< Josué 10 >

1 Or quand Adoni-tsédek, Roi de Jérusalem, eut entendu que Josué avait pris Haï, et qu'il l'avait entièrement détruite à la façon de l'interdit, ayant fait à Haï et à son Roi, comme il avait fait à Jérico et à son Roi, et que les habitants de Gabaon avaient fait la paix avec les Israélites, et étaient parmi eux;
Adoni-Zedeki mfumu ya ku Yerusalemu inamva kuti Yoswa wagonjetsa ndi kuwononga kotheratu mzinda wa Ai pamodzi ndi mfumu yake, monga anachitira ndi Yeriko ndi mfumu yake. Inamvanso kuti anthu a ku Gibiyoni anachita pangano la mtendere ndi Israeli ndipo amakhala pakati pawo.
2 On craignit beaucoup, parce que Gabaon était une grande ville, comme une ville Royale, et elle était plus grande que Haï; et [parce que] tous ses hommes étaient forts.
Choncho iye ndi anthu ake anachita mantha aakulu, chifukwa Gibiyoni unali mzinda waukulu kwambiri, monga mzinda uliwonse wokhala ndi mfumu. Unali waukulu ndipo ankhondo ake anali olimba mtima.
3 C'est pourquoi Adoni-tsédek, Roi de Jérusalem, envoya vers Horam Roi de Hébron, et vers Biréam, Roi de Jarmuth, et vers Japhiah, Roi de Lakis, et vers Débir, Roi de Héglon, pour leur dire:
Chotsatira chake Adoni-Zedeki mfumu ya Yerusalemu inatuma uthenga kwa Hohamu mfumu ya Hebroni, Piramu mfumu ya Yarimuti, Yafiya mfumu ya Lakisi ndi Debri mfumu ya Egiloni.
4 Montez vers moi, et donnez-moi du secours afin que nous frappions Gabaon; car elle a fait la paix avec Josué, et avec les enfants d'Israël.
Iye anatumiza mawu kuti, “Bwerani mudzandithandize kumenyana ndi Gibiyoni, chifukwa anthu ake achita pangano la mtendere ndi Yoswa ndi Aisraeli.”
5 Ainsi cinq Rois des Amorrhéens, [savoir], le Roi de Jérusalem, le Roi de Hébron, le Roi de Jarmuth, le Roi de Lakis, et le Roi de Héglon, s'assemblèrent et montèrent eux et toutes leurs armées, et se campèrent contre Gabaon, et lui firent la guerre.
Mafumu asanu a Aamori aja, mfumu ya Yerusalemu, mfumu ya Hebroni, mfumu ya Yarimuti, mfumu ya Lakisi ndi mfumu ya Egiloni, anagwirizana. Iwo anasonkhanitsa ankhondo awo nazungulira mzinda wa Gibiyoni ndi kuwuthira nkhondo.
6 C'est pourquoi ceux de Gabaon envoyèrent à Josué au camp à Guilgal, en disant: Ne retire point tes mains de tes serviteurs; monte promptement vers nous, et nous garantis, et donne-nous du secours; car tous les Rois des Amorrhéens qui habitent aux montagnes, se sont assemblés contre nous.
Koma anthu a ku Gibiyoni anatumiza uthenga kwa Yoswa ku misasa ya ku Giligala nati, “Musawataye anthu anu! Bwerani msanga mudzatipulumutse! Dzatithandizeni chifukwa mafumu a Aamori ochokera ku dziko la ku mapiri agwirizana kuti adzatithire nkhondo.”
7 Josué donc monta de Guilgal, et avec lui tout le peuple [qui était] propre à la guerre, et tous les hommes forts et vaillants.
Choncho Yoswa ananyamuka kuchoka ku Giligala ndi gulu lake la ankhondo pamodzi ndi anthu ake olimba mtima.
8 Et l'Eternel dit à Josué: Ne les crains point; car je les ai livrés entre tes mains, et aucun d'eux ne subsistera devant toi.
Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope, Ine ndawapereka mʼdzanja lako. Palibe ndi mmodzi mwa amenewa amene adzalimbe.”
9 Josué donc vint promptement à eux; [et] monta de Guilgal toute la nuit.
Atayenda usiku wonse kuchokera ku Giligala, Yoswa anawathira nkhondo mwadzidzidzi.
10 Et l'Eternel les mit en déroute devant Israël, qui en fit un grand carnage près de Gabaon; et les poursuivit par le chemin de la montagne de Beth-horon, et les battit jusqu'à Hazéka, et jusqu'à Makkéda.
Yehova anachititsa mantha adani aja atangoona gulu lankhondo la Israeli. Choncho Aisraeli anagonjetsa Aamori ku Gibiyoni ndipo anawathamangitsa mu msewu wopita ku Beti-Horoni ndi kuwapha njira yonse yopita ku Azeka ndi Makeda.
11 Et comme ils s'enfuyaient de devant Israël, et qu'ils étaient à la descente de Beth-horon, l'Eternel jeta des cieux sur eux de grosses pierres jusqu'à Hazéka, dont ils moururent; et il y en eut encore plus de ceux qui moururent des pierres de grêle, que de ceux que les enfants d'Israël tuèrent avec l'épée.
Pamene ankathawa pamaso pa Israeli pa njira yochokera ku Beti-Horoni mpaka ku Azeka, Yehova anawagwetsera matalala akuluakulu kuchokera kumwamba ndipo ambiri mwa iwo anafa ndi matalala kuposa amene anaphedwa ndi lupanga la Israeli.
12 Alors Josué parla à l'Eternel, le jour que l'Eternel livra l'Amorrhéen aux enfants d'Israël, et dit en la présence d'Israël: Soleil, arrête-toi sur Gabaon, et toi Lune, sur la vallée d'Ajalon.
Pa tsiku limene Yehova anapereka Aamori mʼmanja mwa Israeli, Yoswa ananena kwa Yehova pamaso pa Israeli kuti, “Iwe dzuwa, ima pamwamba pa Gibiyoni, mwezi ima pamwamba pa chigwa cha Ayaloni.”
13 Et le soleil s'arrêta, et la lune aussi s'arrêta, jusqu'à ce que le peuple se fût vengé de ses ennemis. Ceci n'est-il pas écrit au Livre du Droiturier? Le soleil donc s'arrêta au milieu des cieux et ne se hâta point de se coucher environ un jour entier.
Choncho dzuwa linayima, mwezinso unayima, mpaka dziko la Israeli litagonjetsa adani ake. Zimenezi zalembedwa mʼbuku la Yasari. Dzuwa linayima pamodzimodzi pakati pa thambo mlengalenga, osayendanso kwa tsiku lathunthu.
14 Et il n'y a point eu de jour semblable à celui-là, devant ni après, l'Eternel exauçant la voix d'un homme; car l'Eternel combattait pour les Israélites.
Sipanakhaleponso tsiku ngati limeneli kuyambira kale, tsiku limene Yehova anamvera munthu. Izi zinatero chifukwa Yehova ankamenyera nkhondo Aisraeli.
15 Et Josué et tout Israël avec lui, s'en retourna au camp à Guilgal.
Kenaka Yoswa anabwerera pamodzi ndi Aisraeli onse ku misasa ku Giligala.
16 Au reste ces cinq Rois-là s'étaient enfuis, et s'étaient cachés dans une caverne à Makkéda.
Mafumu asanu aja anathawa ndi kukabisala ku phanga la Makeda.
17 Et on avait rapporté à Josué, en disant: On a trouvé les cinq Rois cachés dans une caverne à Makkéda.
Koma Yoswa anamva kuti mafumu asanu awapeza akubisala ku phanga la Makeda.
18 Et Josué avait dit: Roulez de grandes pierres à l'entrée de la caverne, mettez près d'elle quelques hommes pour les garder.
Tsono Yoswa analamula kuti, “Mugubuduzire miyala ikuluikulu pa khomo la phangalo, ndipo muyike anthu ena kuti azilondera.
19 Mais vous, ne vous arrêtez point, poursuivez vos ennemis, et les défaites jusqu'au dernier, [et] ne les laissez point entrer dans leurs villes; car l'Eternel votre Dieu les a livrés en vos mains.
Koma inu musakhaleko! Thamangitsani adani anu, muwathire nkhondo kuchokera kumbuyo ndipo musawalole kuti akafike ku mizinda yawo, pakuti Yehova Mulungu wanu wawapereka mʼmanja mwanu.”
20 Et quand Josué avec les enfants d'Israël eut achevé d'en faire une très grande boucherie, jusqu'à les détruire entièrement, et que ceux d'entr'eux qui étaient échappés se furent retirés dans les villes fermées de murailles;
Kotero Yoswa ndi Aisraeli anapha anthu aja, kupatulapo ochepa amene anathawa nakabisala ku mizinda yawo.
21 Tout le peuple retourna en paix au camp vers Josué à Makkéda; [et] personne ne remua sa langue contre aucun des enfants d'Israël.
Kenaka gulu lonse la ankhondo linabwerera bwinobwino kwa Yoswa ku misasa ya ku Makeda, palibe aliyense mu mzindamo amene anaputanso Aisraeli.
22 Alors Josué dit: Ouvrez l'entrée de la caverne, et amenez-moi ces cinq Rois hors de la caverne.
Yoswa anati, “Tsekulani khomo la phangalo ndipo muwabweretse kwa ine mafumu asanuwo.”
23 Et ils le firent ainsi, et ils amenèrent hors de la caverne ces cinq Rois: le Roi de Jérusalem, le Roi de Hébron, le Roi de Jarmuth, le Roi de Lakis et le Roi de Héglon.
Pamenepo mafumu asanu aja anatulutsidwa, mfumu ya ku Yerusalemu, mfumu ya ku Hebroni, mfumu ya ku Yarimuti, mfumu ya ku Lakisi, ndi mfumu ya ku Egiloni.
24 Et après qu'ils eurent amené à Josué ces cinq Rois hors de la caverne, Josué appela tous les hommes d'Israël, et dit aux Capitaines des gens de guerre qui étaient allés avec lui: Approchez-vous, mettez vos pieds sur le cou de ces Rois; et ils s'approchèrent, et mirent leurs pieds sur leur cou.
Atabwera nawo kwa Yoswa, iye anayitana Aisraeli onse. Ndipo analamula akuluakulu ake amene anapita naye limodzi kuti, “Bwerani kuno ndipo apondeni pakhosi mafumuwa.”
25 Alors Josué leur dit: Ne craignez point, et ne soyez point effrayés, fortifiez-vous, et vous renforcez; car l'Eternel fera ainsi à tous vos ennemis contre lesquels vous combattez.
Yoswa anawawuza kuti, “Musaope kapena kutaya mtima. Khalani amphamvu ndi olimba mtima popeza umo ndi mmene Yehova adzachitire ndi adani anu onse amene mudzamenyana nawo.”
26 Et après cela Josué les frappa, et les fit mourir, et les fit pendre à cinq potences; et ils demeurèrent pendus à ces potences jusqu'au soir.
Kenaka Yoswa anawabaya ndi kuwapha mafumuwo ndipo anawapachika pa mitengo isanu ndipo anakhala pamenepo mpaka madzulo.
27 Et comme le soleil se couchait Josué fit commandement qu'on les ôtât de ces potences, et on les jeta dans la caverne où ils s'étaient cachés; et on mit à l'entrée de la caverne de grandes pierres [qui y sont demeurées] jusqu'à ce jour.
Dzuwa litalowa, Yoswa analamula kuti awachotse pa mitengo ija ndi kuwaponya mʼphanga limene ankabisalamo. Pa khomo pa phangalo anayikapo miyala ikuluikulu imene ilipo mpaka lero.
28 Josué prit aussi en ce même jour Makkéda, et la frappa au tranchant de l'épée, et défit à la façon de l'interdit son Roi et ses [habitants], et ne laissa échapper aucune personne qui fût dans cette ville; et il fit au Roi de Makkéda comme il avait fait au Roi de Jérico.
Tsiku lomwelo Yoswa analanda mzinda wa Makeda. Iye anapha anthu a mu mzindamo ndi mfumu yake ndipo sanasiye aliyense wamoyo. Yoswa anachita ndi mfumu ya ku Makeda monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
29 Après cela Josué et tout Israël avec lui passa de Makkéda à Libna, et fit la guerre à Libna.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Makeda nakafika ku Libina ndi kuthira nkhondo mzindawo.
30 Et l'Eternel la livra aussi entre les mains d'Israël, avec son Roi, et il la frappa au tranchant de l'épée, et ne laissa échapper aucune personne qui fût dans cette ville; et il fit à son Roi comme il avait fait au Roi de Jérico.
Yehova anaperekanso mzindawo ndi mfumu yake mʼmanja mwa Aisraeli. Ndipo Yoswa anapha onse amene anali mu mzindamo. Palibe amene anatsala wamoyo. Ndipo Yoswa anachita ndi mfumu ya Libina monga anachitira ndi mfumu ya Yeriko.
31 Ensuite Josué et tout Israël avec lui passa de Libna à Lakis, et se campa devant elle, et lui fit la guerre.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Libina kupita ku Lakisi. Iye anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
32 Et l'Eternel livra Lakis entre les mains d'Israël, qui la prit le deuxième jour, et la frappa au tranchant de l'épée, et toutes les personnes qui étaient dedans, comme il avait fait à Libna.
Yehova anapereka Lakisi kwa Israeli; ndipo Yoswa anawulanda pa tsiku lachiwiri. Monga anachita ndi mzinda wa Libina, Yoswa anapha anthu onse okhala mu mzinda wa Lakisi, ndipo palibe amene anatsala ndi moyo.
33 Alors Horam Roi de Guézer monta pour secourir Lakis; et Josué le frappa, lui et son peuple, de sorte qu'il n'en laissa pas échapper un seul homme.
Nthawi imeneyi nʼkuti Horamu mfumu ya Gezeri itabwera kudzathandiza Lakisi koma Yoswa anamugonjetsa pamodzi ndi asilikali ake ndipo palibe anatsala wamoyo.
34 Après cela Josué et tout Israël avec lui passa de Lakis à Héglon; et ils se campèrent devant elle, et lui firent la guerre;
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anapitirira kuchokera ku Lakisi nakafika ku Egiloni. Iwo anazungulira mzindawo ndi kuwuthira nkhondo.
35 Et ils la prirent ce jour-là même, et la frappèrent au tranchant de l'épée; et [Josué] défit à la façon de l'interdit en ce même jour-là toutes les personnes qui y étaient, comme il avait fait à Lakis.
Anawulanda tsiku lomwelo ndipo anapha aliyense amene anali mu mzindawo monga momwe anachitira ku Lakisi.
36 Puis Josué et tout Israël avec lui monta d'Héglon à Hébron, et ils lui firent la guerre.
Kenaka Yoswa ndi Aisraeli onse anachoka ku Egiloni nakafika ku Hebroni ndi kukawuthira nkhondo.
37 Et ils la prirent, et la frappèrent au tranchant de l'épée, avec son Roi, et toutes ses villes, et toutes les personnes qui y étaient; il n'en laissa échapper aucune, comme il avait fait à Héglon; et il la défit à la façon de l'interdit, et toutes les personnes qui y étaient.
Iwo analanda mzindawo napha ndi lupanga mfumu yake pamodzi ndi onse amene ankakhala mʼmenemo. Monga anachita ndi mzinda wa Egiloni, kuti sanasiye aliyense ndi moyo, anachitanso chimodzimodzi ndi mzinda wa Hebroni.
38 Ensuite Josué et tout Israël avec lui rebroussa chemin vers Débir, et ils lui firent la guerre.
Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anatembenukira mzinda wa Debri ndi kukawuthira nkhondo.
39 Et il la prit avec son Roi, et toutes ses villes; et ils les frappèrent au tranchant de l'épée, et défirent à la façon de l'interdit toutes les personnes qui y étaient; il n'en laissa échapper aucune. Il fit à Débir et à son Roi comme il avait fait à Hébron, et comme il avait fait à Libna et à son Roi.
Iwo analanda mzindawo ndi midzi ndi kupha mfumu yake pamodzi ndi onse okhala mʼmenemo. Anachita ndi mzinda wa Debri pamodzi ndi mfumu yake zofanana ndi zimene anachita ndi mzinda wa Libina ndi wa Hebroni.
40 Josué donc frappa tout ce pays-là, la montagne, et le Midi, et la plaine, et les pentes des montagnes, et tous leurs Rois; il n'en laissa échapper aucun; et il défit à la façon de l'interdit toutes les personnes vivantes, comme l'Eternel le Dieu d'Israël l'avait commandé.
Motero Yoswa anagonjetsa dziko lonselo. Anapha mafumu onse a dera la kumapiri, dera la kummawa, dera la kumadzulo mʼmphepete mwa phiri, ndiponso dera la ku magomo, kummwera. Iye sanasiye wina aliyense wamoyo. Anapha onse amene anali moyo monga momwe Yehova Mulungu wa Israeli analamulira.
41 [Ainsi] Josué les battit depuis Kadès-barné jusqu'à Gaza, et tout le pays de Gosen, jusqu'à Gabaon.
Yoswa anawagonjetsa iwo kuyambira ku Kadesi Barinea mpaka ku Gaza, ndiponso kuchokera ku chigawo chonse cha Goseni mpaka ku Gibiyoni.
42 Il prit donc tout à la fois ces Rois-là et leur pays; parce que l'Eternel, le Dieu d'Israël, combattait pour Israël.
Yoswa anagonjetsa mafumu onsewa ndi kulanda dziko lawo kamodzinʼkamodzi chifukwa Yehova Mulungu wa Israeli anawamenyera nkhondo.
43 Après quoi Josué et tout Israël avec lui s'en retournèrent au camp à Guilgal.
Pambuyo pake Yoswa ndi Aisraeli onse anabwerera ku misasa yawo ku Giligala.

< Josué 10 >