komatu Ine ndinakonda Yakobo,
3 Mais j'ai haï Esaü, et j'ai mis ses montagnes en désolation, et son héritage pour les dragons du désert.
koma ndinamuda Esau, ndipo dziko lake lamapiri ndalisandutsa chipululu ndipo cholowa chake ndasiyira ankhandwe a mʼchipululu.”
4 Que si Edom dit: Nous avons été appauvris, mais nous retournerons, et rebâtirons les lieux ruinés, l'Eternel des armées dit ainsi: Ils rebâtiront, mais je détruirai, et on les appellera: Pays de méchanceté, et le peuple contre lequel l'Eternel est indigné à toujours.
Mwina Edomu nʼkunena kuti, “Ngakhale taphwanyidwa, tidzamanganso mʼmabwinja.” Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Iwo angathe kumanganso, koma Ine ndidzazigwetsanso. Iwo adzatchedwa dziko loyipa, la anthu amene Yehova wayipidwa nawo mpaka muyaya.
5 Vos yeux le verront, et vous direz: L'Eternel se magnifie sur [ceux qui sont] aux frontières d'Israël.
Inu mudzaziona zimenezi ndi maso anu ndipo mudzati, ‘Yehova ndi Wamkulu, ukulu wake umafika ngakhale kunja kwa malire a Israeli!’
6 Le fils honore le père, et le serviteur son Seigneur; si donc je suis Père, où [est] l'honneur qui m'appartient? et si je suis Seigneur, où est la crainte [qu'on a] de moi? a dit l'Eternel des armées, à vous Sacrificateurs, qui méprisez mon Nom. Et vous avez dit: En quoi avons-nous méprisé ton Nom?
“Mwana amalemekeza abambo ake, ndipo wantchito amaopa abwana ake. Ngati Ine ndine abambo anu, ulemu wanga uli kuti? Ngati ndine mbuye wanu, nanga kundiopa kuli kuti?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Ndinu, inu ansembe, amene mumanyoza dzina langa. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi timanyoza dzina lanu bwanji?’
7 Vous offrez sur mon autel du pain souillé, et vous dites: En quoi t'avons-nous déshonoré? C'est en ce que vous dites: La table de l'Eternel est contemplative.
“Inu mwanyoza dzina langa popereka chakudya chodetsedwa pa guwa langa lansembe. “Komatu mukufunsa kuti, ‘Kodi ife takunyozani bwanji?’ “Mwandinyoza ponena kuti tebulo la Yehova ndi lonyozeka.
8 Et quand vous amenez une bête aveugle pour la sacrifier, n'y a-t-il point de mal [en cela?] Et quand vous l'amenez boiteuse ou malade, n'y a-t-il point de mal [en cela?] Présente-la à ton Gouverneur, t'en saura-t-il gré, ou te recevra-t-il favorablement? a dit l'Eternel des armées.
Mukamapereka nsembe nyama zosaona, kodi sicholakwa? Mukamapereka nsembe nyama zachilema kapena zodwala, kodi sicholakwa? Kayeseni kuzipereka kwa bwanamkubwa wanu! Kodi akasangalatsidwa nanu? Kodi akazilandira? Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
9 Maintenant donc suppliez le [Dieu] Fort, afin qu'il ait pitié de nous; cela [venant] de votre main, vous recevra-t-il favorablement? a dit l'Eternel des armées.
“Tsopano tayesani kupempha Mulungu kuti akuchitireni chifundo. Kodi ndi zopereka zotere mʼmanja mwanu, Iye angakulandireni?” Akutero Yehova Wamphamvuzonse.
10 Qui est aussi celui d'entre vous qui ferme les portes? car n'est-ce pas en vain que vous faites brûler le feu sur mon autel? Je ne prends point de plaisir en vous, a dit l'Eternel des armées; et je n'aurai point pour agréable l'oblation de vos mains.
“Ndikulakalaka mmodzi wa inu akanatseka zitseko za Nyumba ya Mulungu, kuti musayatsemo moto pachabe pa guwa langa lansembe! Ine sindikukondwera nanu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse, “ndipo Ine sindidzalandira zopereka za mʼmanja mwanu.
11 Mais depuis le soleil levant jusqu'au soleil couchant, mon Nom sera grand parmi les nations, et en tous lieux on offrira à mon Nom le parfum, et une oblation pure; car mon Nom sera grand parmi les nations, a dit l'Eternel des armées.
Dzina langa lidzalemekezedwa pakati pa mitundu ya anthu, kuchokera kummawa mpaka kumadzulo. Mʼmalo monse adzapereka nsembe zofukiza ndi zopereka zangwiro mʼdzina langa, chifukwa dzina langa lidzakhala lalikulu pakati pa mitundu ya anthu,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
12 Mais vous l'avez profané, en disant: La table de l'Eternel est souillée, elle et ce qui en revient; sa viande est méprisable.
“Koma inu mumalinyoza ponena kuti tebulo la Ambuye, ‘ndi lodetsedwa,’ ndipo chakudya chake, ‘nʼchonyozeka!’
13 Vous dites aussi: Voici, ô que de travail! et vous soufflez dessus, a dit l'Eternel des armées. Vous amenez ce qui a été dérobé, ce qui est boiteux, et malade, vous l'amenez, dis-je, pour m'être offert. Accepterai-je cela de vos mains, a dit l'Eternel?
Ndipo inu mumati, ‘Ndi zotopetsa zimenezi!’ Ndipo mumandinyogodola Ine,” akutero Yehova Wamphamvuzonse. “Pamene inu mubweretsa nyama zakuba, zolumala kapena zodwala ndi kupereka nsembe, kodi Ine ndizilandire kuchokera mʼmanja mwanu?” Akutero Yehova.
14 C'est pourquoi, maudit soit l'homme trompeur, qui ayant un mâle en son troupeau, et faisant un vœu, sacrifie à l'Eternel ce qui est défectueux; car je suis un grand Roi, a dit l'Eternel des armées, et mon Nom est redouté parmi les nations.
“Atembereredwe munthu wachinyengo amene ali ndi nyama yayimuna yabwino mʼgulu la ziweto zake ndipo analumbira kuyipereka, koma mʼmalo mwake nʼkupereka nsembe kwa Ambuye nyama yosayenera. Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Pakuti ndine mfumu yayikulu, dzina langa liyenera kuopedwa pakati pa anthu a mitundu yonse.’”

< Malachie 1 >