< Isaïe 60 >

1 Lève-toi, sois illuminée; car ta lumière est venue, et la gloire de l'Eternel s'est levée sur toi.
“Dzuka, wala, pakuti kuwala kwako kwafika, ndipo ulemerero wa Yehova wakuwalira.
2 Car voici, les ténèbres couvriront la terre, et l'obscurité couvrira les peuples; mais l'Eternel se lèvera sur toi, et sa gloire paraîtra sur toi.
Taona, mdima waphimba dziko lapansi ndipo mdima wandiweyani wagwa pa anthu a mitundu ina, koma Yehova adzakuwalira iwe, ndipo ulemerero wake udzaoneka pa iwe.
3 Et les nations marcheront à ta lumière, et les Rois à la splendeur qui se lèvera sur toi.
Mitundu ya anthu idzatsata kuwunika kwako ndipo mafumu adzalondola kunyezimira kwa mʼbandakucha wako.
4 Elève tes yeux à l'environ, et regarde; tous ceux-ci se sont assemblés, ils sont venus vers toi; tes fils viendront de loin, et tes filles seront nourries par des nourriciers, [étant portées] sur les côtés.
“Tukula maso ako, yangʼanayangʼana ndipo ona zimene zikuchitika. Onse akusonkhana ndipo akubwera kwa iwe; ana ako a amuna akubwera kuchokera kutali ndipo ana ako aakazi anyamulidwa mʼmanja.
5 Alors tu verras, et tu seras éclairée, et ton cœur s'étonnera, et s'épanouira [de joie], quand l'abondance de la mer se sera tournée vers toi, et que la puissance des nations sera venue chez toi.
Ukadzaona zimenezi udzasangalala kwambiri, mtima wako udzalumpha ndi kudzaza ndi chimwemwe; chuma chakunyanja chidzabwera kwa iwe chuma cha mitundu ya anthu chidzabwera kwa iwe.
6 Une abondance de chameaux te couvrira; les dromadaires de Madian et d'Hépha, et tous ceux de Séba viendront, ils apporteront de l'or et de l'encens, et publieront les louanges de l'Eternel.
Gulu la ngamira lidzaphimba dziko lako, ngamira zingʼonozingʼono zidzachokera ku Midiyani ndi ku Efai. Ndipo onse a ku Seba adzabwera atanyamula golide ndi lubani uku akutamanda Yehova.
7 Toutes les brebis de Kédar seront assemblées vers toi, les moutons de Nébajoth seront pour ton service; ils seront agréables étant offerts sur mon autel, et je rendrai magnifique la maison de ma gloire.
Ziweto zonse za ku Kedara adzazisonkhanitsa kwa inu, nkhosa zazimuna za ku Nabayoti zidzakutumikirani; zidzalandiridwa monga chopereka pa guwa langa la nsembe, ndipo ndidzakongoletsa Nyumba yanga.
8 Quelles sont ces volées, épaisses comme des nuées, qui volent comme des pigeons à leurs trous?
“Kodi ndi zayani izo zikuwuluka ngati mitambo, ngati kapena nkhunda zobwerera ku zisa zawo?
9 Car les Iles s'attendront à moi, et les navires de Tarsis les premiers, afin d'amener tes fils de loin, avec leur argent et leur or, pour l'amour du Nom de l'Eternel ton Dieu, et du Saint d'Israël, parce qu'il t'aura glorifiée.
Ndithu, izi ndi sitima za pa madzi zochokera ku mayiko akutali; patsogolo pali sitima zapamadzi za ku Tarisisi, zikubweretsa ana ako ochokera kutali, pamodzi ndi siliva wawo ndi golide wawo, kudzalemekeza Yehova Mulungu wako, Woyerayo wa Israeli, pakuti Iye wakuvekani inu ulemerero.
10 Et les fils des étrangers rebâtiront tes murailles, et leurs Rois seront employés à ton service; car je t'ai frappée en ma fureur, mais j'ai eu pitié de toi au temps de mon bon plaisir.
“Alendo adzamanganso malinga ako, ndipo mafumu awo adzakutumikira. Ngakhale ndinakukantha ndili wokwiya, koma tsopano ndidzakukomera mtima ndikukuchitira chifundo.
11 Tes portes aussi seront continuellement ouvertes, elles ne seront fermées ni nuit ni jour, afin que les forces des nations te soient amenées, et que leurs Rois y soient conduits.
Zipata zako zidzakhala zotsekula nthawi zonse, sadzazitseka nthawi zonse, usana ndi usiku, kotero anthu adzabwera kwa iwe ndi chuma chawo, akuyenda pa mdipiti mafumu awo ali patsogolo.
12 Car la nation et le Royaume qui ne te serviront point, périront; et ces nations-là seront réduites en une entière désolation.
Pakuti mtundu wa anthu ndi mafumu amene sakutumikira iwe; adzawonongeka kotheratu.
13 La gloire du Liban viendra vers toi, le sapin, l'orme, et le buis ensemble, pour rendre honorable le lieu de mon Sanctuaire; et je rendrai glorieux le lieu de mes pieds.
“Adzabwera nayo kwa iwe mitengo ya payini, mkuyu ndi naphini imene ili mʼnkhalango ya Lebanoni kuti adzakongoletsere malo a nyumba yanga yopatulika; ndipo ndidzalemekeza malo amene Ine ndimapondapo.
14 Même les enfants de ceux qui t'auront affligée viendront vers toi en se courbant; et tous ceux qui te méprisaient se prosterneront à tes pieds, et t'appelleront, La ville de l'Eternel, la Sion du Saint d'Israël.
Ana aja amene anakuzunzani adzabwera ndipo adzakugwadirani; onse amene anakunyozani adzagwada pansi pa mapazi anu. Ndipo adzakutchani kuti Mzinda wa Yehova; Ziyoni mzinda wa Woyerayo wa Israeli.
15 Au lieu que tu as été délaissée et haïe, tellement qu'il n'y avait personne qui passât [parmi toi], je te mettrai dans une élévation éternelle, [et] dans une joie qui sera de génération en génération.
“Ngakhale anthu anakusiya nadana nawe, koma Ine ndidzakukuza mpaka muyaya, ndipo udzakhala malo a chimwemwe cha anthu amibado yonse.
16 Et tu suceras le lait des nations, et tu suceras la mamelle des Rois, et tu sauras que je suis l'Eternel ton Sauveur, et ton Rédempteur, le Puissant de Jacob.
Udzamwa mkaka wa mitundu ya anthu ndi kuleredwa pa maere aufumu, motero udzadziwa kuti Ine Yehova, ndine Mpulumutsi wako, Momboli wako ndiye Wamphamvu wa Yakobo.
17 Je ferai venir de l'or au lieu de l'airain, et je ferai venir de l'argent au lieu du fer, et de l'airain au lieu du bois, et du fer au lieu des pierres; et je ferai que la paix te gouvernera, et que tes exacteurs ne seront que justice.
Ndidzakupatsa golide mʼmalo mwa mkuwa, ndi siliva mʼmalo mwa chitsulo. Ndidzakupatsa mkuwa mʼmalo mwa thabwa ndi chitsulo mʼmalo mwa miyala. Olamulira ako adzakhala a mtendere. Ndidzasandutsa okulamulira kuti akhale achilungamo.
18 On n'entendra plus parler de violence en ton pays, ni de dégât, ni de calamité en tes contrées, mais tu appelleras tes murailles, Salut, et tes portes, Louange.
Ziwawa sizidzamvekanso mʼdziko lako, bwinja kapena chiwonongeko sizidzapezeka mʼdziko lako, ndidzakhala malinga ako okuteteza ndipo udzanditamanda.
19 Tu n'auras plus le soleil pour la lumière du jour, et la lueur de la lune ne t'éclairera plus; mais l'Eternel te sera pour lumière éternelle, et ton Dieu pour ta gloire.
Sipadzakhala dzuwa kuti likuwunikire, kapena mwezi kuti uwunikire usiku, pakuti Yehova ndiye adzakhale kuwunika kwako kwa muyaya, ndipo Mulungu wako adzakhala ulemerero wako.
20 Ton soleil ne se couchera plus, et ta lune ne se retirera plus, car l'Eternel te sera pour lumière perpétuelle, et les jours de ton deuil seront finis.
Dzuwa lako silidzalowanso, ndipo mwezi wako sudzazimiriranso; Yehova adzakhala kuwunika kwako kwamuyaya, ndipo masiku a mavuto ako adzatha.
21 Et quant à ton peuple, ils seront tous justes; ils posséderont éternellement la terre; [savoir] le germe de mes plantes, l'œuvre de mes mains, pour y être glorifié.
Ndipo anthu ako onse adzakhala olungama ndipo dzikolo lidzakhala lawo mpaka muyaya. Iwo ndi mphukira imene Ine ndayidzala, ntchito ya manja anga, kuti aonetse ulemerero wanga.
22 La petite [famille] croîtra jusqu'à mille [personnes], et la moindre deviendra une nation forte. Je suis l'Eternel, je hâterai ceci en son temps.
Kabanja kakangʼono kadzasanduka fuko, kafuko kakangʼono kudzasanduka mtundu wamphamvu. Ine ndine Yehova, nthawi yake ikafika ndidzazichita zimenezi mofulumira.”

< Isaïe 60 >