< Isaïe 66 >
1 Ainsi a dit l'Eternel; les cieux sont mon trône, et la terre est le marchepied de mes pieds: quelle maison me bâtiriez-vous, et quel serait le lieu de mon repos?
Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
2 Car ma main a fait toutes ces choses, et c'est par moi que toutes ces choses ont eu leur être, dit l'Eternel. Mais à qui regarderai-je? à celui qui est affligé, et qui a l'esprit brisé, et qui tremble à ma parole.
Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
3 Celui qui égorge un bœuf, [c'est comme] qui tuerait un homme; celui qui sacrifie une brebis, c'est [comme] qui couperait le cou à un chien; celui qui offre un gâteau, [c'est comme qui offrirait] le sang d'un pourceau; celui qui fait un parfum d'encens, [c'est comme] qui bénirait une idole. Mais ils ont choisi leurs voies, et leur âme a pris plaisir en leurs abominations.
Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
4 Moi aussi je ferai attention à leurs tromperies, et je ferai venir sur eux les choses qu'ils craignent; parce que j'ai crié, et qu'il n'y a eu personne qui répondît: que j'ai parlé, et qu'ils n'ont point écouté; parce qu'ils ont fait ce qui me déplaît, et qu'ils ont choisi les choses auxquelles je ne prends point de plaisir.
Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
5 Ecoutez la parole de l'Eternel, vous qui tremblez à sa parole; vos frères qui vous haïssent, et qui vous rejettent comme une chose abominable, à cause de mon Nom, ont dit; que l'Eternel montre sa gloire. Il sera donc vu à votre joie, mais eux seront honteux.
Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
6 Un son éclatant vient de la ville, un son vient du Temple, le son de l'Eternel, rendant la pareille à ses ennemis.
Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
7 Elle a enfanté avant que de sentir le travail d'enfant; elle a été délivrée d'un enfant mâle, avant que les tranchées lui vinssent.
“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
8 Qui entendit jamais une telle chose, et qui en a jamais vu de semblables? Ferait-on qu'un pays fût enfanté en un jour? ou une nation naîtrait-elle tout d'un coup, que Sion ait enfanté ses fils aussitôt qu'elle a été en travail d'enfant?
Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
9 Moi qui fais enfanter les autres, ne ferais-je point enfanter [Sion]? a dit l'Eternel; Moi qui donne de la postérité aux autres, l'empêcherais-je [d'enfanter?] a dit ton Dieu.
Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 Réjouissez-vous avec Jérusalem, et vous égayez en elle, vous tous qui l'aimez; vous tous qui meniez deuil sur elle, réjouissez-vous avec elle l'une grande joie.
“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
11 Afin que vous soyez allaités, et que vous soyez rassasiés de la mamelle de ses consolations; afin que vous suciez [le lait], et que vous jouissiez à plaisir de toutes les sortes de sa gloire.
Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
12 Car ainsi a dit l'Eternel; voici, je m'en vais faire couler vers elle la paix comme un fleuve, et la gloire des nations comme un torrent débordé; et vous serez allaités, portés sur les côtés, et on vous fera jouer sur les genoux.
Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 Je vous caresserai pour vous apaiser, comme quand une mère caresse son enfant pour l'apaiser; car vous serez consolés en Jérusalem.
Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
14 Et vous le verrez, et votre cœur se réjouira, et vos os germeront comme l'herbe; et la main de l'Eternel sera connue envers ses serviteurs; mais il sera ému à indignation contre ses ennemis.
Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
15 Car voici, l'Eternel viendra avec le feu, et ses chariots seront comme la tempête, afin qu'il tourne sa colère en fureur, et sa menace en flamme de feu.
Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
16 Car l'Eternel exercera jugement contre toute chair par le feu, et avec son épée, et le nombre de ceux qui seront mis à mort par l'Eternel, sera grand.
Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
17 Ceux qui se sanctifient et se purifient au milieu des jardins, l'un après l'autre, qui mangent de la chair de pourceau, et des choses abominables, [comme] des souris, seront ensemble consumés, a dit l'Eternel.
Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
18 Mais pour moi, [voyant] leurs œuvres, et leurs pensées, [le temps] vient d'assembler toutes les nations et les langues; ils viendront, et verront ma gloire.
“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
19 Car je mettrai une marque en eux, et j'enverrai ceux d'entre eux qui seront réchappés, vers les nations, en Tarsis, en Pul, en Lud, gens tirant de l'arc, en Tubal, et en Javan, [et vers] les Iles éloignées qui n'ont point entendu ma renommée, et qui n'ont point vu ma gloire, et ils annonceront ma gloire parmi les nations.
“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
20 Et ils amèneront tous vos frères, d'entre toutes les nations, sur des chevaux, sur des chariots, et dans des litières, sur des mulets, et sur des dromadaires, pour offrande à l'Eternel, à la montagne de ma sainteté, à Jérusalem, a dit l'Eternel, comme lorsque les enfants d'Israël apportent l'offrande dans un vaisseau net, à la maison de l'Eternel.
Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
21 Et même j'en prendrai d'entre eux pour Sacrificateurs, [et] pour Lévites, a dit l'Eternel.
Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
22 Car comme les nouveaux cieux et la nouvelle terre que je m'en vais faire, seront établis devant moi, dit l'Eternel; ainsi sera établie votre postérité, et votre nom.
“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
23 Et il arrivera que depuis une nouvelle lune jusqu'à l'autre, et d'un Sabbat à l'autre, toute chair viendra se prosterner devant ma face, a dit l'Eternel.
“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
24 Et ils sortiront dehors, et verront les corps morts des hommes qui auront péché contre moi; car leur ver ne mourra point, et leur feu ne sera point éteint; et ils seront méprisés de tout le monde.
“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”