< Luc 18 >
1 Il leur proposa aussi une parabole, [pour faire voir] qu'il faut toujours prier, et ne se lasser point;
Kenaka Yesu anawuza ophunzira ake fanizo kuwaonetsa kuti iwo ayenera kumapemphera nthawi zonse ndikuti asafowoke.
2 Disant: Il y avait dans une ville un juge, qui ne craignait point Dieu, et qui ne respectait personne.
Iye anati, “Mʼmudzi wina munali woweruza wosaopa Mulungu ngakhalenso kulabadira za anthu.
3 Et dans la même ville il y avait une veuve, qui l'allait souvent trouver, et lui dire: fais-moi justice de ma partie adverse.
Ndipo panali mkazi wamasiye mʼmudzimo amene ankabwerabwera kwa iye ndi dandawulo lake kuti, ‘Mundiweruze mlandu mwachilungamo pakati pa ine ndi otsutsana nane.’
4 Pendant longtemps il n'en voulut rien faire. Mais après cela il dit en lui-même: quoique je ne craigne point Dieu, et que je ne respecte personne,
“Kwa nthawi yayitali woweruzayo ankakana. Koma pa mapeto analingalira nati, ‘Ngakhale kuti sindiopa Mulungu kapena kulabadira za anthu,
5 Néanmoins, parce que cette veuve me donne de la peine, je lui ferai justice, de peur qu'elle ne vienne perpétuellement me rompre la tête.
koma chifukwa chakuti mkazi wamasiyeyu akundivutitsa, ine ndimuweruzira mlandu wake mwachilungamo kuti asanditopetse ndi kubwerabwera kwakeko!’”
6 Et le Seigneur dit: écoutez ce que dit le juge inique.
Ndipo Ambuye anati, “Tamvani zimene woweruza wopanda chilungamoyu wanena.
7 Et Dieu ne vengera-t-il point ses élus qui crient à lui jour et nuit, quoiqu'il diffère de s'irriter pour l'amour d'eux?
Tsono chingamuletse nʼchiyani Mulungu kubweretsa chilungamo kwa osankhika ake, amene amalira kwa Iye usana ndi usiku? Kodi adzapitirirabe osawalabadira?
8 Je vous dis que bientôt il les vengera. Mais quand le Fils de l'homme viendra, [pensez-vous] qu'il trouve de la foi sur la terre.
Ine ndikukuwuzani inu, adzaonetsetsa kuti alandire chilungamo, ndiponso mofulumira. Komabe, pamene Mwana wa Munthu akubwera, kodi adzapeza chikhulupiriro pa dziko lapansi?”
9 Il dit aussi cette parabole à quelques-uns qui se confiaient en eux-mêmes d'être justes, et qui tenaient les autres pour rien.
Yesu ananena fanizoli kwa amene amadzikhulupirira mwa iwo okha kuti anali wolungama nanyoza ena onse.
10 Deux hommes montèrent au Temple pour prier, l'un Pharisien; et l'autre, péager.
“Anthu awiri anapita ku Nyumba ya Mulungu kukapemphera, wina Mfarisi ndi winayo wolandira msonkho.
11 Le Pharisien se tenant à l'écart priait en lui-même en ces termes: ô Dieu! je te rends grâces de ce que je ne suis point comme le reste des hommes, [qui sont] ravisseurs, injustes, adultères, ni même comme ce péager.
Mfarisiyo anayimirira ndipo anapemphera za iye mwini kuti, ‘Mulungu, ine ndikuyamika kuti sindili ngati anthu ena onse, achifwamba, ochita zoyipa, achigololo, sindilinso ngati wolandira msonkhoyu.
12 Je jeûne deux fois la semaine, [et] je donne la dîme de tout ce que je possède.
Ine ndimasala kudya kawiri pa Sabata ndipo ndimapereka chakhumi pa zonse ndimapeza.’
13 Mais le péager se tenant loin, n'osait pas même lever les yeux vers le ciel, mais frappait sa poitrine, en disant: ô Dieu! sois apaisé envers moi qui suis pécheur!
“Koma wolandira msonkhoyo ali chiyimire potero, sanathe nʼkomwe kuyangʼana kumwamba; koma anadziguguda pachifuwa ndipo anati, ‘Mulungu, chitireni chifundo, ine wochimwa.’
14 Je vous dis que celui-ci descendit en sa maison justifié, plutôt que l'autre; car quiconque s'élève, sera abaissé, et quiconque s'abaisse, sera élevé.
“Ine ndikukuwuzani kuti munthu wolandira msonkhoyu, osati Mfarisiyu, anapita kwawo atalungamitsidwa pamaso pa Mulungu. Chifukwa chake, aliyense wodzikweza adzachepetsedwa, ndipo wodzichepetsa adzakwezedwa.”
15 Et quelques-uns lui présentèrent aussi de petits enfants, afin qu'il les touchât, ce que les Disciples voyant, ils censurèrent [ceux qui les présentaient].
Anthu amabweretsanso ana aangʼono kwa Yesu kuti awadalitse. Ophunzira ataona izi, anawadzudzula.
16 Mais Jésus les ayant fait venir à lui, dit: laissez venir à moi les petits enfants, et ne les en empêchez point; car le Royaume de Dieu est pour ceux qui leur ressemblent.
Koma Yesu anayitana anawo kuti abwere kwa Iye nati, “Lolani ana abwere kwa Ine ndipo musawatsekereze, pakuti ufumu wa Mulungu uli wa anthu otere.
17 En vérité je vous dis: que quiconque ne recevra point comme un enfant le Royaume de Dieu, n'y entrera point.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene salandira ufumu wa Mulungu ngati mwana wamngʼono, sadzalowamo.”
18 Et un Seigneur l'interrogea, disant: Maître qui es bon, que ferai-je pour hériter la vie éternelle? (aiōnios )
Oweruza wina wake anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi abwino, ndichite chiyani kuti ndilandire moyo wosatha?” (aiōnios )
19 Jésus lui dit: pourquoi m'appelles-tu bon? Il n'y a nul bon qu'un seul, [qui est] Dieu.
Yesu anamuyankha kuti, “Chifukwa chiyani ukunditcha wabwino, palibe wabwino kupatula Mulungu yekha.
20 Tu sais les Commandements: tu ne commettras point adultère. Tu ne tueras point. Tu ne déroberas point. Tu ne diras point faux témoignage. Honore ton père et ta mère.
Iwe umadziwa malamulo: ‘Usachite chigololo, usaphe, usabe, usapereke umboni wonama, lemekeza abambo ndi amayi ako.’”
21 Et il lui dit: j'ai gardé toutes ces choses dès ma jeunesse.
Iye anati, “Zonsezi ndinasunga kuyambira ndili mnyamata.”
22 Et quand Jésus eut entendu cela, il lui dit: il te manque encore une chose: vends tout ce que tu as, et le distribue aux pauvres, et tu auras un trésor au ciel; puis viens, et me suis.
Yesu atamva izi, anati kwa iye, “Ukusowabe chinthu chimodzi: Gulitsa zonse zimene uli nazo ndipo uzipereke kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Kenaka ubwere, nunditsate ine.”
23 Mais lui ayant entendu ces choses devint fort triste, car il était extrêmement riche.
Atamva zimenezi, anakhumudwa kwambiri chifukwa anali munthu wachuma chambiri.
24 Et Jésus voyant qu'il était devenu fort triste, dit: qu'il est malaisé que ceux qui ont des biens entrent dans le Royaume de Dieu!
Yesu anamuyangʼana nati, “Nʼkwapatali kwambiri kuti anthu achuma akalowe mu ufumu wa Mulungu!
25 Il est certes plus aisé qu'un chameau passe par le trou d'une aiguille, qu'il ne l'est qu'un riche entre dans le Royaume de Dieu.
Ndithudi, nʼkwapafupi kuti ngamira idutse pa kabowo ka zingano kusiyana ndi munthu wachuma kulowa mu ufumu wa Mulungu.”
26 Et ceux qui entendirent cela, dirent: Et qui peut donc être sauvé?
Amene anamva izi anafunsa kuti, “Nanga ndani amene angapulumuke?”
27 Et il leur dit: les choses qui sont impossibles aux hommes sont possibles à Dieu.
Yesu anayankha kuti, “Zinthu zosatheka ndi anthu zimatheka ndi Mulungu.”
28 Et Pierre dit: voici, nous avons tout quitté, et nous t'avons suivi.
Petro anati kwa Iye, “Ife tinasiya zonse tinali nazo kutsatira Inu!”
29 Et il leur dit: en vérité je vous dis, qu'il n'y en a pas un qui ait quitté sa maison, ou ses parents, ou ses frères, ou sa femme, ou ses enfants pour l'amour du Royaume de Dieu,
Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti palibe amene anasiya nyumba kapena mkazi kapena abale kapena makolo kapena ana chifukwa cha ufumu wa Mulungu
30 Qui ne reçoive beaucoup plus en ce temps-ci, et au siècle à venir la vie éternelle. (aiōn , aiōnios )
adzalephera kulandira mowirikiza mʼmoyo uno, ndi mʼmoyo ukubwerawo, moyo wosatha.” (aiōn , aiōnios )
31 Puis Jésus prit à part les douze, et il leur dit: voici, nous montons à Jérusalem, et toutes les choses qui sont écrites par les Prophètes touchant le Fils de l'homme, seront accomplies.
Yesu anatengera khumi ndi awiriwo pambali ndi kuwawuza kuti, “Taonani ife tikupita ku Yerusalemu, ndipo zonse zimene zalembedwa ndi Aneneri za Mwana wa Munthu zidzakwaniritsidwa.
32 Car il sera livré aux Gentils; il sera moqué, et injurié, et on lui crachera au visage.
Iye adzaperekedwa kwa anthu a mitundu ina. Ndipo adzamuchita chipongwe, adzamunyoza, adzamulavulira,
33 Et après qu'ils l'auront fouetté, ils le feront mourir; mais il ressuscitera le troisième jour.
adzamukwapula ndi kumupha. Tsiku lachitatu Iye adzaukanso.”
34 Mais ils ne comprirent rien de tout cela, et ce discours était si obscur pour eux qu'ils ne comprirent point ce qu'il leur disait.
Ophunzira sanazindikire china chilichonse cha izi. Tanthauzo lake linabisika kwa iwo, ndipo sanadziwe chimene Iye amayankhula.
35 Or il arriva comme il approchait de Jéricho, qu'il y avait un aveugle assis près du chemin, et qui mendiait.
Yesu atayandikira ku Yeriko, munthu wina wosaona amene amakhala pambali pa msewu namapempha,
36 Et entendant la multitude qui passait, il demanda ce que c'était.
anamva gulu la anthu likudutsa. Iye anafunsa chomwe chimachitika.
37 Et on lui dit que Jésus le Nazarien passait.
Iwo anamuwuza kuti “Yesu wa ku Nazareti akudutsa.”
38 Alors il cria, disant: Jésus, Fils de David, aie pitié de moi!
Iye anayitana mofuwula, “Yesu Mwana wa Davide, mundichitire chifundo!”
39 Et ceux qui allaient devant, le reprenaient, afin qu'il se tût; mais il criait beaucoup plus fort: Fils de David, aie pitié de moi!
Iwo amene amamutsogolera njira anamudzudzula ndi kumuwuza kuti akhale chete, koma iye anafuwulabe, “Mwana wa Davide, chitireni chifundo!”
40 Et Jésus s'étant arrêté commanda qu'on le lui amenât; et quand il se fut approché, il l'interrogea,
Yesu anayima nalamula kuti abwere naye kwa Iye. Atabwera pafupi, Yesu anamufunsa kuti,
41 Disant: que veux-tu que je te fasse? Il répondit: Seigneur, que je recouvre la vue.
“Kodi ukufuna kuti ndikuchitire chiyani?” Iye anayankha kuti, “Ambuye, ine ndifuna ndionenso.”
42 Et Jésus lui dit: recouvre la vue; ta foi t'a sauvé.
Yesu anati kwa iye, “Onanso; chikhulupiriro chako chakupulumutsa.”
43 Et à l'instant il recouvra la vue; et il suivait [Jésus], glorifiant Dieu. Et tout le peuple voyant cela, en loua Dieu.
Nthawi yomweyo anaonanso ndipo anayamba kumutsatira Yesu, akulemekeza Mulungu. Anthu onse ataona izi, iwonso analemekeza Mulungu.