< Lamentations 3 >
1 [Aleph.] Je suis l’homme qui ai vu l’affliction par la verge de sa fureur.
Ine ndine munthu amene ndaona masautso ndi ndodo ya ukali wake.
2 Il m’a conduit et amené dans les ténèbres, et non dans la lumière.
Wandipititsa kutali ndipo wandiyendetsa mu mdima osati mʼkuwala;
3 Certes il s’est tourné contre moi, il a tous les jours tourné sa main [contre moi].
zoonadi anandikantha ndi dzanja lake mobwerezabwereza tsiku lonse.
4 [Beth.] Il a fait vieillir ma chair et ma peau, il a brisé mes os.
Wakalambitsa khungu langa ndi mnofu wanga, ndipo waphwanya mafupa anga.
5 Il a bâti contre moi, et m’a environné de fiel et de travail.
Wandizinga ndi kundizungulira ndi zowawa ndi zolemetsa.
6 Il m’a fait tenir dans des lieux ténébreux, comme ceux qui sont morts dès longtemps.
Wandikhazika mu mdima ngati amene anafa kale.
7 [Guimel.] Il a fait une cloison autour de moi, afin que je ne sorte point; il a appesanti mes fers.
Wandimangira khoma kotero kuti sindingathawe, wandimanga ndi maunyolo.
8 Même quand je crie et que j’élève ma voix, il rejette ma requête.
Ngakhale pamene ndifuwula kapena kupempha chithandizo, amakana pemphero langa.
9 Il a fait un mur de pierres de taille [pour fermer] mes chemins, il a renversé mes sentiers.
Wanditsekera njira yanga ndi miyala yosema; ndipo wakhotetsa tinjira tanga.
10 [Daleth.] Ce m’est un ours qui est aux embûches, et un lion qui se tient dans un lieu caché.
Wandidikirira ngati chimbalangondo, wandibisalira ngati mkango.
11 Il a détourné mes chemins, et m’a mis en pièces, il m’a rendu désolé.
Wandikokera pambali ndi kundingʼambangʼamba, ndipo wandisiya wopanda thandizo.
12 Il a tendu son arc, et m’a mis comme une butte pour la flèche.
Wakoka uta wake ndipo walunjikitsa mivi yake pa ine.
13 [He.] Il a fait entrer dans mes reins les flèches dont son carquois est plein.
Walasa mtima wanga ndi mivi ya mʼphodo mwake.
14 J’ai été en risée à tous les peuples, et leur chanson, tout le jour.
Ndinakhala choseketsa cha anthu anga onse; amandinyodola mʼnyimbo zawo tsiku lonse.
15 Il m’a rassasié d’amertume, il m’a enivré d’absinthe.
Wandidyetsa zowawa ndipo wandimwetsa ndulu.
16 [Vau.] Il m’a cassé les dents avec du gravier, il m’a couvert de cendre;
Wathyola mano anga ndi miyala; wandiviviniza mʼfumbi;
17 Tellement que la paix s’est éloignée de mon âme; j’ai oublié ce que c’est que d’être à son aise.
Wandichotsera mtendere; ndayiwala kuti kupeza bwino nʼchiyani.
18 Et j’ai dit: ma force est perdue, et mon espérance aussi que j’avais en l’Eternel.
Choncho ndikuti, “Ulemerero wanga wachoka ndi zonse zimene ndimayembekeza kwa Yehova.”
19 [Zajin.] Souviens-toi de mon affliction, et de mon pauvre état, qui n’est qu’absinthe et que fiel.
Kukumbukira masautso anga ndi kusowa pokhala, zili ngati zowawa ndi ndulu.
20 Mon âme s’[en] souvient sans cesse, et elle est abattue au dedans de moi.
Ine ndikuzikumbukira bwino izi, ndipo moyo wanga wathedwa mʼkati mwanga.
21 [Mais] je rappellerai ceci en mon cœur, [et] c’est pourquoi j’aurai espérance;
Komabe ndimakumbukira zimenezi, nʼchifukwa chake ndili ndi chiyembekezo.
22 [Heth.] Ce sont les gratuités de l’Eternel que nous n’avons point été consumés, parce que ses compassions ne sont point taries.
Ife sitinawonongekeretu chifukwa chikondi cha Yehova ndi chachikulu, ndi chifundo chake ndi chosatha.
23 Elles se renouvellent chaque matin; [c’est] une chose grande que ta fidélité.
Zimaoneka zatsopano mmawa uliwonse; kukhulupirika kwanu nʼkwakukulu.
24 L’Eternel est ma portion, dit mon âme, c’est pourquoi j’aurai espérance en lui.
Mu mtima mwanga ndimati, “Yehova ndiye zanga zonse; motero ndimamuyembekezera.”
25 [Teth.] L’Eternel est bon à ceux qui s’attendent à lui, [et] à l’âme qui le recherche.
Yehova ndi wabwino kwa amene amayembekezera Iye, kwa munthu amene amafunafuna Iyeyo;
26 C’est une chose bonne qu’on attende, même en se tenant en repos, la délivrance de l’Eternel.
nʼkwabwino kudikira chipulumutso cha Yehova modekha.
27 C’est une chose bonne à l’homme de porter le joug en sa jeunesse.
Nʼkwabwino kuti munthu asenze goli pamene ali wamngʼono.
28 [Jod.] Il est assis solitaire et se tient tranquille, parce qu’on l’a chargé sur lui.
Akhale chete pa yekha, chifukwa Yehova wamusenzetsa golilo.
29 Il met sa bouche dans la poussière, si peut-être il y aura quelque espérance.
Abise nkhope yake mʼfumbi mwina chiyembekezo nʼkukhalapobe.
30 Il présente la joue à celui qui le frappe; il est accablé d’opprobre.
Apereke tsaya lake kwa iye amene angamumenye, ndipo amuchititse manyazi.
31 [Caph.] Car le Seigneur ne rejette point à toujours.
Chifukwa Ambuye satayiratu anthu nthawi zonse.
32 Mais s’il afflige quelqu’un, il en a aussi compassion selon la grandeur de ses gratuités.
Ngakhale amabweretsa zowawa, Iye adzawachitira chifundo, chifukwa chikondi chake ndi chosatha.
33 Car ce n’est pas volontiers qu’il afflige et contriste les fils des hommes.
Pakuti sabweretsa masautso mwadala, kapena zowawa kwa ana a anthu.
34 [Lamed.] Lorsqu’on foule sous ses pieds tous les prisonniers du monde;
Kuphwanya ndi phazi a mʼndende onse a mʼdziko,
35 Lorsqu’on pervertit le droit de quelqu’un en la présence du Très-haut;
kukaniza munthu ufulu wake pamaso pa Wammwambamwamba,
36 Lorsqu’on fait tort à quelqu’un dans son procès, le Seigneur ne le voit-il point?
kumana munthu chiweruzo cholungama— kodi Ambuye saona zonsezi?
37 [Mem.] Qui est-ce qui dit que cela a été fait, [et] que le Seigneur ne l’[a] point commandé?
Kodi ndani angayankhule zinthu nʼkuchitika ngati Ambuye sanavomereze?
38 Les maux, et les biens ne procèdent-ils point de l’ordre du Très-haut?
Kodi zovuta ndi zabwino sizituluka mʼkamwa mwa Wammwambamwamba?
39 Pourquoi se dépiterait l’homme vivant, l’homme, [dis-je], à cause de ses péchés?
Kodi nʼchifukwa chiyani munthu aliyense wamoyo amadandaula akalangidwa chifukwa cha machimo ake?
40 [Nun.] Recherchons nos voies, et [les] sondons, et retournons jusqu’à l’Eternel.
Tiyeni tisanthule ndi kuyesa njira zathu, ndipo tiyeni tibwerere kwa Yehova.
41 Levons nos cœurs et nos mains au [Dieu] Fort qui est aux cieux, [en disant]:
Tiyeni tikweze mitima yathu ndi manja athu kwa Mulungu kumwamba ndipo tinene kuti:
42 Nous avons péché, nous avons été rebelles, tu n’as point pardonné.
“Ife tachimwa ndi kuwukira ndipo inu simunakhululuke.
43 [Samech.] Tu nous as couverts de [ta] colère, et nous as poursuivis, tu as tué, tu n’as point épargné.
“Mwadzikuta ndi mkwiyo ndi kutilondola ndipo mwatitha mopanda chifundo.
44 Tu t’es couvert d’une nuée, afin que la requête ne passât point.
Mwadzikuta mu mtambo kotero mapemphero athu sakukufikani.
45 Tu nous as fait être la raclure et le rebut au milieu des peuples.
Mwatisandutsa zinyatsi ndi zinyalala pakati pa mitundu ya anthu.
46 [Pe.] Tous nos ennemis ont ouvert leur bouche sur nous.
“Adani anthu atitsekulira pakamwa.
47 La frayeur et la fosse, le dégât et la calamité nous sont arrivés.
Ife tadzazidwa ndi mantha pakuti tagwa mʼdzenje, tapasuka ndi kuwonongedwa.”
48 Mon œil s’est fondu en ruisseaux d’eaux à cause de la plaie de la fille de mon peuple.
Misozi mʼmaso mwanga ikungoti mbwembwembwe chifukwa anthu anga akuwonongedwa.
49 [Hajin.] Mon œil verse des larmes, et ne cesse point, parce qu’il n’y a aucun relâche.
Misozi idzatsika kosalekeza, ndipo sidzasiya,
50 Jusques à ce que l’Eternel regarde et voie des cieux.
mpaka Yehova ayangʼane pansi kuchokera kumwamba ndi kuona.
51 Mon œil afflige mon âme à cause de toutes les filles de ma ville.
Mtima wanga ukupweteka poona zimenezi chifukwa cha akazi onse a mu mzinda.
52 [Tsadi.] Ceux qui me sont ennemis sans cause m’ont poursuivi à outrance, comme on chasse après l’oiseau.
Akundisaka ngati mbalame, amene anali adani anga, popanda chifukwa.
53 Ils ont enserré ma vie dans une fosse, et ont roulé une pierre sur moi.
Ayesa kundipha pondiponya mʼdzenje ndi kundiponya miyala;
54 Les eaux ont regorgé par-dessus ma tête; je disais: je suis retranché.
madzi anamiza mutu wanga ndipo ndinkaganiza kuti imfa yayandikira.
55 [Koph.] J’ai invoqué ton Nom, ô Eternel! d’une des plus basses fosses.
Ndinayitana dzina lanu Inu Yehova, kuchokera mʼdzenje lozama.
56 Tu as ouï ma voix, ne ferme point ton oreille, afin que je n’expire point à force de crier.
Inu munamva kudandaula kwanga. “Mundimvere kulira kwanga kopempha thandizo.”
57 Tu t’es approché au jour que je t’ai invoqué, et tu as dit: ne crains rien.
Munafika pafupi pamene ndinakuyitanani, ndipo munati, “Usaope.”
58 [Resch.] Ô Seigneur! tu as plaidé la cause de mon âme; et tu as garanti ma vie.
Inu Ambuye munandiwombola ku mlandu wanga; munapulumutsa moyo wanga.
59 Tu as vu, ô Eternel! le tort qu’on me fait, fais-moi droit.
Yehova, mwaona zoyipa zimene andichitira. Mundiweruzire ndinu!
60 Tu as vu toutes les vengeances dont ils ont usé, et toutes leurs machinations contre moi.
Mwaona kuzama kwa kubwezera kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine.
61 [Scin.] Tu as ouï, ô Eternel! leur opprobe et toutes leurs machinations contre moi.
Inu Yehova mwamva kunyoza kwawo, chiwembu chawo chonse pa ine,
62 Les discours de ceux qui s’élèvent contre moi, et leur dessein qu’ils ont contre moi tout le long du jour.
manongʼonongʼo a adani anga ondiwukira ine tsiku lonse.
63 Considère quand ils s’asseyent, et quand ils se lèvent, [car] je suis leur chanson.
Tawaonani! Kaya ali pansi kapena kuyimirira, akundinyoza mu nyimbo zawo.
64 [Thau.] Rends-leur la pareille, ô Eternel! selon l’ouvrage de leurs mains.
Inu Yehova, muwabwezere chowayenera, chifukwa cha zimene manja awo achita.
65 Donne-leur un tel ennui qu’il leur couvre le cœur; donne-leur ta malédiction.
Phimbani mitima yawo, ndipo matemberero anu akhale pa iwo!
66 Poursuis-les en ta colère, et les efface de dessous les cieux de l’Eternel.
Muwalondole mwaukali ndipo muwawonongeretu pa dziko lapansi.