< Isaïe 44 >
1 Mais maintenant, ô Jacob! mon serviteur, écoute; et toi Israël que j'ai élu.
Yehova akuti, “Mvera tsopano, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Israeli, amene ndinakusankha.
2 Ainsi a dit l'Eternel, qui t'a fait et formé dès le ventre, [et qui] t'aide; ne crains point, ô Jacob mon serviteur! et toi Jésurun que j'ai élu.
Yehova amene anakupanga iwe, anakuwumba iwe mʼmimba ya amayi ako, ndi amene adzakuthandiza iwe. Iye akuti, Usachite mantha, iwe Yakobo, mtumiki wanga, Yesuruni, amene ndinakusankha.
3 Car je répandrai des eaux sur celui qui est altéré, et des rivières sur la [terre] sèche; je répandrai mon esprit sur ta postérité, et ma bénédiction sur ceux qui sortiront de toi.
Pakuti ndidzathira madzi pa nthaka yowuma, ndi kuyendetsa mitsinje mʼdziko lowuma; ndidzatumiza Mzimu wanga pa ana anu, ndi kutsitsa madalitso anga pa zidzukulu zanu.
4 Et ils germeront [comme] parmi l'herbage, comme les saules auprès des eaux courantes.
Iwo adzakula ngati udzu wothirira bwino ndi ngati bango lomera mʼmbali mwa mitsinje ya madzi oyenda.
5 L'un dira; je suis à l'Eternel, et l'autre se réclamera du nom de Jacob; et un autre écrira de sa main; je suis à l'Eternel; et se surnommera du Nom d'Israël.
Wina adzanena kuti, ‘Ine ndine wa Yehova;’ wina adzadzitcha yekha wa banja la Yakobo; winanso adzalemba pa dzanja lake, ‘Wa Yehova’ ndipo adzadzitcha wa banja la Israeli.
6 Ainsi a dit l'Eternel, le Roi d'Israël et son Rédempteur, l'Eternel des armées; je suis le premier, et je suis le dernier; et il n'y a point d'autre Dieu que moi.
“Yehova Mfumu ndi Mpulumutsi wa Israeli, Yehova Wamphamvuzonse akuti: Ine ndine woyamba ndi wotsiriza; palibenso Mulungu wina koma Ine ndekha.
7 Et qui est celui qui ait appelé comme moi, qui m'ait déclaré, et ordonné cela, depuis que j'ai établi le peuple ancien? qu'ils leur déclarent les choses à venir, les choses, [dis-je], qui arriveront ci-après.
Ndani nanga angafanane ndi Ine? Muloleni kuti ayankhule. Muloleni andifotokozere ndi kundiyalira bwino lomwe zimene zinachitika kuyambira pamene ndinkakhazikitsa anthu anga akalekale, ndi ziti zimene zidzachitike; inde, muloleni alosere zimene zikubwera.
8 Ne soyez point effrayés, et ne soyez point troublés; ne te l'ai-je pas fait entendre et déclaré dès ce temps-là? et vous m'en êtes témoins; y-a-t-il quelque autre Dieu que moi? certes il n'y a point d'autre Rocher; je n'en connais point.
Musanjenjemere, musachite mantha. Kodi sindinakuwuzeni zimenezi ndi kuzilosera kalekale lomwe? Inu ndinu mboni zanga. Kodi aliponso Mulungu wina kupatula Ine? Ayi, palibe Thanthwe linanso limene sindikulidziwa.”
9 Les ouvriers des images taillées ne sont tous qu'un rien, et leurs choses les plus précieux ne profitent de rien; et ils leur sont témoins qu'ils ne voient point, et ne connaissent point, afin qu'ils soient honteux.
Onse amene amapanga mafano ngachabe, ndipo milungu imene amayilemekeza ndi yopanda phindu. Iwo amene amapembedza mafano ndi wosaona; ndipo sazindikira kanthu. Choncho adzawachititsa manyazi.
10 [Mais] qui est-ce qui a formé un [Dieu] Fort, et qui a fondu une image taillée, pour n'en avoir aucun profit?
Ndani amasema mulungu ndi kuwumba fano, limene silingamupindulire?
11 Voici, tous ses compagnons seront honteux, car ces ouvriers-là sont d'entre les hommes; ils seront effrayés et rendus honteux tous ensemble.
Iye pamodzi ndi anzake onse adzawachititsa manyazi; amisiri a mafano ndi anthu chabe. Aloleni onse asonkhane ndi kuyima pabwalo la milandu; onse adzaopsedwa ndipo adzachita manyazi.
12 Le forgeron de fer [prend] le ciseau et travaille avec le charbon, il le forme avec des marteaux, il le fait à force de bras, même ayant faim, tellement qu'il n'en peut plus; et s'il ne boit point d'eau, il en est tout fatigué.
Mmisiri wa zitsulo amatenga chitsulo ndipo amachiyika pa makala amoto; ndi dzanja lake lamphamvu amachisula pochimenya ndi nyundo. Pambuyo pake mʼmisiri uja amamva njala natha mphamvu; iye samwa madzi, ndipo amalefuka.
13 Le menuisier étend sa règle, et le crayonne avec de la craie; il le fait avec des équerres, et le forme au compas, et le fait à la ressemblance d'un homme, et le pare comme un homme, afin qu'il demeure dans la maison.
Mmisiri wa matabwa nayenso amayeza mtengo ndi chingwe ndipo amajambula chithunzi ndi cholembera; amasema bwinobwino ndi chipangizo chake ndipo amachiwongola bwino ndi chida chake. Amachipanga ngati munthu, munthu wake wokongola kuti aliyike mʼnyumba yake yachipembedzo.
14 Il se coupe des cèdres, et prend un cyprès, ou un chêne, qu'il a laissé croître parmi les arbres de la forêt; il plante un frêne, et la pluie le fait croître.
Amagwetsa mitengo ya mkungudza, mwinanso amatenga mtengo wa payini kapena wa thundu nʼkudzisankhira mtengo wabwino pakati pa mitengo ya mʼnkhalango, ndipo amadzala mtengo wa payini ndi kuwuleka kuti ukule ndi mvula.
15 Puis il servira à l'homme pour brûler; car il en prend, et s'en chauffe; il en fait, dis-je, du feu, et en cuit du pain; il en fait aussi un Dieu, et se prosterne [devant lui]; il en fait une image taillée, et l'adore.
Mitengoyo munthu amachitako nkhuni; nthambi zina amasonkhera moto wowotha, amakolezera moto wophikira buledi ndi mbali ina ya mtengowo amapangira mulungu ndipo amapembedza; iye amapanga fano ndi kumaligwadira.
16 Il en brûle au feu une partie, et d'une autre partie il mange sa chair, laquelle il rôtit, et s'en rassasie; il s'en chauffe aussi, et il dit; ha! ha! je me suis réchauffé, j'ai vu la lueur [du feu].
Chigawo china cha mtengowo amasonkhera moto wowotcherapo nyama imene amadya, nakhuta. Iye amawotha motowo ndipo amanena kuti, “Aa! Ndikumva kutentha; pano pali moto.”
17 Puis du reste il en fait un Dieu pour être son image taillée; il l'adore et se prosterne devant lui, et lui fait sa requête, [et lui dit]; Délivre-moi, car tu es mon Dieu.
Chigawo chotsala amapanga kamulungu, fano lake limenelo; amaligwadira ndi kulipembedza. Amapemphera kwa fanolo ndipo amanena kuti, “Iwe ndiwe mulungu wanga, ndipulumutse.”
18 [Ces gens] ne savent et n'entendent rien; car on leur a plâtré les yeux, afin qu'ils ne voient point; et leurs cœurs, afin qu'ils n'entendent point.
Anthu otere sadziwa kanthu, samvetsa kanthu kalikonse; maso awo ndi omatirira ndipo sangathe kuona, ndipo mitu yawo ndi yogontha kotero sangathe kumvetsa.
19 Nul ne rentre en soi-même, et n'a ni connaissance, ni intelligence, pour dire; j'ai brûlé la moitié de ceci au feu, et même j'en ai cuit du pain sur les charbons; j'en ai rôti de la chair, et j'en ai mangé; et du reste en ferais-je une abomination? adorerais-je une branche de bois?
Palibe amene amayima nʼkulingalira. Palibe wanzeru kapena womvetsa zinthu bwino woti nʼkunena kuti, chigawo china cha mtengowo ndinasonkhera moto; pa makala ake ndinaphikira buledi, ndinawotchapo nyama ndipo ndinadya. Chigawo chotsalachi ndipangire chinthu chonyansachi. Kodi ndidzagwadira mtengo?
20 Il se paît de cendre, et son cœur abusé le fait égarer; et il ne délivrera point son âme, et ne dira point; [ce qui] est dans ma main droite n'est-il pas une fausseté?
Munthu wotere ali ngati wodya phulusa, maganizo ake opusa amusocheretsa; motero kuti sangathe kudzipulumutsa yekha kapena kudzifunsa kuti, “Kodi chinthu chili mʼmanja mwangachi si chabodza?”
21 Jacob et Israël, souviens-toi de ces choses, car tu es mon serviteur; je t'ai formé, tu es mon serviteur, ô Israël! je ne te mettrai point en oubli.
Yehova akuti, “Iwe Yakobo, kumbukira zinthu izi popeza kuti ndiwe mtumiki wanga, iwe Israeli. Ine ndinakupanga iwe, ndiwe mtumiki wanga; iwe Israeli, sindidzakuyiwala.
22 J'ai effacé tes forfaits comme une nuée épaisse, et tes péchés, comme une nuée; retourne à moi, car je t'ai racheté.
Ndachotsa zolakwa zako ngati mitambo, ndi machimo ako ngati nkhungu ya mmawa. Bwerera kwa Ine, popeza ndakupulumutsa.”
23 O cieux! réjouissez-vous avec chant de triomphe, car l'Eternel a opéré; lieux bas de la terre, jetez des cris de réjouissance; montagnes, éclatez de joie avec chant de triomphe; [et vous aussi] forêts, et tous les arbres qui êtes en elles, parce que l'Eternel a racheté Jacob, et s'est manifesté glorieusement en Israël.
Imbani mwachimwemwe, inu zolengedwa zamlengalenga, pakuti Yehova wachita zimenezi; fuwula, iwe dziko lapansi. Imbani nyimbo, inu mapiri, inu nkhalango ndi mitengo yonse, chifukwa Yehova wawombola Yakobo, waonetsa ulemerero wake mwa Israeli.
24 Ainsi a dit l'Eternel ton Rédempteur, et celui gui t'a formé dès le ventre; je suis l'Eternel qui ai fait toutes choses, qui [seul] ai étendu les cieux, et qui ai par moi-même aplani la terre;
Yehova Mpulumutsi wanu, amene anakuwumbani mʼmimba ya amayi anu akuti: “Ine ndine Yehova, amene anapanga zinthu zonse, ndinatambasula ndekha zinthu zakuthambo, ndinayala ndekha dziko lapansi.
25 Qui dissipe les signes des menteurs, qui rends insensés les devins; qui renverse l'esprit des sages, et qui fais que leur science devient une folie.
Ndine amene ndinalepheretsa mipingo ya anthu onyenga, ndipo ndimapusitsa owombeza mawula. Ndimasokoneza anthu a nzeru, ndi kuonetsa kuti nzeru zawo nʼzopusa.
26 C'est lui qui met en exécution la parole de son serviteur, et qui accomplit le conseil de ses messagers; qui dit à Jérusalem; tu seras [encore] habitée; et aux villes de Juda; vous serez rebâties; et je redresserai ses lieux déserts.
Ndine amene ndimatsimikiza mawu a atumiki ake ndi kukwaniritsa zimene analosera amithenga ake. “Ndine amene ndinanena za Yerusalemu kuti mudzakhalanso anthu. Ndinanenanso za mizinda ya Yuda kuti idzamangidwanso. Za mabwinja awo ndinanena kuti ndidzawawutsanso.
27 Qui dit au gouffre; sois asséché, et je tarirai tes fleuves.
Ndine amene ndinawuza nyanga yayikulu kuti, ‘Uma’ ndipo ndidzawumitsa mitsinje yako.
28 Qui dit de Cyrus; c'est mon Berger; il accomplira tout mon bon plaisir, disant même à Jérusalem; tu seras rebâtie; et au Temple; tu seras fondé.
Ndine amene ndinanena kwa Koresi kuti, ‘Iye ndiye mʼbusa wanga,’ ndipo adzachita zonse zimene ndikufuna; iye adzalamula kuti, ‘Yerusalemu amangidwenso’ ndi kuti, ‘Maziko a Nyumba ya Mulungu ayikidwenso.’”