< Jérémie 2 >
1 Et la parole de l'Eternel me fut [adressée], en disant:
Yehova anandiwuza kuti,
2 Va, et crie, ceux de Jérusalem l'entendant, et dis: Ainsi a dit l'Eternel: il me souvient [pour l'amour] de toi de la compassion que j'ai eue pour toi en ta jeunesse, et de l'amour de tes épousailles, quand tu venais après moi dans le désert, en un pays qu'on ne sème point.
“Pita ukalengeze kwa anthu a ku Yerusalemu kuti Yehova akuti, “‘Ine ndikukumbukira mmene umakhulupirikira pa unyamata wako, mmene unkandikondera ngati momwe amachitira mkwatibwi, mmene unkanditsata mʼchipululu muja; mʼdziko losadzalamo kanthu.
3 Israël était une chose sainte à l'Eternel, c'étaient les prémices de son revenu; tous ceux qui le dévoraient étaient [trouvés] coupables, il leur en arrivait du mal, dit l'Eternel.
Israeli anali wopatulika wa Yehova, anali ngati zipatso zake zoyamba kucha pa nthawi yokolola; onse amene anamuzunza anapezeka kuti ndi olakwa ndipo mavuto anawagwera,’” akutero Yehova.
4 Ecoutez la parole de l'Eternel, maison de Jacob, et vous toutes les familles de la maison d'Israël:
Imvani mawu a Yehova, inu zidzukulu za Yakobo, inu mafuko onse a Israeli.
5 Ainsi a dit l'Eternel: quelle injustice ont trouvée vos pères en moi, qu'ils se soient éloignés de moi, qu'ils aient marché après la vanité, et qu'ils soient devenus vains?
Yehova akuti, “Kodi makolo anu anandipeza nʼcholakwa chanji, kuti andithawe? Iwo anatsata milungu yachabechabe, nawonso nʼkusanduka achabechabe.
6 Et ils n'ont point dit: où est l'Eternel qui nous a fait remonter du pays d'Egypte, qui nous a conduits par un désert, par un pays de landes et montagneux, par un pays aride et d'ombre de mort, par un pays où aucun homme n'avait passé, et où personne n'avait habité?
Iwo sanafunse nʼkomwe kuti, ‘Kodi Yehova ali kuti, amene anatitulutsa mʼdziko la Igupto natitsogolera mʼchipululu mʼdziko lowuma ndi lokumbikakumbika, mʼdziko lopanda mvula ndi la mdima, dziko limene munthu sadutsamo ndipo simukhala munthu aliyense?’
7 Car je vous ai fait entrer dans un pays de Carmel, afin que vous mangeassiez ses fruits, et de ses biens; mais sitôt que vous [y] êtes entrés, vous avez souillé mon pays, et avez rendu abominable mon héritage.
Ndinakufikitsani ku dziko lachonde kuti mudye zipatso zake ndi zabwino zake zina. Koma inu mutafika munaliyipitsa dziko langa ndi kusandutsa cholowa changa kukhala chonyansa.
8 Les Sacrificateurs n'ont point dit: où est l'Eternel? Et ceux qui expliquaient la Loi, ne m'ont point connu; et les pasteurs ont prévariqué contre moi, et les prophètes ont prophétisé de par Bahal, et ont marché après des choses qui ne profitent de rien.
Ansembe nawonso sanafunse kuti, ‘Yehova ali kuti?’ Iwo amene amaphunzitsa malamulo sanandidziwe; atsogoleri anandiwukira. Aneneri ankanenera mʼdzina la Baala, ndi kutsatira mafano achabechabe.
9 Pour cette cause encore je plaiderai avec vous, dit l'Eternel, et je plaiderai avec les enfants de vos enfants.
“Chifukwa chake Ine ndidzakuyimbaninso mlandu,” akutero Yehova. “Ndipo ndidzayimbanso mlandu zidzukulu zanu.
10 Car passez par les Îles de Kittim, et voyez; envoyez en Kédar, et considérez bien, et regardez s'il y a eu rien de tel.
Pitani kumadzulo ku chilumba cha Kitimu, ndipo mukaone, tumizani anthu ku Kedara kuti akafufuze bwino; ndipo muona kuti zinthu zoterezi sizinachitikepo nʼkale lomwe:
11 Y a-t-il aucune nation qui ait changé de dieux, lesquels toutefois ne [sont] pas dieux? Mais mon peuple a changé sa gloire en ce qui ne profite de rien.
Kodi ulipo mtundu wa anthu uliwonse umene unasinthapo milungu yake? (Ngakhale kuti si milungu nʼkomwe). Koma anthu anga asinthitsa Mulungu wawo waulemerero ndi mafano achabechabe.
12 Cieux soyez étonnés de ceci; ayez-[en] de l'horreur, et soyez extrêmement asséchés, dit l'Eternel.
Inu mayiko akumwamba, dabwani ndi zimenezi, ndipo njenjemerani ndi mantha aakulu,” akutero Yehova.
13 Car mon peuple a fait deux maux; ils m'ont abandonné, moi [qui suis] la source des eaux vives, pour se creuser des citernes, des citernes crevassées qui ne peuvent point contenir d'eau.
“Popeza anthu anga achita machimo awiri: Andisiya Ine kasupe wa madzi a moyo, ndi kukadzikumbira zitsime zawo, zitsime zongʼaluka, zomwe sizingathe kusunga madzi.
14 Israël est-il un esclave, ou un esclave né dans la maison? pourquoi donc a-t-il été mis au pillage?
Israeli si wantchito kapena kapolo wobadwira mʼnyumba, ayi. Nanga nʼchifukwa chiyani amuwononga chotere?
15 Les lionceaux ont rugi, et ont jeté leur cri sur lui; et on a mis leur pays en désolation, ses villes ont été brûlées, de sorte qu'il n'y a personne qui y habite.
Adani ake abangulira ndi kumuopseza ngati mikango. Dziko lake analisandutsa bwinja; mizinda yake anayitentha popanda wokhalamo.
16 Même les enfants de Noph, et de Taphnés te casseront le sommet de la tête.
Ndiponso Aigupto a ku Mefisi ndi a ku Tapanesi akuphwanyani mitu.
17 Ne t'es-tu pas fait cela parce que tu as abandonné l'Eternel ton Dieu, dans le temps qu'il te menait par le chemin?
Zimenezitu zakuchitikirani chifukwa munasiya Yehova Mulungu wanu pamene Iye ankakutsogolerani pa njira yanu?
18 Et maintenant, qu'as-tu affaire d'aller en Egypte pour y boire de l'eau de Sihor? et qu'as-tu affaire d'aller en Assyrie, pour y boire de l'eau du fleuve?
Tsopano mudzapindula chiyani mukapita ku Igupto, kukamwa madzi a mu Sihori? Ndipo mudzapindulanji mukapita ku Asiriya, kukamwa madzi a mu mtsinje wa Yufurate?
19 Ta malice te châtiera, et tes débauches te réprimanderont, afin que tu saches et que tu voies que c'est une chose mauvaise et amère, que tu aies abandonné l'Eternel ton Dieu, et que tu ne sois point rempli de ma frayeur, dit le Seigneur l'Eternel des armées.
Kuyipa kwanuko kudzakulangani; kubwerera mʼmbuyo kwanuko kudzakutsutsani. Tsono ganizirani bwino, popeza ndi chinthu choyipa kundisiya Ine Yehova Mulungu wanu; ndi chinthu chowawa ndithu kusandiopa Ine Mulungu wanu. Akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
20 Parce que depuis longtemps j'ai brisé ton joug, et rompu tes liens, tu as dit: je ne serai plus dans la servitude; c'est pourquoi tu as erré en te prostituant sur toute haute colline, et sous tout arbre vert.
“Kuyambira kalekale inu munathyola goli lanu ndi kudula msinga zanu; munanena kuti, ‘Sitidzakutumikirani!’ Ndithudi, inu mwakhala ngati mkazi wachiwerewere. Mukupembedza milungu ina pa phiri lililonse lalitali ndiponso pansi pa mtengo uliwonse wa masamba ambiri.
21 Or je t'avais moi-même plantée [comme] une vigne exquise, de laquelle tout le plant était franc; comment donc t'es-tu changée en sarments d'une vigne abâtardie?
Ine ndinakudzala iwe ngati mtengo wampesa wosankhika; unali mpesa wabwino kwambiri ndi wodalirika. Nanga nʼchifukwa chiyani wasanduka mpesa wachabechabe wonga wa kutchire?
22 Quand tu te laverais avec du nitre, et que tu prendrais beaucoup de savon, ton iniquité [demeurerait] encore marquée devant moi, dit le Seigneur l'Eternel.
Ngakhale utasamba ndi soda kapena kusambira sopo wambiri, kuthimbirira kwa machimo ako kumaonekabe pamaso panga,” akutero Ambuye Yehova.
23 Comment dis-tu: je ne me suis point souillée, je ne suis point allée après les Bahalins? Regarde ton train dans la vallée, reconnais ce que tu as fait, dromadaire légère, qui ne tiens point de route certaine.
“Iwe ukunena bwanji kuti, ‘Ine sindinadziyipitse; sindinatsatire Abaala’? Takumbukira mmene unkandichimwira mʼchigwa muja; zindikira bwino zomwe wachita. Iwe uli ngati ngamira yayikazi yaliwiro yomangothamanga uku ndi uku,
24 Anesse sauvage, accoutumée au désert, humant le vent à son plaisir; et qui est-ce qui lui pourrait faire rebrousser sa course? nul de ceux qui la cherchent ne se lassera après elle, on la trouvera en son mois.
wakhala ngati mbidzi yozolowera mʼchipululu, yonka ninunkhiza pa nthawi yachisika. Ndani angayiretse chilakolako chakecho? Mphongo iliyonse yoyikhumba sidzavutika. Pa nthawi yachisika chakecho mphongoyo idzayipeza.
25 Retiens ton pied, que tu ne marches déchaussée, et ton gosier, que tu ne sois altérée. Mais tu as dit: c'en est fait. Non; car j'aime les étrangers, et j'irai après eux.
Iwe usathamange, nsapato zingakuthere kuphazi ndi kukhosi kwako kuwuma ndi ludzu. Koma unati, ‘Zamkutu! Ine ndimakonda milungu yachilendo, ndipo ndidzayitsatira.’
26 Comme le larron est confus, quand il est surpris, ainsi sont confus ceux de la maison d'Israël, eux, leurs Rois, les principaux d'entre eux, leurs Sacrificateurs, et leurs Prophètes;
“Monga momwe mbala imachitira manyazi pamene yagwidwa, moteronso nyumba ya Israeli idzachita manyazi; Aisraeliwo, mafumu ndi akuluakulu awo, ansembe ndi aneneri awo.
27 Qui disent au bois: tu es mon père; et à la pierre: tu m'as engendré. Car ils m'ont tourné le dos, et non pas la face; puis ils disent dans le temps de leur calamité: lève-toi, et nous délivre.
Iwo amawuza mtengo kuti, ‘Iwe ndiwe abambo athu,’ ndipo amawuza mwala kuti, ‘Iwe ndiye amene unatibala.’ Iwo andifulatira Ine, ndipo safuna kundiyangʼana; Koma akakhala pa mavuto amati, ‘Bwerani mudzatipulumutse!’
28 Et où sont tes dieux que tu t'es faits? qu'ils se lèvent pour voir s'ils te délivreront au temps de la calamité; car, ô Juda! tu as eu autant de dieux que de villes.
Nanga ili kuti milungu yanu imene munadzipangira nokha? Ibweretu ngati ingathe kukupulumutsani pamene muli pamavuto! Inu anthu a ku Yuda, milungu yanu ndi yambiri kuchuluka kwake ngati mizinda yanu.
29 Pourquoi plaideriez-vous contre moi? vous avez tous péché contre moi, dit l'Eternel.
“Kodi mukundizengeranji mlandu? Nonse mwandiwukira,” akutero Yehova.
30 J'ai frappé en vain vos enfants, ils n'ont point reçu d'instruction; votre épée a dévoré vos Prophètes, comme un lion qui ravage [tout].
“Ine ndinalanga anthu ako popanda phindu; iwo sanaphunzirepo kanthu. Monga mkango wolusa, lupanga lanu lapha aneneri anu.
31 Ô race! considérez vous-mêmes la parole de l'Eternel, [qui dit]: Ai-je été un désert à Israël? ai-je été une terre toute ténébreuse? Pourquoi mon peuple a-t-il dit: nous sommes les maîtres; nous ne viendrons plus à toi?
“Inu anthu a mʼbado uno, ganizirani bwino mawu a Yehova: “Kodi Ine ndinakhalapo ngati chipululu kwa Israeli kapena ngati dziko la mdima wandiweyani? Chifukwa chiyani anthu anga akunena kuti, ‘Ife tili ndi ufulu omayendayenda; sitidzabweranso kwa Inu’?
32 La vierge oubliera-t-elle son ornement? l'épouse ses atours? mais mon peuple m'a oublié durant des jours sans nombre.
Kodi namwali amayiwala zokongoletsera zake, kapena kuyiwala zovala zake za ukwati? Komatu anthu anga andiyiwala masiku osawerengeka.
33 Pourquoi rends-tu ainsi affectée ta contenance pour chercher des amoureux, en sorte que tu as même enseigné tes manières de faire aux femmes de mauvaise vie?
Mumadziwa bwino njira zopezera zibwenzi! Choncho ngakhale akazi oyipa omwe mumawaphunzitsa njira zanu.
34 Même dans les pans de ta robe a été trouvé le sang des âmes des pauvres innocents, que tu n'avais point surpris en fracture, mais il y a été trouvé pour toutes ces choses-là.
Ngakhale pa zovala zako anthu amapezapo magazi a anthu osauka osalakwa. Anthuwo simunawapeze akuthyola nyumba. Komabe ngakhale zinthu zili chomwechi,
35 Et tu dis: je suis innocente; quoi qu'il en soit, sa colère s'est détournée de moi. Voici, je m'en vais contester contre toi, sur ce que tu as dit: je n'ai point péché.
inu mukunena kuti, ‘Ndife osalakwa, sadzatikwiyira.’ Ndidzakuyimbani mlandu chifukwa mukunena kuti, ‘Ife sitinachimwe.’
36 Pourquoi te donnes-tu tant de mouvement, changeant de chemin? tu seras aussi confuse d'Egypte, que tu as été confuse d'Assyrie.
Chifukwa chiyani mukunkabe nimusinthasintha njira zanu? Aigupto adzakukhumudwitsani monga momwe Asiriya anakuchititsani manyazi.
37 Tu sortiras même d'ici, ayant tes mains sur ta tête, parce que l'Eternel a rejeté les fondements de ta confiance, et tu n'auras aucune prospérité par eux.
Mudzachokanso kumeneko manja ali kunkhongo. Popeza Ine Yehova ndawakana anthu amene munkawadalira, choncho sadzakuthandizani konse.