< Jérémie 33 >

1 Et la parole de l'Eternel fut [adressée] une seconde fois à Jérémie, quand il était encore enfermé dans la cour de la prison, en disant:
Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
2 Ainsi a dit l'Eternel qui s'en va faire ceci, l'Eternel qui s'en va le former pour l'établir, le Nom duquel est l'Eternel.
“Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
3 Crie vers moi, je te répondrai, et je te déclarerai des choses grandes et cachées, lesquelles tu ne sais point.
‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
4 Car ainsi a dit l'Eternel, le Dieu d'Israël, touchant les maisons de cette ville-ci, et les maisons des Rois de Juda; elles s'en vont être démolies par le moyen des terrasses, et par l'épée.
Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
5 Ils sont venus à combattre contre les Caldéens, mais ç'a été pour remplir leurs maisons des corps morts des hommes que j'ai fait frapper en ma colère et en ma fureur, et parce que j'ai caché ma face de cette ville à cause de toute leur malice.
Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
6 Voici, je m'en vais lui donner la santé et la guérison, je les guérirai, et je leur ferai voir abondance de paix et de vérité.
“‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
7 Et je ferai retourner les captifs de Juda, et les captifs d'Israël, et je les rétablirai comme auparavant.
Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
8 Et je les purifierai de toute leur iniquité, par laquelle ils ont péché contre moi; et je pardonnerai toutes leurs iniquités par lesquelles ils ont péché contre moi, et par lesquelles ils ont péché grièvement contre moi.
Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
9 Et [cette ville] me sera un sujet de réjouissance, de louange et de gloire, chez toutes les nations de la terre qui entendront parler de tout le bien que je vais leur faire, et elles seront effrayées et épouvantées à cause de tout le bien, et de toute la prospérité que je vais lui donner.
Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
10 Ainsi a dit l'Eternel: dans ce lieu-ci duquel vous dites: il est désert, n'y ayant ni homme ni bête, dans les villes de Juda, et dans les rues de Jérusalem, qui sont désolées, n'y ayant ni homme, ni habitant, ni aucune bête, on y entendra encore,
“Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
11 La voix de joie, et la voix d'allégresse, la voix de l'époux, et la voix de l'épouse, [et] la voix de ceux qui disent: célébrez l'Eternel des armées; car l'Eternel est bon, parce que sa miséricorde demeure à toujours, lorsqu'ils apportent des oblations d'action de grâces à la maison de l'Eternel; car je ferai retourner les captifs de ce pays, [et je les mettrai] au même état qu'auparavant, a dit l'Eternel.
mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
12 Ainsi a dit l'Eternel des armées: en ce lieu désert, où il n'y a ni homme ni bête, et dans toutes ses villes, il y aura encore des cabanes de bergers qui y feront reposer leurs troupeaux;
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
13 Dans les villes des montagnes, et dans les villes de la plaine, dans les villes du Midi, dans le pays de Benjamin, dans les environs de Jérusalem, et dans les villes de Juda; et les troupeaux passeront encore sous les mains de celui qui les compte, a dit l'Eternel.
Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
14 Voici, les jours viennent, dit l'Eternel, que je mettrai en effet la bonne parole que j'ai prononcée touchant la maison d'Israël, et la maison de Juda.
“‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
15 En ces jours-là, et en ce temps-là je ferai germer à David le Germe de justice, qui exercera le jugement et la justice en la terre.
“‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
16 En ces jours-là Juda sera délivré, et Jérusalem habitera en assurance, et c'est ici le nom dont elle sera appelée: l'Eternel notre justice.
Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
17 Car ainsi a dit l'Eternel, il ne manquera jamais à David d'homme assis sur le trône de la maison d'Israël;
Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
18 Et d'entre les Sacrificateurs Lévites, il ne manquera jamais d'y avoir devant moi d'homme offrant des holocaustes, faisant les parfums de gâteau, et faisant des sacrifices tous les jours.
ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
19 Davantage la parole de l'Eternel fut [adressée] à Jérémie, en disant:
Yehova anawuza Yeremiya kuti:
20 Ainsi a dit l'Eternel: Si vous pouvez abolir mon alliance touchant le jour, et mon alliance touchant la nuit, tellement que le jour et la nuit ne soient plus en leur temps;
Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
21 Aussi mon alliance avec David mon serviteur sera abolie; tellement qu'il n'ait plus de fils régnant sur son trône; et avec les Lévites Sacrificateurs, faisant mon service.
Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
22 Car [comme] on ne peut compter l'armée des cieux, ni mesurer le sable de la mer, ainsi je multiplierai la postérité de David mon serviteur, et les Lévites qui font mon service.
Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
23 La parole de l'Eternel fut encore [adressée] à Jérémie, en disant:
Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
24 N'as-tu pas vu ce que ce peuple a prononcé, disant: l'Eternel a rejeté les deux familles qu'il avait élues; car [par là] ils méprisent mon peuple; tellement qu'à leur compte il ne sera plus une nation?
“Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
25 Ainsi a dit l'Eternel: si [je n'ai point établi] mon alliance touchant le jour et la nuit, et si je n'ai point établi les ordonnances des cieux et de la terre;
‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
26 Aussi rejetterai-je la postérité de Jacob, et celle de David mon serviteur, pour ne prendre plus de sa postérité des gens qui dominent sur la postérité d'Abraham, d'Isaac, et de Jacob; car je ferai retourner leurs captifs, et j'aurai compassion d'eux.
monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”

< Jérémie 33 >