< Juges 10 >

1 Après Abimélec, Tolah fils de Puah, fils de Dodo, homme d'Issacar, fut suscité pour délivrer Israël, et il habitait à Samir en la montagne d'Ephraïm.
Atafa Abimeleki panabwera Tola mwana wa Puwa, mdzukulu wa Dodo kudzapulumutsa Aisraeli. Iyeyu anali wa fuko la Isakara ndipo ankakhala ku Samiri mʼdziko la mapiri la Efereimu.
2 Et il jugea Israël vingt-trois ans, puis il mourut, et fut enseveli à Samir.
Iye anatsogolera Aisraeli kwa zaka 23, ndipo anamwalira ndi kuyikidwa ku Samiri.
3 Après lui fut suscité Jaïr Galaadite, qui jugea Israël vingt-deux ans.
Atafa Tola panabwera Yairi wa ku Giliyadi, amene anatsogolera Israeli kwa zaka 22.
4 Et il eut trente fils, qui montaient sur trente ânons, et qui avaient trente villes, qu'on appelle les villes de Jaïr jusqu'à ce jour, lesquelles sont au pays de Galaad.
Iyeyu anali ndi ana aamuna makumi atatu, amene ankakwera pa abulu makumi atatu. Iwo anali ndi mizinda makumi atatu mʼdziko la Giliyadi, imene mpaka lero ikutchedwa kuti Havoti Yairi.
5 Et Jaïr mourut, et fut enseveli à Kamon.
Atamwalira Yairi anayikidwa mʼmanda ku Kamoni.
6 Puis les enfants d'Israël recommencèrent à faire ce qui déplaît à l'Eternel, et servirent les Bahalins, et Hastaroth, savoir, les dieux de Syrie, les dieux de Sidon, les dieux de Moab, les dieux des enfants de Hammon, et les dieux des Philistins; et ils abandonnèrent l'Eternel, et ne le servaient plus.
Aisraeli anachitanso zoyipira Yehova. Iwo anatumikira Abaala ndi Asitoreti, milungu ya ku Aramu, Sidoni, Mowabu, Aamoni ndi Afilisti. Choncho analeka osatumikiranso Yehova.
7 Alors la colère de l'Eternel s'enflamma contre Israël, et il les vendit en la main des Philistins, et en la main des enfants de Hammon;
Tsono Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa Afilisti ndi Aamoni.
8 Qui opprimèrent et foulèrent les enfants d'Israël cette année-là, qui était la dix-huitième; [savoir] tous les enfants d'Israël, qui étaient au-delà du Jourdain au pays des Amorrhéens, qui est en Galaad.
Iwowa anawagonjetseratu Aisraeli mʼchaka chimenechi, ndipo kwa zaka 18 anakhala akusautsa Aisraeli onse amene anali pa tsidya la Yorodani, mʼdziko la Aamori ku Giliyadi.
9 Même les enfants de Hammon passèrent le Jourdain pour combattre aussi contre Juda, et contre Benjamin, et contre la maison d'Ephraïm; et Israël fut fort serré.
Aamori anawoloka mtsinje wa Yorodani kukathira nkhondo mafuko a Yuda, Benjamini ndi Efereimu kotero kuti Israeli anavutika kwambiri.
10 Alors les enfants d'Israël crièrent à l'Eternel, en disant: Nous avons péché contre toi, et certes nous avons abandonné notre Dieu, et nous avons servi les Bahalins.
Kenaka Aisraeli analira kwa Yehova kuti, “Ife takuchimwirani popeza tasiya Inu Mulungu wathu ndi kutumikira Abaala.”
11 Mais l'Eternel répondit aux enfants d'Israël: N'avez-vous pas été opprimés par les Egyptiens, les Amorrhéens, les enfants de Hammon, les Philistins,
Yehova anawafunsa kuti, “Suja ine ndinakupulumutsani kwa Aigupto, Aamori, Aamoni ndi Afilisti?
12 Les Sidoniens, les Hamalécites, et les Mahonites? cependant quand vous avez crié vers moi, je vous ai délivrés de leurs mains.
Ndiponso pamene Asidoni, Aamaleki ndi Amoni anakuzunzani, inu nʼkulirira kwa ine suja ndinakupulumutsani kwa anthu amenewa?
13 Mais vous m'avez abandonné, et vous avez servi d'autres dieux; c'est pourquoi je ne vous délivrerai plus.
Komabe inu mwandikana ndipo mukutumikira milungu ina. Choncho sindidzakupulumutsaninso.
14 Allez, et criez aux dieux que vous avez choisis; qu'ils vous délivrent au temps de votre détresse.
Pitani kalireni kwa milungu imene mwayisankha. Iyoyo ikupulumutseni ku mavuto anuwo.”
15 Mais les enfants d'Israël répondirent à l'Eternel: Nous avons péché, fais-nous, comme il te semblera bon; nous te prions seulement que tu nous délivres aujourd'hui.
Koma Aisraeli anayankha Yehova kuti, “Ife tachimwa. Tichitireni chimene mukuona kuti ndi chabwino, koma chonde tipulumutseni lero lokha.”
16 Alors ils ôtèrent du milieu d'eux les dieux des étrangers, et servirent l'Eternel, qui fut touché en son cœur de l'affliction d'Israël.
Ndipo anachotsa milungu ya chilendo pakati pawo ndi kuyamba kutumikira Yehova. Ndipo Yehova anamva chisoni poona mmene Aisraeli ankazunzikira.
17 Or les enfants de Hammon s'assemblèrent, et se campèrent en Galaad; et les enfants d'Israël aussi s'assemblèrent, et se campèrent à Mitspa.
Tsono Aamoni anasonkhana ndi kumanga zithando za nkhondo ku Giliyadi. Nawonso Aisraeli anasonkhana ndi kumanga zithando zawo za nkhondo ku Mizipa.
18 Et le peuple, [et] les principaux de Galaad dirent l'un à l'autre: Qui sera l'homme qui commencera à combattre contre les enfants de Hammon? il sera pour chef à tous les habitants de Galaad.
Kenaka anthuwo ndi atsogoleri a Agiliyadi anayamba kufunsana kuti, “Kodi ndi munthu wotani amene atayambe kuthira nkhondo Aamoni? Iyeyu adzakhala mtsogoleri wolamulira anthu onse a ku Giliyadi.”

< Juges 10 >