< Josué 23 >

1 Or il arriva plusieurs jours après, que l'Eternel ayant donné du repos à Israël de tous leurs ennemis à l'environ, Josué était vieux, fort avancé en âge.
Panapita nthawi yayitali kuchokera pamene Yehova anakhazikitsa mtendere pakati pa Aisraeli ndi adani awo owazungulira. Nthawi imeneyi nʼkuti Yoswa atakalamba, ali ndi zaka zambiri.
2 Et Josué appela tout Israël, ses Anciens, et ses chefs, et ses juges, et ses officiers, et leur dit: Je suis devenu vieux, fort avancé en âge.
Yoswayo anayitanitsa Aisraeli onse pamodzi ndi akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi oyangʼanira anthu antchito ndipo anawawuza kuti, “Ine ndakalamba ndipo ndili ndi zaka zambiri.
3 Vous avez vu aussi tout ce que l'Eternel votre Dieu a fait à toutes ces nations, à cause de vous; car l'Eternel votre Dieu est celui qui combat pour vous.
Inu mwaona zonse zimene Yehova Mulungu wanu wachita kwa mitundu yonseyi chifukwa cha inu. Ndi Yehova Mulungu wanu amene anakumenyerani nkhondo.
4 Voyez, je vous ai partagé par sort en héritage selon vos Tribus, [le pays de] ces nations qui sont restées, depuis le Jourdain, et [le pays de] toutes les nations que j'ai exterminées, jusqu'à la grande mer, vers le soleil couchant.
Tsono onani! Mitundu ya anthu otsalawa ndayipereka kwa mafuko anu pamodzi ndi mitundu ya anthu ya pakati pa Yorodani ndi Nyanja Yayikulu ya kumadzulo imene ndinayigonjetsa.
5 Et l'Eternel votre Dieu les chassera de devant vous, et les dépossédera; et vous posséderez leur pays en héritage, comme l'Eternel votre Dieu vous [en] a parlé.
Yehova Mulungu wanu ndiye adzawathamangitsa pamaso panu. Mudzatenga dziko lawo monga Yehova anakulonjezerani.
6 Fortifiez-vous donc de plus en plus, pour garder et faire tout ce qui est écrit au livre de la Loi de Moïse; afin que vous ne vous en détourniez ni à droite ni à gauche;
“Choncho khalani amphamvu, ndipo samalani kuti mumvere zonse zimene zalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose. Musapatuke pa malamulo onse amene alembedwamo.
7 Et que vous ne vous mêliez point avec ces nations qui sont restées parmi vous; que vous ne fassiez point mention du nom de leurs dieux; et que vous ne fassiez jurer personne [par eux], et que vous ne les serviez point, et ne vous prosterniez point devant eux.
Musagwirizane ndi mitundu ya anthu imene yatsala pakati panu. Musatchule mayina a milungu yawo kapena kuyitchula polumbira. Musayitumikire kapena kuyigwadira.
8 Mais attachez-vous à l'Eternel votre Dieu, comme vous avez fait jusqu'à ce jour.
Koma mukuyenera kugwiritsa Yehova Mulungu wanu, monga mwachitira mpaka lero lino.
9 C'est pour cela que l'Eternel a dépossédé de devant vous des nations grandes et fortes; et quant à vous, nul n'a subsisté devant vous jusqu'à ce jour.
“Yehova wapirikitsa patsogolo panu mitundu ya anthu ikuluikulu ndi yolimba. Mpaka lero palibe amene watha kulimbana nanu.
10 Un seul homme d'entre vous en poursuivra mille; car l'Eternel votre Dieu est celui qui combat pour vous, comme il vous en a parlé.
Aliyense wa inu atha kuthamangitsa anthu 1,000 chifukwa Yehova Mulungu wanu ndiye amakumenyerani nkhondo, monga momwe analonjezera.
11 Prenez donc garde soigneusement sur vos âmes, que vous aimiez l'Eternel votre Dieu.
Choncho samalitsani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu.
12 Autrement si vous vous en détournez en aucune manière et que vous vous attachiez au reste de ces nations, [savoir] à ceux qui sont demeurés de reste avec vous, et que vous fassiez alliance avec eux, et que vous vous mêliez avec eux, et eux avec vous;
“Koma ngati mubwerera mʼmbuyo ndi kuphatikizana ndi mitundu yotsalayi imene ili pakati panu ndi kumakwatirana nayo,
13 Sachez certainement que l'Eternel votre Dieu ne continuera plus à déposséder ces nations devant vous; mais elles vous seront en pièges, et en filet, et comme un fléau à vos côtés, et comme des épines à vos yeux, jusqu'à ce que vous périssiez de dessus cette bonne terre que l'Eternel votre Dieu vous a donnée.
pamenepo mudziwe kuti Yehova, Mulungu wanu, sadzapirikitsa mitundu imeneyi pamaso panu, koma idzakhala ngati msampha kwa inu kapenanso khwekhwe lokukolani. Idzakhala ngati zikwapu pa msana panu kapenanso ngati minga mʼmaso mwanu mpaka mutatha psiti mʼdziko labwinoli limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.
14 Or voici, je m'en vais aujourd'hui par le chemin de toute la terre; et vous connaîtrez dans tout votre cœur, et dans toute votre âme qu'il n'est point tombé un seul mot de toutes les bonnes paroles que l'Eternel votre Dieu a dites de vous; tout vous est arrivé, il n'en est pas tombé un seul mot.
“Aliyense wa inu akudziwa mu mtima mwake komanso mʼmoyo mwake kuti zabwino zonse zimene Yehova Mulungu wanu anakulonjezani zachitika. Palibe lonjezo ndi limodzi lomwe limene silinakwaniritsidwe.
15 Et il arrivera que comme toutes les bonnes paroles que l'Eternel votre Dieu vous avait dites vous sont arrivées; ainsi l'Eternel fera venir sur vous toutes les mauvaises paroles, jusqu'à ce qu'il vous ait exterminés de dessus cette bonne terre que l'Eternel votre Dieu vous a donnée.
Monga momwe Yehova Mulungu wanu wakuchitirani zabwino zonse zimene ananena kuti adzachita, Yehovayo angathenso kukuchitirani zoyipa zonse zimene waopseza, mpaka kukuchotsani mʼdziko lokoma limene anakupatsani.
16 Quand vous aurez transgressé l'alliance de l'Eternel votre Dieu, qu'il vous a commandée, et que vous serez allés servir d'autres dieux, et vous serez prosternés devant eux, la colère de l'Eternel s'enflammera contre vous, et vous périrez incontinent de dessus cette bonne terre qu'il vous a donnée.
Ngati muphwanya pangano la Yehova Mulungu wanu, limene anakulamulirani nʼkumapita kukatumikira milungu ina ndi kuyigwadira, Yehova adzakukwiyirani, ndiye mudzachotsedwa mʼdziko labwinoli limene Yehova wakupatsani.”

< Josué 23 >