< Isaïe 38 >

1 En ces jours-là Ezéchias fut malade à la mort, et Esaïe le Prophète fils d'Amots vint vers lui, et lui dit; ainsi a dit l'Eternel; dispose de ta maison, car tu t'en vas mourir, et tu ne vivras plus.
Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”
2 Alors Ezéchias tourna sa face contre la muraille, et fit sa prière à l'Eternel.
Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti,
3 Et dit; souviens-toi maintenant je te prie, ô Eternel! comment j'ai marché devant toi en vérité et en intégrité de cœur, et comment j'ai fait ce qui t'était agréable; et Ezéchias pleura abondamment.
“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.
4 Or la parole de l'Eternel fut adressée à Esaïe, en disant;
Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti:
5 Va, et dis à Ezéchias ainsi a dit l'Eternel, le Dieu de David ton père; j'ai exaucé ta prière, j'ai vu tes larmes; voici, je m'en vais ajouter quinze années à tes jours.
“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako.
6 Et je te délivrerai de la main du Roi des Assyriens, toi et cette ville, et je garantirai cette ville.
Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
7 Et ce signe t'est donné par l'Eternel, [pour faire voir] que l'Eternel accomplira cette parole qu'il a prononcée;
“‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza:
8 Voici, je m'en vais faire retourner l'ombre des degrés par lesquels elle est descendue au cadran d'Achaz, de dix degrés en arrière avec le soleil; et le soleil retourna de dix degrés par les degrés par lesquels il était descendu.
Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
9 Or c'est ici l'Ecrit d'Ezéchias Roi de Juda, touchant ce qu'il fut malade, et qu'il fut guéri de sa maladie.
Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
10 J'avais dit dans le retranchement de mes jours; je m'en irai aux portes du sépulcre, je suis privé de ce qui restait de mes années. (Sheol h7585)
Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol h7585)
11 J'avais dit; je ne contemplerai plus l'Eternel, l'Eternel, dans la terre des vivants; je ne verrai plus personne avec les habitants du monde.
Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova, mʼdziko la anthu amoyo, sindidzaonanso mtundu wa anthu kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
12 Ma durée s'en est allée, et a été transportée d'avec moi, comme une cabane de berger; j'ai tranché ma vie comme le tisserand [coupe sa toile]; il me coupera dès les pesnes: du matin au soir tu m'auras enlevé.
Nyumba yanga yasasuka ndipo yachotsedwa. Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga, ngati munthu wowomba nsalu; kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
13 Je me proposais jusqu'au matin qu'il était comme un lion, qu'il briserait ainsi tous mes os; du matin au soir tu m'auras enlevé.
Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa; koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango, ndipo mwakhala mukundisiya.
14 Je grommelais comme la grue, et [comme] l'hirondelle; je gémissais comme le pigeon; mes yeux défaillaient à force de regarder en haut; Seigneur, on me fait force, sois mon garant.
Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
15 Que dirai-je? il m'a parlé; et lui même l'a fait; je m'en irai tout doucement, tous les ans de ma vie, dans l'amertume de mon âme.
Koma ine ndinganene chiyani? Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi. Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga, ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
16 Seigneur, par ces choses-là on a la vie, et dans tout [ce qui est] en ces choses consiste la vie de mon esprit; ainsi tu me rétabliras, et me feras revivre.
Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu. Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu. Munandichiritsa ndi kundikhalitsa ndi moyo.
17 Voici, dans ma paix une grande amertume m'était survenue, mais tu as embrassé ma personne, afin qu'elle ne tombât point dans la fosse de la pourriture; parce que tu as jeté tous mes péchés derrière ton dos.
Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere kuti ndikhale ndi moyo; Inu munandisunga kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko chifukwa mwakhululukira machimo anga onse.
18 Car le sépulcre ne te célébrera point, la mort ne te louera point; ceux qui descendent en la fosse, ne s'attendent plus à ta vérité. (Sheol h7585)
Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol h7585)
19 Mais le vivant, le vivant, est celui qui te célébrera, comme moi aujourd'hui; le père conduira les enfants à la connaissance de ta vérité.
Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani, monga mmene ndikuchitira ine lero lino; abambo amawuza ana awo za kukhulupirika kwanu.
20 L'Eternel m'est venu délivrer, et à cause de cela nous jouerons sur les instruments mes cantiques tous les jours de notre vie, dans la maison de l'Eternel.
Yehova watipulumutsa. Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe masiku onse a moyo wathu mʼNyumba ya Yehova.
21 Or Esaïe avait dit; qu'on prenne une masse de figues sèches, et qu'on en fasse une emplâtre sur l'ulcère, et il guérira.
Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”
22 Et Ezéchias avait dit; quel est le signe que je monterai en la maison de l'Eternel?
Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”

< Isaïe 38 >