< Josué 13 >
1 Or quand Josué fut devenu vieux, fort avancé en âge, l'Eternel lui dit: Tu es devenu vieux, fort avancé en âge, et il reste encore un fort grand pays à posséder.
Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.
2 C'est ici le pays qui demeure de reste, toutes les contrées des Philistins, et tout Guésuri.
“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri
3 Depuis Sihor, qui est au devant de l'Egypte, même jusqu'aux frontières de Hekron vers le Septentrion; cela est réputé des Cananéens; [savoir] les cinq gouvernements des Philistins, qui sont celui de Gaza, celui d'Asdod, celui d'Askélon, celui de Gath, et celui de Hekron, et les Hauviens.
kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto.
4 Du côté du Midi tout le pays des Cananéens, et Méhara qui est aux Sidoniens, jusques vers Aphek, jusqu'aux frontières des Amorrhéens.
Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori.
5 Le pays aussi qui appartient aux Guibliens, et tout le Liban; vers le soleil levant, depuis Bahal-Gad, sous la montagne de Hermon, jusqu'à l'entrée de Hamath.
Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
6 Tous les habitants de la montagne depuis le Liban jusqu'aux eaux de Masréphoth; tous les Sidoniens; je les chasserai moi-même de devant les enfants d'Israël; fais seulement qu'on en jette [les lots], afin qu'elle soit à Israël en héritage, comme je te l'ai commandé.
“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira.
7 Maintenant donc divise ce pays en héritage aux neuf Tribus, et à la moitié de la Tribu de Manassé;
Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”
8 Avec laquelle les Rubénites et les Gadites ont pris leur héritage; lequel Moïse leur a donné au delà du Jourdain vers l'Orient, selon que Moïse serviteur de l'Eternel le leur a donné;
Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.
9 Depuis Haroher, qui est sur le bord du torrent d'Arnon, et la ville qui [est] au milieu du torrent, et tout le plat pays de Médéba, jusqu'à Dibon.
Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni.
10 Et toutes les villes de Sihon, Roi des Amorrhéens, qui régnait à Hesbon, jusqu'aux limites des enfants de Hammon;
Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni.
11 Et Galaad, et les limites des Guésuriens et des Mahacathiens, et toute la montagne de Hermon, et tout Basan jusqu'à Salca;
Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka.
12 Tout le Royaume de Hog en Basan, lequel Hog régnait à Hastaroth, et à Edréhi, [et] était demeuré de reste des Réphaïms, lesquels [Rois] Moïse défit, et les déposséda.
Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali.
13 (Or les enfants d'Israël ne dépossédèrent point les Guésuriens et les Mahacathiens; mais les Guésuriens et les Mahacathiens ont habité parmi Israël jusqu'à ce jour.)
Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.
14 Seulement il ne donna point d'héritage à la Tribu de Lévi; les sacrifices de l'Eternel, le Dieu d'Israël, faits par feu étant son héritage, comme il lui [en] avait parlé.
Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.
15 Moïse donc donna un héritage à la Tribu des enfants de Ruben selon leurs familles.
Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.
16 Et leurs bornes furent depuis Haroher qui est sur le bord du torrent d'Arnon, et la ville qui est au milieu du torrent, et tout le plat pays qui est près de Médéba.
Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba.
17 Hesbon et toutes ses villes, qui étaient au plat pays; Dibon, et Bamoth-Bahal, et Beth-Bahal-mehon.
Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni,
18 Et Jahatsa, et Kédémoth, et Méphahath.
Yahaza, Kedemoti, Mefaati.
19 Et Kirjathajim, et Sibma, et Tseretsahar en la montagne de la vallée.
Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa,
20 Et Beth-Péhor, et Asdoth de Pisga, et Beth-jesimoth.
Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti.
21 Et toutes les villes du plat pays, et tout le Royaume de Sihon, Roi des Amorrhéens qui régnait à Hesbon; lequel Moïse défit, avec les principaux de Madian, Evi, Rekem, Tsur, Hur, et Rébah, Princes relevant de Sihon, [et] habitant au pays.
Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni.
22 Les enfants d'Israël firent passer aussi par l'épée Balaam fils de Béhor, le devin, avec les autres qui y furent tués.
Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga.
23 Et les bornes des enfants de Ruben furent le Jourdain, et sa borne. Tel fut l'héritage des enfants de Ruben selon leurs familles, [savoir] ces villes-là, et leurs villages.
Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.
24 Moïse donna aussi [un héritage] à la Tribu de Gad pour les enfants de Gad, selon leurs familles.
Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:
25 Et leur pays fut Jahzer, et toutes les villes de Galaad, et la moitié du pays des enfants de Hammon, jusqu'à Haroher, qui est vis-à-vis de Rabba.
Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba;
26 Et depuis Hesbon jusqu'à Ramath-mitspé, et Bétonim, et depuis Mahanajim jusqu'aux frontières de Débir.
ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri.
27 Et dans la vallée, Beth-haram, et Beth-nimra, et Succoth, et Tsaphon; le reste du Royaume de Sihon Roi de Hesbon, le Jourdain, et sa borne, jusqu'au bout de la mer de Kinnereth, au delà du Jourdain, vers l'Orient.
Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto.
28 Tel fut l'héritage des enfants de Gad, selon leurs familles; [savoir] ces villes-là et leurs villages.
Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.
29 Moïse aussi donna à la moitié de la Tribu de Manassé [un héritage], qui est demeuré à la moitié de la Tribu des enfants de Manassé, selon leurs familles.
Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.
30 Leur pays fut depuis Mahanajim, tout Basan, [et] tout le Royaume de Hog, Roi de Basan, et tous les bourgs de Jaïr qui sont en Basan, soixante villes.
Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko.
31 Et la moitié de Galaad, et Hastaroth, et Edréhi, villes du Royaume de Hog en Basan, furent aux enfants de Makir, fils de Manassé, [savoir] à la moitié des enfants de Makir, selon leurs familles.
Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.
32 Ce sont là [les pays] que Moïse [étant] dans les campagnes de Moab avait partagés en héritage, de ce qui était au delà du Jourdain de Jérico, vers l'Orient.
Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani.
33 Or Moïse ne donna point d'héritage à la Tribu de Lévi; [car] l'Eternel le Dieu d'Israël est leur héritage, comme il leur en a parlé.
Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.