< Isaïe 59 >
1 Voici, la main de l'Eternel n'est pas raccourcie pour ne pouvoir pas délivrer, et son oreille n'est pas devenue pesante, pour ne pouvoir pas ouïr.
Taonani, mkono wa Yehova si waufupi kuti sungathe kupulumutsa, kapena khutu lake kuti ndilogontha kuti sangamve.
2 Mais ce sont vos iniquités qui ont fait séparation entre vous et votre Dieu; et vos péchés ont fait qu'il a caché [sa] face de vous, afin qu'il ne vous entende point.
Koma zoyipa zanu zakulekanitsani ndi Mulungu wanu; ndipo wakufulatirani chifukwa cha machimo anu, kotero Iye sadzamva.
3 Car vos mains sont souillées de sang, et vos doigts d'iniquité; vos lèvres ont proféré le mensonge, [et] votre langue a prononcé la perversité.
Pakuti manja anu ali psuu ndi magazi. Munayipitsa zala zanu ndi zamphulupulu. Pakamwa panu payankhula zabodza, ndipo lilime lanu lanena zinthu zoyipa.
4 Il n'y a personne qui crie pour la justice, et il n'y a personne qui plaide pour la vérité; on se fie en des choses de néant, et on parle vanité; on conçoit le travail, et on enfante le tourment.
Palibe amene akuyimba mnzake mlandu molungama, palibe amene akupita ku mlandu moona mtima. Iwo amadalira mawu opanda pake ndipo amayankhula mabodza; amalingalira za mphulupulu ndipo amachita zoyipa.
5 Ils ont éclos des œufs de basilic, et ils ont tissu des toiles d'araignée; celui qui aura mangé de leurs œufs en mourra; et si on les écrase, il en sortira une vipère.
Iwo amayikira mazira a mamba ndipo amaluka ukonde wakangawude. Aliyense amene adzadya mazira awo adzafa, ndipo ngati dzira limodzi lasweka limatulutsa mphiri.
6 Leurs toiles ne serviront point à faire des vêtements, et on ne se couvrira point de leurs ouvrages; car leurs ouvrages sont des ouvrages de tourment, et il y a en leurs mains des actions de violence.
Ukonde wawo wa kangawude sangawuvale ngati chovala; ndipo chimene apangacho sangachifunde. Ntchito zawo ndi zoyipa, ndipo amakonda kuchita zandewu ndi manja awo.
7 Leurs pieds courent au mal, et se hâtent pour répandre le sang innocent; leurs pensées sont des pensées de tourment; le dégât et la calamité est dans leurs voies.
Amathamangira kukachita zoyipa; sachedwa kupha anthu osalakwa. Maganizo awo ndi maganizo oyipa; kulikonse kumene amapita amasiyako bwinja ndi chiwonongeko.
8 Ils ne connaissent point le chemin de la paix, et il n'y a point de jugement dans leurs ornières, ils se sont pervertis dans leurs sentiers, tous ceux qui y marchent ignorent la paix.
Iwo sadziwa kuchita za mtendere; zonse zimene amachita nʼzopanda chilungamo. Njira zawo zonse nʼzokhotakhota; aliyense oyenda mʼnjira zimenezo sadzapeza mtendere.
9 C'est pourquoi le jugement s'est éloigné de nous, et la justice ne vient point jusques à nous; nous attendions la lumière, et voici les ténèbres; la splendeur, [et] nous marchons dans l'obscurité.
Anthu akuti, “Chifukwa cha zimenezi chilungamo chatitalikira; ndipo chipulumutso sichitifikira. Timafunafuna kuwala koma timangopeza mdima okhaokha; tinayembekezera kuyera koma timayenda mu mdima wandiweyani.
10 Nous avons tâtonné après la paroi comme des aveugles; nous avons, dis-je, tâtonné comme ceux qui sont sans yeux; nous avons bronché en plein midi comme sur la brune, [et nous avons été] dans les lieux abondants comme [y seraient] des morts.
Timapapasapapasa khoma ngati munthu wosaona, kuyangʼanayangʼana njira ngati anthu opanda maso. Timapunthwa dzuwa lili paliwombo ngati kuti ndi usiku; timakhala pansi mu mdima ngati anthu akufa.
11 Nous rugissons tous comme des ours, et nous ne cessons de gémir comme des colombes; nous attendions le jugement, et il n'y en a point; la délivrance, et elle s'est éloignée de nous.
Tonse timabangula ngati zimbalangondo: Timalira modandaula ngati nkhunda. Tinayembekezera kuweruza kolungama; koma sitikupeza. Timayembekezera chipulumutso koma chimakhala nafe kutali.”
12 Car nos forfaits se sont multipliés devant toi, et chacun de nos péchés a témoigné contre nous; parce que nos forfaits sont avec nous, et nous connaissons nos iniquités;
Pakuti zolakwa zathu nʼzochuluka pamaso panu, ndipo machimo athu akutsutsana nafe. Zolakwa zathu zili ndi ife nthawi zonse ndipo tikuvomereza machimo athu:
13 Qui sont de pécher et de mentir contre l'Eternel, de s'éloigner de notre Dieu, de proférer l'oppression et la révolte; de concevoir et prononcer du cœur des paroles de mensonge.
Tawukira ndi kumukana Yehova. Tafulatira Mulungu wathu, pa kupondereza anzathu ndi kupandukira Yehova, ndi pa kuyankhula mabodza amene tawaganiza mʼmitima mwathu.
14 C'est pourquoi le jugement s'est éloigné et la justice s'est tenue loin; car la vérité est tombée par les rues, et la droiture n'y a pu entrer.
Motero kuweruza kolungama kwalekeka ndipo choonadi chili kutali ndi ife; kukhulupirika sikukupezekanso mʼmabwalo a milandu, ndipo kuona mtima sikukupezekanso mʼmenemo.
15 Même la vérité a disparu, et quiconque se retire du mal est exposé au pillage; l'Eternel l'a vu, et cela lui a déplu, parce qu'il n'y a point de droiture.
Choonadi sichikupezeka kumeneko, ndipo wina akakana kuchita nawo zoyipa amapeza mavuto. Yehova anaziona zimenezi ndipo zinamunyansa kuti panalibe chiweruzo cholungama.
16 Il a vu aussi qu'il n'[y avait] point d'homme [qui soutînt l'innocence] et il s'est étonné que personne ne se mettait à la brèche; c'est pourquoi son bras l'a délivré, et sa propre justice l'a soutenu.
Yehova anaona kuti panalibe ndi mmodzi yemwe, Iye anadabwa kuti panalibe ndi mmodzi yemwe woti nʼkupembedzera; Choncho mphamvu zake zomwe zinamuthandiza, ndipo anadzilimbitsa ndi kulungama kwake;
17 Car il s'est revêtu de la justice comme d'une cuirasse, et le casque du salut a été sur sa tête; il s'est revêtu des habits de la vengeance [comme] d'un vêtement, et s'est couvert de jalousie comme d'un manteau.
Iye anavala chilungamo ngati chovala chachitsulo chapachifuwa, ndipo kumutu kwake amavala chipewa chachipulumutso; anavala kulipsira ngati chovala ndipo anadzikuta ndi mkwiyo ngati chofunda.
18 Comme pour les rétributions, et comme quand quelqu'un veut rendre la pareille, [savoir] la fureur à ses adversaires, et la rétribution à ses ennemis; il rendra ainsi la rétribution aux Iles.
Iye adzawabwezera chilango adani a anthu ake molingana ndi zimene anachita, adzaonetsa ukali kwa adani ake ndi kubwezera chilango odana naye. Adzalanga ngakhale okhala mayiko akutali.
19 Et on craindra le Nom de l'Eternel depuis l'Occident; et sa gloire depuis le Soleil levant; car l'ennemi viendra comme un fleuve, [mais] l'Esprit de l'Eternel lèvera l'enseigne contre lui.
Choncho akadzabwera ngati madzi oyendetsedwa ndi mphepo yamphamvu yamkuntho. Anthu onse kuyambira kumadzulo mpaka kummawa adzaopa dzina la Yehova ndi ulemerero wake.
20 Et le Rédempteur viendra en Sion, et vers ceux de Jacob qui se convertissent de leur péché, dit l'Eternel.
“Mpulumutsi adzabwera ku Ziyoni kudzapulumutsa anthu a fuko la Yakobo amene analapa machimo awo,” akutero Yehova.
21 Et quant à moi; c'est ici mon alliance que je ferai avec eux, a dit l'Eternel; mon Esprit qui est sur toi, et mes paroles que j'ai mises en ta bouche, ne bougeront point de ta bouche, ni de la bouche de ta postérité, ni de la bouche de la postérité de ta postérité, a dit l'Eternel, dès maintenant et à jamais.
Yehova akuti, “Kunena za pangano lake ndi iwo, Mzimu wanga umene uli pa inu, ndiponso mawu anga amene ndayika mʼkamwa mwanu sadzachoka mʼkamwa mwanu, kapena kuchoka mʼkamwa mwa ana anu, kapena mʼkamwa mwa zidzukulu zawo kuyambira tsopano mpaka kalekale,” akutero Yehova.