< Job 25 >

1 Alors Bildad Suhite prit la parole, et dit:
Apo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
2 Le règne et la terreur sont par-devers Dieu; il maintient la paix dans ses hauts lieux.
“Ulamuliro ndi kuopsa ndi za Mulungu, Iye amakhazikitsa bata mu ufumu wake kumwambako.
3 Ses armées se peuvent-elles compter? et sur qui sa lumière ne se lève-t-elle point?
Kodi magulu ake ankhondo nʼkuwerengeka? Kodi kuwala kwake sikuwalira ndani?
4 Et comment l'homme [mortel] se justifierait-il devant le [Dieu] Fort? Et comment celui qui est né de femme serait-il pur?
Kodi munthu angakhale bwanji wolungama pamaso pa Mulungu? Kodi munthu wobadwa mwa mayi angakhale wangwiro?
5 Voilà, [qu'on aille] jusqu'à la lune, et elle ne luira point; les étoiles ne seront point pures devant ses yeux.
Ngati mwezi sutha kuwala kwenikweni, ndipo nyenyezi sizitha kuwala pamaso pake,
6 Combien moins l'homme qui n'est qu'un ver; et le fils d'un homme, qui n'est qu'un vermisseau!
nanji tsono munthu amene ali ngati mphutsi, mwana wa munthu amene ali ngati nyongolotsi!”

< Job 25 >