< Jérémie 44 >
1 La parole qui fut [adressée] à Jérémie touchant tous les Juifs qui demeuraient au pays d'Egypte, et qui habitaient à Migdol, à Taphnés, à Noph, et au pays de Patros, en disant:
Uthenga umene Yeremiya analandira wonena za Ayuda onse amene ankakhala ku Igupto, ku mizinda ya Migidoli, Tapanesi ndi Mefisi, ndiponso ku Patirosi ndi uwu:
2 Ainsi a dit l'Eternel des armées, le Dieu d'Israël: vous avez vu tout le mal que j'ai fait venir sur Jérusalem, et sur toutes les villes de Juda; et voici elles [sont] aujourd'hui un désert, et personne n'y demeure;
“Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu mwaona mavuto aakulu amene ndinawabweretsa pa Yerusalemu ndi mizinda yonse ya Yuda. Lero mizinda yonseyo yasanduka mabwinja, yopanda munthu wokhalamo.
3 A cause des maux qu'ils ont faits pour m'irriter, en allant faire des encensements pour servir d'autres dieux, lesquels ils n'ont point connus, ni eux, ni vous, ni vos pères.
Zimenezi zinachitika chifukwa cha zoyipa zomwe anachita. Iwo anaputa mkwiyo wanga pofukiza lubani ndi potumikira milungu ina imene iwo kapena inu ngakhalenso makolo anu sanayidziwe.
4 Et je vous ai envoyé tous mes serviteurs les Prophètes, me levant dès le matin, et les envoyant pour vous dire: ne commettez point maintenant cette chose abominable, laquelle je hais.
Kawirikawiri Ine ndakhala ndikutuma atumiki anga, aneneri, amene anati, ‘Musachite chinthu chonyansachi chimene Ine ndimadana nacho!’
5 Mais ils n'ont point écouté, et n'ont point incliné leur oreille pour se détourner de leur malice, afin de ne faire point d'encensements à d'autres dieux.
Koma iwo sanamvere kapena kulabadira; sanatembenuke kusiya zoyipa zawo kapena kuleka kufukiza lubani kwa milungu ina.
6 C'est pourquoi ma fureur et ma colère s'est répandue sur eux et s'est allumée dans les villes de Juda, et dans les rues de Jérusalem, qui sont réduites en désert, [et] en désolation, comme [il paraît] aujourd'hui.
Nʼchifukwa chake mkwiyo wanga unayaka ngati moto kutentha mizinda ya ku Yuda ndi misewu ya mu Yerusalemu ndi kuyisandutsa bwinja mpaka lero.
7 Maintenant donc, ainsi a dit l'Eternel, le Dieu des armées, le Dieu d'Israël: pourquoi faites-vous ce grand mal contre vous-mêmes, pour vous faire retrancher du milieu de Juda, hommes et femmes, petits enfants, et ceux qui tètent, afin qu'on ne vous laisse aucun de reste?
“Ndiye tsopano Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena kuti, ‘Chifukwa chiyani mukufuna kudziwononga chotere? Kodi mukufuna kuti amuna, akazi, ana ndi makanda onse aphedwe ndi kuti mu Yuda musatsale ndi munthu mmodzi yemwe?
8 En m'irritant par les œuvres de vos mains, en faisant des encensements à d'autres dieux dans le pays d'Egypte, auquel vous venez d'entrer pour y séjourner, afin que vous soyez retranchés, et que vous soyez en malédiction et en opprobre parmi toutes les nations de la terre?
Chifukwa chiyani mukuputa mkwiyo wanga popembedza mafano pofukiza lubani kwa milungu ina mʼdziko lino la Igupto mʼmene mukukhalamo. Kodi mukuchita zimenezi kuti mudziwononge nokha ndi kuti mudzisandutse chinthu choseketsa ndi chonyozeka pakati pa mitundu yonse ya dziko lapansi?
9 Avez-vous oublié les crimes de vos pères, et les crimes des Rois de Juda, et les crimes de leurs femmes, et vos propres crimes, et les crimes de vos femmes, qu'elles ont commis dans le pays de Juda, et dans les rues de Jérusalem?
Kodi mwayiwala zoyipa zimene anachita makolo anu, mafumu a ku Yuda ndi akazi awo, ndiponso zoyipa zimene munachita inuyo ndi akazi anu mʼdziko la Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
10 Jusques à ce jour ils n'ont point été affligés, ils n'ont point eu de crainte, et ils n'ont point marché en ma Loi, ni en mes ordonnances, que je vous ai proposées, et à vos pères aussi.
Koma mpaka lero simunalape. Simunandilemekeze kapena kumvera malamulo anga amene ndinayikira inuyo ndi makolo anu.
11 C'est pourquoi ainsi a dit l'Eternel des armées, le Dieu d'Israël: voici, je m'en vais tourner ma face contre vous pour vous nuire, et pour retrancher tout Juda.
“Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, ‘Ine ndatsimikiza zobweretsa mavuto pa inu ndi kuwatheratu anthu a ku Yuda.
12 Et je prendrai le reste de ceux de Juda qui se sont préparés pour entrer au pays d'Egypte, et y séjourner, et ils seront tous consumés; ils tomberont dans le pays d'Egypte, ils seront consumés par l'épée, et par la famine, depuis le plus petit jusqu’au plus grand; ils mourront par l'épée, et par la famine; et ils seront en exécration, en étonnement, en malédiction, et en opprobre.
Ndidzatenga anthu otsala a ku Yuda amene atsimikiza zopita ku Igupto ndi kukakhala kumeneko. Onse adzathera ku Igupto. Adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, adzaphedwa ndi lupanga kapena kufa ndi njala. Adzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, chinthu choseketsa ndi chonyozeka.
13 Et je punirai ceux qui demeurent au pays d'Egypte, comme j'ai puni Jérusalem, par l'épée, par la famine, et par la mortalité.
Ndidzalanga Ayuda okhala ku Igupto ndi lupanga, njala ndi mliri, ngati mmene ndinalangira anthu a ku Yerusalemu.
14 Et il n'y aura personne des restes de Juda d'entre ceux qui sont venus pour demeurer là, [c'est-à-dire], au pays d'Egypte, pour retourner au pays de Juda, auquel ils se promettent de retourner pour y demeurer, qui échappe, et qui y reste; car pas un ne retournera, sinon ceux qui se seront échappés [des autres].
Motero mwa anthu amene anapita ku Igupto palibe ndi mmodzi yemwe adzapulumuke, kapena kukhala ndi moyo, kapena kubwerera ku Yuda. Palibe amene adzabwerere kupatula othawa nkhondo.’”
15 Mais tous ceux qui savaient que leurs femmes faisaient des encensements à d'autres dieux, et toutes les femmes qui étaient là en grande compagnie; et tout le peuple qui demeurait dans le pays d'Egypte, à Patros, répondirent à Jérémie, en disant:
Tsono amuna onse amene anadziwa kuti akazi awo ankafukiza lubani kwa milungu ina, ndiponso akazi onse amene anali pamenepo, gulu lalikulu la anthu, pamodzi ndi anthu onse amene amakhala ku Patirosi mʼdziko la Igupto, anati kwa Yeremiya,
16 Quant à la parole que tu nous as dite au Nom de l'Eternel, nous ne t'écouterons point;
“Ife sitimvera uthenga umene watiwuza mʼdzina la Yehova!
17 Mais nous ferons assurément tout ce qui est sorti de notre bouche en faisant des encensements à la Reine des cieux, et lui faisant des aspersions, comme nous et nos pères, nos Rois, et les principaux d'entre nous avons fait dans les villes de Juda, et dans les rues de Jérusalem, et nous avons eu alors abondamment de pain, nous avons été à notre aise, et nous n'avons point vu de mal.
Koma tidzachitadi chilichonse chimene tinanena kuti tidzachita: Tidzafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndipo tidzayipatsa nsembe yachakumwa ngati mmene tinkachitira ifeyo ndi makolo athu, mafumu athu ndi akuluakulu mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu. Nthawi imeneyo ife tinali ndi chakudya chochuluka ndipo tinali pabwino, sitimapeza mavuto.
18 Mais depuis le temps que nous avons cessé de faire des encensements à la Reine des cieux, et de lui faire des aspersions, nous avons eu faute de tout, et nous avons été consumés par l'épée et par la famine.
Koma kuchokera nthawi imene tinasiya kufukiza lubani ndi kupereka chopereka cha chakumwa kwa mfumukazi yakumwamba, ifeyo takhala tikusowa zinthu ndipo takhala tikuphedwa ndi lupanga ndi kufa ndi njala.”
19 Quand nous faisions des encensements à la Reine des cieux, et quand nous lui faisions des aspersions, lui avons-nous offert à l'insu de nos maris des gâteaux sur lesquels elle était représentée, ou lui avons-nous répandu des aspersions?
Akazi anawonjezera kunena kuti, “Pamene tinkafukiza lubani kwa mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa, kodi suja amuna athu ankavomereza mmene timayipangira mfumukazi yakumwambayo makeke abwino olembapo chinthunzi chake ndi kuyipatsa chopereka cha chakumwa?”
20 Alors Jérémie parla à tout le peuple, contre les hommes, et contre les femmes, et contre tout le peuple qui avait fait cette réponse, et leur dit:
Yeremiya atamva kuyankha kumeneku anawawuza kuti,
21 L'Eternel ne s'est-il pas souvenu des encensements que vous avez faits dans les villes de Juda, et dans les rues de Jérusalem, vous et vos pères, vos Rois et les principaux d'entre vous, et le peuple du pays, et son cœur n'en a-t-il pas été touché?
“Kodi mukuganiza kuti Yehova nʼkuyiwala kuti inuyo ndi makolo anu, mafumu anu ndi akuluakulu anu, ndiponso anthu onse, munkafukiza lubani kwa mafano a mʼmizinda ya ku Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu?
22 En sorte que l'Eternel ne l'a pu supporter davantage, à cause de la malice de vos actions, et à cause des abominations que vous avez commises; tellement que votre pays a été réduit en désert, et en étonnement, et en malédiction, sans que personne y habite, comme [il paraît] aujourd'hui.
Ndiye Yehova sakanathanso kupirira ndi machitidwe anu ndi zonyansa zimene munkachita. Nʼchifukwa chake dziko lanu linasanduka chipululu, chinthu choopsa ndi chotembereredwa. Dziko lopandamo anthu monga zilili lero lino.
23 Parce donc que vous avez fait ces encensements, et que vous avez péché contre l'Eternel, et que vous n'avez point écouté la voix de l'Eternel, et n'avez point marché en sa Loi, ni en ses ordonnances, ni en ses témoignages, à cause de cela ce mal vous est arrivé, comme [il paraît] aujourd'hui.
Mavuto awa akugwerani chifukwa munkafukiza lubani ndipo munkachimwira Yehova pokana kumvera mawu ake ndi kutsatira malamulo ndi malangizo ake.”
24 Puis Jérémie dit à tout le peuple, et à toutes les femmes: vous tous ceux de Juda, qui êtes au pays d'Egypte, écoutez la parole de l'Eternel.
Kenaka Yeremiya anawuza anthu onse, makamaka akazi kuti, “Imvani mawu a Yehova, anthu onse a ku Yuda amene muli mu Igupto.
25 Ainsi a parlé l'Eternel des armées le Dieu d'Israël, en disant: c'est vous, et vos femmes qui ont parlé par votre bouche touchant ce que vous avez accompli de vos mains, en disant: certainement nous accomplirons nos vœux que nous avons voués, en faisant des encensements à la Reine des cieux; et lui faisant des aspersions. Vous avez entièrement accompli vos vœux, et vous les avez effectués très exactement.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Inu ndi akazi anu munalonjeza ndi pakamwa panu, ndipo malonjezowo mwakwaniritsa. Inu munanena kuti, ‘Tidzachita zimene tinalonjeza, kufukizira lubani mfumukazi yakumwamba ndi kuyipatsa chopereka cha zakumwa.’ Tsopano chitanitu zimene munalonjezazo! Kwaniritsani malumbiro anu. “Yambani, chitani zimene munalonjeza! Kwaniritsani malumbiro anu!
26 C'est pourquoi écoutez la parole de l'Eternel, vous tous ceux de Juda qui demeurez au pays d'Egypte: voici, j'ai juré par mon grand Nom, a dit l'Eternel, que mon Nom ne sera plus réclamé par la bouche d'aucun de Juda, qui dise en tout le pays d'Egypte: le Seigneur l'Eternel est vivant.
Koma imvani mawu a Yehova, inu Ayuda nonse amene mukukhala mu Igupto: Yehova akuti, ‘Ine ndikulumbira mʼdzina langa lopambana kuti palibe wochokera ku Yuda amene akukhala mu Igupto amene adzatchule dzina langa polumbira kuti, ‘Pali Ambuye Yehova wamoyo.’
27 Voici, je veille contre eux pour [leur] mal, et non pour [leur] bien; et tous les hommes de Juda qui sont au pays d'Egypte seront consumés par l'épée, et par la famine, jusqu’à ce qu'il n'y en ait plus aucun.
Pakuti ndionetsetsa kuti ndiwachitire choyipa, osati chabwino. Anthu a ku Yuda amene akukhala ku Igupto adzaphedwa pa nkhondo. Ena adzafa ndi njala mpaka onse atatheratu.
28 Et ceux qui seront échappés de l'épée retourneront du pays d'Egypte au pays de Juda en fort petit nombre, et tout le reste de ceux de Juda qui seront entrés au pays d'Egypte pour y séjourner, saura quelle est la parole qui s'accomplira, la mienne, ou la leur.
Amene adzapulumuke ku lupanga ndi kubwerera ku dziko la Yuda kuchokera ku Igupto adzakhala ochepa kwambiri. Choncho otsala onse a ku Yuda amene anapita kukakhala ku Igupto adzadziwa kuti mawu woona ndi ati, anga kapena awo.
29 Et ceci vous sera pour signe, dit l'Eternel, que je vous punirai en ce lieu-ci, afin que vous sachiez que mes paroles seront infailliblement accomplies contre vous en mal.
“Ine Yehova ndikukupatsani chizindikiro chakuti ndidzakulangani ku malo ano. Motero mudzadziwa kuti mawu anga akuti ndidzakulangani ndi woona.
30 Ainsi a dit l'Eternel: voici, je m'en vais livrer Pharaon-Hophrah Roi d'Egypte en la main de ses ennemis, et en la main de ceux qui cherchent sa vie, comme j'ai livré Sédécias Roi de Juda en la main de Nébucadnetsar Roi de Babylone son ennemi, et qui cherchait sa vie.
Yehova akuti, ‘Ine ndidzamupereka Farao Hofira mfumu ya Igupto kwa adani ake amene akufuna kumupha, monga momwe ndinaperekera Zedekiya mfumu ya Yuda kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, mdani wake amene ankafuna kumupha.’”