< Job 39 >

1 Sais-tu le temps auquel les chamois des rochers font leurs petits? As-tu observé quand les biches faonnent?
“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera? Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?
2 Compteras-tu les mois qu'elles achèvent leur portée, et sauras-tu le temps auquel elles feront leurs petits,
Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere? Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?
3 Et qu'elles se courberont pour mettre bas leurs petits, [et] qu'elles se délivreront de leurs douleurs?
Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo; pamenepo ululu wobereka nʼkutha.
4 Leurs fans se portent bien, ils croissent dans les blés; ils s'écartent, et ne retournent plus vers elles.
Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo; kenaka amachoka ndipo sabwereranso.
5 Qui est-ce qui a laissé aller libre l'âne sauvage, et qui a délié les liens de l'âne farouche,
“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera? Ndani amamasula zingwe zake?
6 Auquel j'ai donné la campagne pour maison, la terre inhabitée pour ses retraites?
Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake, nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo
7 Il se rit du bruit de la ville; il n'entend point les clameurs de l'exacteur;
Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda; ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.
8 Les montagnes qu'il va épiant çà et là, sont ses pâturages, et il cherche toute sorte de verdure.
Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.
9 La licorne voudra-t-elle te servir, ou demeurera-t-elle à ta crèche?
“Kodi njati ingavomere kukutumikira? Kodi ingagone mu gome lako usiku?
10 Lieras-tu la licorne avec son licou pour labourer? ou rompra-t-elle les mottes des vallées après toi?
Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima? Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?
11 T'assureras-tu d'elle, sous ombre que sa force est grande, et lui abandonneras-tu ton travail?
Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake? Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?
12 Te fieras-tu qu'elle te porte ta moisson, et qu'elle l'amasse dans ton aire?
Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako ndi kumuyika ku malo opunthira?
13 As-tu donné aux paons ce plumage qui est si brillant, ou à l'autruche les ailes et les plumes?
“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira, koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.
14 Néanmoins elle abandonne ses œufs à terre, et les fait échauffer sur la poussière,
Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi ndipo amafundidwa ndi nthaka,
15 Et elle oublie que le pied les écrasera, ou que les bêtes des champs les fouleront.
nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa, ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.
16 Elle se montre cruelle envers ses petits, comme s'ils n'étaient pas à elle; et son travail est souvent inutile et elle ne s'en soucie point.
Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake; Imayiwala zoti inavutika powabala.
17 Car Dieu l'a privée de sagesse, et ne lui a point donné d'intelligence;
Chifukwa Mulungu anayimana nzeru, simvetsa kanthu kalikonse.
18 A la première occasion elle se dresse en haut, et se moque du cheval et de celui qui le monte.
Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga, imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.
19 As-tu donné la force au cheval? [et] as-tu revêtu son cou d'un [hennissement] éclatant comme le tonnerre?
“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?
20 Feras-tu bondir le cheval comme la sauterelle? le son magnifique de ses narines est effrayant.
Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira, ukali wake nʼkumachititsa mantha?
21 Il creuse la terre [de son pied], il s'égaie en sa force, il va à la rencontre d'un homme armé;
Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake, ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.
22 Il se rit de la frayeur, il ne s'épouvante de rien, et il ne se détourne point de devant l'épée.
Iye sachita mantha, saopa chilichonse; sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.
23 [Il n'a point peur des] flèches qui sifflent tout autour de lui, ni du fer luisant de la hallebarde et du javelot.
Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.
24 Il creuse la terre, plein d'émotion et d'ardeur au son de la trompette, et il ne peut se retenir.
Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha; satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.
25 Au son bruyant de la trompette, il dit: Ha! ha! Il flaire de loin la bataille, le tonnerre des Capitaines, et le cri de triomphe.
Lipenga likalira amati, ‘Twee!’ Amamva fungo la nkhondo ali patali, kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.
26 Est-ce par ta sagesse que l'épervier se remplume, et qu'il étend ses ailes vers le Midi?
“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako, ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?
27 Sera-ce à ton commandement que l'aigle prendra l'essor, et qu'elle élèvera sa nichée en haut?
Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?
28 Elle habite sur les rochers, et elle s'y tient; [même] sur les sommets des rochers et dans des lieux forts.
Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku; chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.
29 De là elle découvre le gibier, ses yeux voient de loin.
Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye; maso ake amachionera patali chinthucho.
30 Ses petits aussi sucent le sang, et où il y a des corps morts, elle y est aussitôt.
Ana ake amayamwa magazi, ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”

< Job 39 >