< Job 15 >

1 Alors Eliphas Témanite prit la parole, et dit:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Un homme sage proférera-t-il dans ses réponses une science aussi légère que le vent, des opinions vaines; et remplira-t-il son ventre du vent d'Orient;
“Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
3 Disputant avec des discours qui ne servent de rien, et avec des paroles dont on ne peut tirer aucun profit?
Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
4 Certainement tu abolis la crainte [de Dieu], et tu anéantis peu à peu la prière qu'on doit présenter au [Dieu] Fort.
Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
5 Car ta bouche fait connaître ton iniquité, et tu as choisi un langage trompeur.
Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
6 C'est ta bouche qui te condamne, et non pas moi; et tes lèvres témoignent contre toi.
Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
7 Es-tu le premier homme né? ou as-tu été formé avant les montagnes?
“Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
8 As-tu été instruit dans le conseil secret de Dieu, et renfermes-tu seul la sagesse?
Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
9 Que sais-tu que nous ne sachions? quelle connaissance as-tu que nous n'ayons?
Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
10 Il y a aussi parmi nous des hommes à cheveux blancs, et des gens d'une fort grande vieillesse, il y en a même de plus âgés que ton père.
Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
11 Les consolations du [Dieu] Fort te semblent-elles trop petites? et as-tu quelque chose de caché par-devers toi?
Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
12 Qu'est-ce qui t'ôte le cœur, et pourquoi clignes-tu les yeux?
Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
13 Que tu pousses ton souffle contre le [Dieu] Fort, et que tu fasses sortir de ta bouche de tels discours?
moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
14 Qu'est-ce que de l'homme [mortel], qu'il soit pur, et de celui qui est né de femme, qu'il soit juste?
“Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
15 Voici, [le Dieu fort] ne s'assure point sur ses saints, et les cieux ne se trouvent point purs devant lui;
Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
16 Et combien plus l'homme, qui boit l'iniquité comme l'eau, est-il abominable et impur?
nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
17 Je t'enseignerai, écoute-moi, et je te raconterai ce que j'ai vu;
“Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
18 Savoir ce que les sages ont déclaré, et qu'ils n'ont point caché; ce qu'ils avaient [reçu] de leurs pères;
zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
19 Eux à qui seuls la terre a été donnée, et parmi lesquels l'étranger n'est point passé.
(Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
20 Le méchant est [comme] en travail d'enfant tous les jours de sa vie, et un [petit] nombre d'années est réservé à l'homme violent.
Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
21 Un cri de frayeur est dans ses oreilles; au milieu de la paix [il croit] que le destructeur se jette sur lui.
Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
22 Il ne croit point pouvoir sortir des ténèbres; et il est toujours regardé de l'épée.
Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
23 Il court après le pain, en [disant]: où y en a-t-il? il sait que le jour de ténèbres est tout prêt, et il le touche comme avec la main.
Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
24 L'angoisse et l'adversité l'épouvantent, et chacune l'accable, comme un Roi équipé pour le combat.
Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
25 Parce qu'il a élevé sa main contre le [Dieu] Fort, et qu'il s'est roidi contre le Tout-puissant;
chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
26 Il lui sautera au collet, [et] sur l'épaisseur de ses gros boucliers.
Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
27 Parce que la graisse aura couvert son visage, et qu'elle aura fait des replis sur son ventre.
“Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
28 Et qu'il aura habité dans les villes détruites, et dans des maisons où il ne demeurait plus personne, et qui étaient réduites en monceaux de pierres.
munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
29 Mais il n'en sera pas plus riche, car ses biens ne subsisteront point, et leur entassement ne se répandra point sur la terre.
Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
30 Il ne pourra point se tirer des ténèbres; la flamme séchera ses branches encore tendres; il s'en ira par le souffle de la bouche du [Tout-puissant].
Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
31 Qu'il ne s'assure [donc] point sur la vanité par laquelle il a été séduit, car son changement lui sera inutile.
Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
32 Ce sera fait de lui avant son temps, ses branches ne reverdiront point.
Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
33 On lui ravira son aigret comme à une vigne; et on [lui] fera tomber ses boutons comme à un olivier.
Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
34 Car la bande des hypocrites sera désolée; le feu dévorera les tentes de [ceux qui reçoivent les] présents.
Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
35 Ils conçoivent le travail, et ils enfantent le tourment, et machinent dans le cœur des fraudes.
Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”

< Job 15 >