< Jérémie 36 >
1 Or il arriva, en la quatrième année de Jéhojakim fils de Josias Roi de Juda, que cette parole fut [adressée] par l'Eternel à Jérémie, en disant:
Chaka chachinayi cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
2 Prends-toi un rouleau de livre, et y écris toutes les paroles que je t'ai dites contre Israël, et contre Juda, et contre toutes les nations, depuis le jour que je t'ai parlé, [c'est-à-dire], depuis les jours de Josias, jusqu’à aujourd'hui.
“Tenga buku ndipo ulembemo mawu onse amene ndayankhula nawe otsutsa Israeli, Yuda ndi mitundu yonse ya anthu, kuyambira nthawi imene ndinayamba kuyankhula nawe pa nthawi ya ulamuliro wa Yosiya mpaka lero lino.
3 Peut-être que la maison de Juda fera attention à tout le mal que je pense de leur faire, afin que chacun se détourne de sa mauvaise voie, et que je leur pardonne leur iniquité, et leur péché.
Mwina mwake anthu a ku Yuda adzamva za zoopsa zonse zimene ndakonza kuti ndiwachitire, ndipo munthu aliyense adzatembenuka ndi kusiya ntchito zake zoyipa. Motero ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndi machimo awo.”
4 Jérémie donc appela Baruc, fils de Nérija, et Baruc écrivit de la bouche de Jérémie dans le rouleau de livre toutes les paroles de l'Eternel, lesquelles il lui dicta.
Tsono Yeremiya anayitana Baruki mwana wa Neriya. Baruki analemba mʼbuku mawu onse amene Yeremiya ankamuwuza, mawu amene Yehova anamuwuza Yeremiya.
5 Puis Jérémie donna charge à Baruc, en disant: je suis retenu, [et] je ne puis entrer dans la maison de l'Eternel.
Kenaka Yeremiya anawuza Baruki kuti, “Ine andiletsa kupita ku Nyumba ya Mulungu.
6 Tu y entreras donc, et tu liras dans le rouleau que tu as écrit, [et que je t'ai dicté] de ma bouche, les paroles de l'Eternel, le peuple l'entendant, en la maison de l'Eternel, au jour du jeûne; tu les liras, dis-je, tous ceux de Juda, qui seront venus de leurs villes, l'entendant.
Tsono iwe upite ku Nyumba ya Yehova pa tsiku losala kudya ndipo ukawerenge mawu a Yehova ochokera mʼbukumu amene ndinakulembetsa anthu onse akumva. Ukawawerengere anthu onse a ku Yuda amene amabwera ku Nyumba ya Mulungu kuchokera ku mizinda yawo.
7 Peut-être que leur supplication sera reçue devant l'Eternel, et que chacun se détournera de sa mauvaise voie; car la colère et la fureur que l'Eternel a déclarée contre ce peuple [est] grande.
Mwina mwake adzapempha kwa Yehova ndipo aliyense adzatembenuka ndi kusiya makhalidwe ake oyipa pakuti mkwiyo ndi ukali wa Yehova pa anthu awa ndi woopsa kwambiri.”
8 Baruc donc fils de Nérija fit selon tout ce que Jérémie le Prophète lui avait commandé, lisant dans le livre les paroles de l'Eternel, en la maison de l'Eternel.
Baruki mwana wa Neriya anachita zonse zimene mneneri Yeremiya anamuwuza kuti achite. Mʼnyumba ya Yehova, iye anawerenga mawu a Yehova ochokera mʼbukulo.
9 Or il arriva en la cinquième année de Jéhojakim fils de Josias Roi de Juda, au neuvième mois, qu'on publia le jeûne en la présence de l'Eternel à tout le peuple de Jérusalem et à tout le peuple qui était venu des villes de Juda à Jérusalem.
Pa mwezi wachisanu ndi chinayi wa chaka chachisanu cha Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, anthu onse a mu Yerusalemu ndi onse amene anabwera kumeneko kuchokera ku mizinda ya Yuda, anapangana za kusala kudya kuti apepese Yehova.
10 Et Baruc lut dans le livre les paroles de Jérémie, en la maison de l'Eternel, dans la chambre de Guémaria fils de Saphan, Secrétaire, dans le haut parvis, à l'entrée de la porte neuve de la maison de l'Eternel, tout le peuple l'entendant.
Atayima pa chipinda cha Gemariya mwana wa mlembi Safani, chimene chinali mʼbwalo lapamwamba, pafupi ndi Chipata Chatsopano cholowera ku Nyumba ya Yehova, Baruki anawerenga mawu onse a Yeremiya amene anali mʼbuku muja kwa anthu onse amene anali ku Nyumba ya Yehova.
11 Et quand Michée fils de Guémaria, fils de Saphan, eut ouï [par la lecture] du livre toutes les paroles de l'Eternel;
Mikaya mwana wa Gemariya, mwana wa Safani, atamva mawu onse a Yehova ochokera mʼbukumo,
12 Il descendit en la maison du Roi vers la chambre du Secrétaire, et voici tous les principaux y étaient assis, [savoir] Elisamah le Secrétaire, et Délaia fils de Sémahia, Elnathan fils de Hacbor, et Guémaria fils de Saphan, et Sédécias fils de Hanania, et tous les principaux.
anapita ku nyumba ya mfumu nakalowa ku chipinda cha mlembi. Akuluakulu, mlembi Elisama, Delaya mwana wa Semaya, Elinatani mwana wa Akibori, Gemariya mwana wa Safani, Zedekiya mwana wa Hananiya pamodzi ndi akuluakulu ena onse, anali atasonkhana kumeneko.
13 Et Michée leur rapporta toutes les paroles qu'il avait ouïes quand Baruc lisait au livre le peuple l'entendant.
Tsono Mikaya anawafotokozera mawu onse amene anamva pamene Baruki ankawerenga buku lija anthu onse akumva.
14 C'est pourquoi tous les principaux envoyèrent vers Baruc, Jéhudi, fils de Néthania, fils de Sélemja, fils de Cusci, pour lui dire: prends en ta main le rouleau dans lequel tu as lu, le peuple l'entendant, et viens ici. Baruch donc fils de Nérija prit le rouleau en sa main, et vint vers eux.
Pambuyo pake akuluakulu onsewo anatuma Yehudi mwana wa Netaniya, mwana wa Selemiya, mwana wa Kusi, kwa Baruki kukamuwuza kuti, “Bwera ndi buku limene unawerenga kwa anthu.” Ndipo Baruki mwana wa Neriya anapita nalo bukulo kwa anthuwo.
15 Et ils lui dirent: assieds-toi maintenant, et y lis, nous l'entendant; et Baruc lut, eux l'écoutant.
Iwo anati, “Khala pansi, ndipo tiwerengere bukuli.” Ndipo Baruki anawawerengera.
16 Et il arriva que sitôt qu'ils eurent ouï toutes ces paroles, ils furent effrayés entre eux, et dirent à Baruc: nous ne manquerons point de rapporter au Roi toutes ces paroles.
Atamva mawu onsewo, anayangʼanana mwa mantha ndipo anamuwuza Baruki kuti, “Ndithudi tikafotokozera mfumu mawu onsewa.”
17 Et ils interrogèrent Baruc, en disant: déclare-nous maintenant comment tu as écrit toutes ces paroles-là de sa bouche.
Tsono anamufunsa Baruki kuti, “Tatiwuze, unalemba bwanji mawu onsewa? Kodi ndi Yeremiya anakulembetsa zimenezi?”
18 Et Baruc leur dit: il me dictait de sa bouche toutes ces paroles, et je les écrivais avec de l'encre dans le livre.
Baruki anayankha kuti, “Inde, ndi Yeremiya amene anandiwuza mawu onsewa, ndipo ine ndinawalemba ndi utoto mʼbukumu.”
19 Alors les principaux dirent à Baruc: va, et te cache, toi et Jérémie, et que personne ne sache où vous serez.
Kenaka akuluakuluwo anamuwuza Baruki kuti, “Iweyo ndi Yeremiya, pitani mukabisale. Munthu aliyense asadziwe kumene muli.”
20 Puis ils s'en allèrent vers le Roi au parvis, mais ils mirent en garde le rouleau dans la chambre d'Elisamah le Secrétaire; et ils racontèrent toutes ces paroles, le Roi l'entendant.
Atayika bukulo mʼchipinda cha mlembi Elisama, analowa mʼbwalo, napita kwa mfumu ndi kukayifotokozera zonse.
21 Et le Roi envoya Jéhudi pour prendre le rouleau; et quand Jéhudi l'eut pris de la chambre d'Elisamah le Secrétaire, il le lut, le Roi et tous les principaux qui assistaient autour de lui l'entendant.
Itamva zimenezi mfumu inatuma Yehudi kuti akatenge bukulo, ndipo Yehudi anakalitenga ku chipinda cha mlembi Elisama ndipo anawerengera mfumu pamodzi ndi akuluakulu ake amene anali naye.
22 Or le Roi était assis dans l'appartement d'hiver, au neuvième mois, et [il y avait] devant lui un brasier ardent.
Unali mwezi wachisanu ndi chinayi ndipo mfumu inali mʼnyumba ya pa nyengo yozizira, ikuwotha moto umene anasonkha.
23 Et il arriva qu'aussitôt que Jéhudi en eut lu trois ou quatre pages, le Roi le coupa avec le canif du Secrétaire, et le jeta au feu du brasier, jusqu'à ce que tout le rouleau fût consumé au feu qui [était] dans le brasier.
Yehudi ankati akawerenga masamba atatu kapena anayi a bukulo, mfumu inkawangʼamba ndi mpeni ndi kuwaponya pa moto ndipo anapitiriza kuchita zimenezi mpaka buku lonse linapsa.
24 Et ni le Roi ni tous ses serviteurs qui entendirent toutes ces paroles n'en furent point effrayés, et ne déchirèrent point leurs vêtements.
Mfumu pamodzi ndi omutumikira ake onse amene anamva mawu onsewa sanachite mantha kapena kungʼamba zovala zawo.
25 Toutefois Elnathan, et Délaia, et Guémaria intercédèrent envers le Roi, afin qu'il ne brûlât point le rouleau, mais il ne les écouta point.
Ngakhale kuti Elinatani, Delaya, ndi Gemariya anapempha mfumu kuti isatenthe bukulo, mfumuyo sinawamvere.
26 Même le Roi commanda à Jérahméel fils de Hammélec, et à Séraja fils de Hazriel, et à Sélemja fils de Habdéel, de saisir Baruc le secrétaire, et Jérémie le Prophète; mais l'Eternel les cacha.
Mʼmalo mwake, mfumu inalamula Yerahimeeli mwana wake, Seraya mwana wa Azirieli ndi Selemiya mwana wa Abideeli kuti agwire mlembi Baruki ndi mneneri Yeremiya. Koma pamenepo nʼkuti Yehova atawabisa.
27 Et la parole de l'Eternel fut [adressée] à Jérémie, après que le Roi eut brûlé le rouleau, et les paroles que Baruc avait écrites de la bouche de Jérémie, en disant:
Mfumu itatentha buku limene linali ndi mawu amene Yeremiya anamulembetsa Baruki, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
28 Prends encore un autre rouleau, et y écris toutes les premières paroles qui étaient dans le premier rouleau que Jéhojakim Roi de Juda a brûlé.
“Tenganso buku lina ndipo ulembe mawu onse amene anali mʼbuku loyamba lija, limene Yehoyakimu analitentha.
29 Et tu diras à Jéhojakim Roi de Juda: ainsi a dit l'Eternel: tu as brûlé ce rouleau, et tu as dit: pourquoi y as-tu écrit, en disant que le Roi de Babylone viendra certainement, et qu'il ravagera ce pays, et en exterminera les hommes et les bêtes?
Ndiponso akamuwuze Yehoyakimu mfumu ya Yuda kuti, ‘Yehova akuti: Iwe unatentha buku lija ndipo unati: Nʼchifukwa chiyani unalemba kuti mfumu ya ku Babuloni idzabwera ndithu kudzawononga dziko lino ndi kupha anthu pamodzi ndi nyama zomwe?’
30 C'est pourquoi ainsi a dit l'Eternel touchant Jéhojakim Roi de Juda: il n'aura personne qui soit assis sur le trône de David, et son corps mort sera jeté de jour à la chaleur, et de nuit à la gelée.
Nʼchifukwa chake kunena za Yehoyakimu mfumu ya Yuda Yehova akuti sipadzaoneka munthu wina wolowa mʼmalo mwake pa mpando wa Davide. Akadzafa mtembo wake udzaponyedwa kunja ndipo udzakhala pa dzuwa masana, ndi pachisanu chowundana usiku.
31 Je visiterai donc sur lui, et sur sa postérité, et sur ses serviteurs, leur iniquité; et je ferai venir sur eux, et sur les habitants de Jérusalem, et sur les hommes de Juda, tout le mal que je leur ai prononcé, et qu'ils n'ont point écouté.
Ndidzamulanga pamodzi ndi ana ake ndiponso omutumikira ake chifukwa cha zoyipa zawo; ndidzagwetsa pa iwo ndi pa onse amene akukhala mu Yerusalemu ndiponso pa anthu a ku Yuda masautso onse amene ndinawanena, chifukwa sanamvere.”
32 Jérémie donc prit un autre rouleau, et le donna à Baruc fils de Nérija Secrétaire, lequel y écrivit de la bouche de Jérémie toutes les paroles du livre que Jéhojakim Roi de Juda avait brûlé au feu, et plusieurs paroles semblables y furent encore ajoutées.
Choncho Yeremiya anatenga buku lina napatsa mlembi Baruki mwana wa Neriya, ndipo Yeremiya anamulembetsa mawu onse amene anali mʼbuku limene Yehoyakimu mfumu ya Yuda anatentha. Ndipo anawonjezerapo mawu ambiri monga omwewo.