< Josué 3 >
1 Or Josué se leva de bon matin; ils partirent de Sittim, ils vinrent jusqu'au Jourdain, lui et tous les enfants d'Israël, et ils logèrent là cette nuit, avant qu'ils passassent.
Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo.
2 Et au bout de trois jours les officiers passèrent par le camp;
Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse,
3 Et ils commandèrent au peuple en disant: Sitôt que vous verrez l'Arche de l'alliance de l'Eternel votre Dieu, et les Sacrificateurs de la race de Lévi qui la porteront, vous partirez de votre quartier, et vous marcherez après elle.
kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira.
4 Et afin que vous n'approchiez point d'elle, il y aura entre vous et elle une distance de la mesure d'environ deux mille coudées, afin que vous connaissiez le chemin par lequel vous devez marcher; car vous n'avez point ci-devant passé par ce chemin.
Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”
5 Josué dit aussi au peuple: Sanctifiez-vous; car l'Eternel fera demain, au milieu de vous des choses merveilleuses.
Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”
6 Josué parla aussi aux Sacrificateurs, en disant: Chargez [sur vous] l'Arche de l'alliance, et passez devant le peuple. Ainsi ils chargèrent [sur eux] l'Arche de l'alliance, et marchèrent devant le peuple.
Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.
7 Or l'Eternel avait dit à Josué: Aujourd'hui je commencerai de t'élever à la vue de tout Israël; afin qu'ils connaissent que comme j'ai été avec Moïse, je serai [aussi] avec toi.
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose.
8 Tu commanderas donc aux Sacrificateurs qui portent l'Arche de l'alliance, en [leur] disant: Sitôt que vous arriverez au bord de l'eau du Jourdain, vous vous arrêterez au Jourdain.
Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’”
9 Et Josué dit aux enfants d'Israël: Approchez-vous d'ici, et écoutez les paroles de l'Eternel votre Dieu.
Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu.
10 Puis Josué dit: Vous reconnaîtrez à ceci que le [Dieu] Fort, [et] vivant, est au milieu de vous, et qu'il chassera certainement de devant vous les Cananéens, les Héthiens, les Héviens, les Phérésiens, les Guirgasiens, les Amorrhéens, et les Jébusiens.
Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi.
11 Voici, l'Arche de l'alliance du Dominateur de toute la terre s'en va passer devant vous au travers du Jourdain.
Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu.
12 Maintenant donc choisissez douze hommes des Tribus d'Israël, un homme de chaque Tribu.
Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli.
13 Et il arrivera qu'aussitôt que les plantes des pieds des Sacrificateurs qui portent l'Arche de l'Eternel, le Dominateur de toute la terre, seront posées dans les eaux du Jourdain, les eaux du Jourdain seront coupées, les eaux, [dis-je], qui descendent d'en haut, et elles s'arrêteront en un monceau.
Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”
14 Et il arriva que le peuple étant parti de ses tentes pour passer le Jourdain, les Sacrificateurs qui portaient l'Arche de l'alliance, étaient devant le peuple.
Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo.
15 Et sitôt que ceux qui portaient l'Arche furent arrivés au Jourdain, et que les pieds des Sacrificateurs qui portaient l'Arche furent mouillés au bord de l'eau, (or le Jourdain regorge par dessus tous ses bords durant tout le temps de la moisson.)
Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo,
16 Les eaux qui descendaient d'en-haut, s'arrêtèrent, et s'élevèrent en un monceau fort loin, depuis la ville d'Adam, qui [est] à côté de Tsartan; et celles [d'embas], qui descendaient vers la mer de la campagne, qui est la mer salée, défaillirent et s'écoulèrent, et le peuple passa vis-à-vis de Jérico.
madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko.
17 Mais les Sacrificateurs qui portaient l'Arche de l'alliance de l'Eternel, s'arrêtèrent [de pied] ferme sur le sec au milieu du Jourdain, pendant que tout Israël passa à sec, jusqu'à ce que tout le peuple eût achevé de passer le Jourdain.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.